< 2 Samuel 4 >

1 Then Ishbosheth, the son of Saul, heard that Abner had fallen in Hebron. And his hands were weakened, and all of Israel was troubled.
Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
2 Now the son of Saul had two men, leaders among robbers. The name of the one was Baanah, and the name of the other was Rechab, sons of Rimmon, a Beerothite from the sons of Benjamin. For indeed, Beeroth, too, was reputed with Benjamin.
Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
3 And the Beerothites had fled into Gittaim. And they were strangers there, until that time.
chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
4 Now Jonathan, the son of Saul, had a son with disabled feet. For he was five years old when the report about Saul and Jonathan arrived from Jezreel. And so, his nurse, taking him up, fled. And while she was hurrying, so that she might flee, he fell and was made lame. And he was called Mephibosheth.
(Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
5 And so, the sons of Rimmon the Beerothite, Rechab and Baanah, arrived and entered the house of Ishbosheth, in the heat of the day. And he was sleeping on his bed at midday. And the doorkeeper of the house, who was cleaning the wheat, fell fast asleep.
Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
6 Then they entered the house secretly, taking the ears of grain. And Rechab and his brother Baanah stabbed him in the groin, and they fled away.
Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
7 For when they had entered the house, he was sleeping on his bed in a closed room. And striking him, they killed him. And taking his head, they departed by the way of the desert, walking throughout the night.
Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
8 And they brought the head of Ishbosheth to David in Hebron. And they said to the king: “Behold, the head of Ishbosheth, the son of Saul, your enemy, who was seeking your life. And so, the Lord has avenged my lord the king, this day, from Saul and from his offspring.”
Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
9 But David, responding to Rechab and his brother Baanah, the sons of Rimmon the Beerothite, said to them: “As the Lord lives who has rescued my soul from all distress,
Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
10 the one who reported to me and said, ‘Saul is dead,’ who was thinking that he announced good news, I apprehended. And at Ziklag I killed him who ought to have been given a reward for the news.
pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
11 How much more so now, when impious men have put to death an innocent man in his own house, upon his bed, shall I not require his blood from your hand, and take you away from the earth?”
Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
12 And so, David commanded his servants, and they put them to death. And cutting off their hands and feet, they suspended them up over the pool in Hebron. But the head of Ishbosheth they took and buried in the sepulcher of Abner at Hebron.
Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.

< 2 Samuel 4 >