< Romans 1 >

1 Paul, a servant of Jesus Christ, called as an Apostle, separated for the Gospel of God,
Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu
2 which he had promised beforehand, through his Prophets, in the Holy Scriptures,
umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake.
3 about his Son, who was made for him from the offspring of David according to the flesh,
Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide.
4 the Son of God, who was predestined in virtue according to the Spirit of sanctification from the resurrection of the dead, our Lord Jesus Christ,
Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu,
5 through whom we have received grace and Apostleship, for the sake of his name, for the obedience of faith among all the Gentiles,
ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe.
6 from whom you also have been called by Jesus Christ:
Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
7 To all who are at Rome, the beloved of God, called as saints. Grace to you, and peace, from God our Father and from the Lord Jesus Christ.
Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima. Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
8 Certainly, I give thanks to my God, through Jesus Christ, first for all of you, because your faith is being announced throughout the entire world.
Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu.
9 For God is my witness, whom I serve in my spirit by the Gospel of his Son, that without ceasing I have kept a remembrance of you
Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse.
10 always in my prayers, pleading that in some way, at some time, I may have a prosperous journey, within the will of God, to come to you.
Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
11 For I long to see you, so that I may impart to you a certain spiritual grace to strengthen you,
Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni
12 specifically, to be consoled together with you through that which is mutual: your faith and mine.
ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake.
13 But I want you to know, brothers, that I have often intended to come to you, (though I have been hindered even to the present time) so that I might obtain some fruit among you also, just as also among the other Gentiles.
Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
14 To the Greeks and to the uncivilized, to the wise and to the foolish, I am in debt.
Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe.
15 So within me there is a prompting to evangelize to you also who are at Rome.
Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
16 For I am not ashamed of the Gospel. For it is the power of God unto salvation for all believers, the Jew first, and the Greek.
Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene.
17 For the justice of God is revealed within it, by faith unto faith, just as it was written: “For the just one lives by faith.”
Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
18 For the wrath of God is revealed from heaven over every impiety and injustice among those men who fend off the truth of God with injustice.
Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa.
19 For what is known about God is manifest in them. For God has manifested it to them.
Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo.
20 For unseen things about him have been made conspicuous, since the creation of the world, being understood by the things that were made; likewise his everlasting virtue and divinity, so much so that they have no excuse. (aïdios g126)
Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios g126)
21 For although they had known God, they did not glorify God, nor give thanks. Instead, they became weakened in their thoughts, and their foolish heart was obscured.
Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima.
22 For, while proclaiming themselves to be wise, they became foolish.
Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa.
23 And they exchanged the glory of the incorruptible God for the likeness of an image of corruptible man, and of flying things, and of four-legged beasts, and of serpents.
Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
24 For this reason, God handed them over to the desires of their own heart for impurity, so that they afflicted their own bodies with indignities among themselves.
Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo.
25 And they exchanged the truth of God for a lie. And they worshipped and served the creature, rather than the Creator, who is blessed for all eternity. Amen. (aiōn g165)
Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
26 Because of this, God handed them over to shameful passions. For example, their females have exchanged the natural use of the body for a use which is against nature.
Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo.
27 And similarly, the males also, abandoning the natural use of females, have burned in their desires for one another: males doing with males what is disgraceful, and receiving within themselves the recompense that necessarily results from their error.
Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
28 And since they did not prove to have God by knowledge, God handed them over to a morally depraved way of thinking, so that they might do those things which are not fitting:
Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo.
29 having been completely filled with all iniquity, malice, fornication, avarice, wickedness; full of envy, murder, contention, deceit, spite, gossiping;
Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche,
30 slanderous, hateful toward God, abusive, arrogant, self-exalting, devisers of evil, disobedient to parents,
osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo,
31 foolish, disorderly; without affection, without fidelity, without mercy.
alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza.
32 And these, though they had known the justice of God, did not understand that those who act in such a manner are deserving of death, and not only those who do these things, but also those who consent to what is done.
Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.

< Romans 1 >