< 2 Samuel 23 >

1 These are the last words of David. Now David, the son of Jesse, the man to whom it was appointed concerning the Christ of the God of Jacob, the preeminent psalmist of Israel said:
Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
2 “The Spirit of the Lord has spoken through me, and his word was spoken through my tongue.
“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
3 The God of Israel spoke to me, the Strong One of Israel spoke, the Ruler of men, the Just Ruler, in the fear of God,
Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
4 like the first light of the morning as the sun is rising, when a morning without clouds glows red, and like plants springing forth from the earth after a rainfall.
amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
5 But my house is not so great with God that he should undertake an eternal covenant with me, firm and fortified in all things. For he is the entirety of my salvation and the entirety of my will. And there is nothing of this which will not spring forth.
“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
6 But all prevaricators shall be plucked out like thorns, yet they are not taken away by hands.
Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
7 And if anyone wishes to touch them, he must be armed with iron and a wooden lance. And they shall be set ablaze and burned to nothing.”
Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
8 These are the names of the valiant of David. Sitting in the chair was the wisest leader among the three; he was like a very tender little worm in a tree, who killed eight hundred men in one attack.
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
9 After him, there was Eleazar, the son of his paternal uncle, an Ahohite, who was among the three valiant men who were with David when they chastised the Philistines, and they were gathered together in battle there.
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
10 And when the men of Israel had gone up, he himself stood fast and struck down the Philistines, until his hand grew weak and stiff with the sword. And the Lord wrought a great salvation on that day. And the people who had fled returned to take up the spoils of the slain.
Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
11 And after him, there was Shammah, the son of Agee, from Hara. And the Philistines gathered together at an outpost. For a field full of lentils was in that place. And when the people had fled from the face of the Philistines,
Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
12 he stood fast in the middle of the field, and it was protected by him. And he struck down the Philistines. And the Lord wrought a great salvation.
Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
13 And moreover, before this, the three who were leaders among the thirty descended and went to David at harvest time, in the cave of Adullam. But the camp of the Philistines was positioned in the Valley of the giants.
Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
14 And David was in a stronghold. Moreover, there was a garrison of the Philistines at that time in Bethlehem.
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
15 Then David desired, and he said, “If only someone would give me a drink of the water from the cistern, which is in Bethlehem beside the gate!”
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
16 Therefore, the three valiant men burst into the encampment of the Philistines, and they drew water from the cistern of Bethlehem, which was beside the gate. And they brought it to David. Yet he was not willing to drink; instead, he poured it out to the Lord,
Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
17 saying: “May the Lord be gracious to me, so that I may not do this. Should I drink the blood of these men who have set out to the peril of their own lives?” Therefore, he was not willing to drink. These things were accomplished by these three robust men.
Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
18 Also Abishai, the brother of Joab, the son of Zeruiah, was first among the three. It was he who lifted up his spear against three hundred men, whom he killed. And he was renowned among the three,
Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
19 and he was the noblest of the three, and he was their leader. But at first he did not attain to the three.
Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
20 And Benaiah, the son of Jehoiada, a very strong man of great deeds, was from Kabzeel. He slew the two lions of Moab, and he descended and slew a lion in the middle of a den, in the days of snow.
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
21 He also killed an Egyptian who had a spear in his hand, a man worthy to behold. And yet he had gone down to him with only a staff. And he forced the spear from the hand of the Egyptian, and he killed him with his own spear.
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
22 Benaiah, the son of Jehoiada, accomplished these things.
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
23 And he was renowned among the three robust men, who were the most noble among the thirty. Yet truly, he did not attain to the three, until David made him his secret advisor.
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
24 Among the thirty were: Asahel, the brother of Joab, Elhanan, the son of his paternal uncle, from Bethlehem,
Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
25 Shammah from Harod, Elika from Harod,
Sama Mharodi, Elika Mherodi,
26 Helez from Palti, Ira, the son of Ikkesh, from Tekoa,
Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
27 Abiezer from Anathoth, Mebunnai from Hushah,
Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
28 Zalmon the Ahohite, Maharai the Netophathite,
Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
29 Heleb, the son of Baanah, also himself a Netophathite, Ittai, the son of Ribai, from Gibeah, of the sons of Benjamin,
Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
30 Benaiah the Pirathonite, Hiddai from the Torrent Gaash,
Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
31 Abialbon the Arbathite, Azmaveth from Beromi,
Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
32 Eliahba from Shaalbon; the sons of Jashen, Jonathan,
Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
33 Shammah from Orori, Ahiam, the son of Sharar, the Hararite,
mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
34 Eliphelet, the son of Ahasbai, the son of Maacath, Eliam, the son of Ahithophel, the Gilonite,
Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
35 Hezrai from Carmel, Paarai from Arbi,
Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
36 Igal, the son of Nathan, from Zobah, Bani from Gad,
Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
37 Zelek from Ammon, Naharai the Beerothite, the armor bearer of Joab, the son of Zeruiah,
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
38 Ira the Ithrite, Gareb also an Ithrite,
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
39 Uriah the Hittite: altogether thirty seven
ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.

< 2 Samuel 23 >