< 2 Kings 14 >

1 In the second year of Joash, the son of Jehoahaz, the king of Israel: Amaziah, the son of Jehoash, reigned as king of Judah.
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 He was twenty-five years old when he had begun to reign. And he reigned for twenty-nine years in Jerusalem. The name of his mother was Jehoaddin from Jerusalem.
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 And he did what is right before the Lord, yet truly, not like David, his father. He acted in accord with all the things that his father Jehoash did,
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 except for this alone: he did not take away the high places. For still the people were immolating, and burning incense, in the high places.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 And when he had obtained the kingdom, he struck down those of his servants who had killed his father, the king.
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 But the sons of those who had been killed he did not put to death, in accord with what was written in the book of the law of Moses, just as the Lord instructed, saying: “The fathers shall not die for the sons, and the sons shall not die for the fathers. Instead, each one shall die for his own sin.”
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 He struck down ten thousand men of Idumea, in the Valley of the Salt Pits. And he captured ‘the Rock’ in battle, and he called its name ‘Subdued by God,’ even to the present day.
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 Then Amaziah sent messengers to Joash, the son of Jehoahaz, the son of Jehu, the king of Israel, saying: “Come, and let us see one another.”
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 And Joash, the king of Israel, sent a reply to Amaziah, the king of Judah, saying: “A thistle of Lebanon sent to a cedar, which is in Lebanon, saying: ‘Give your daughter as wife to my son.’ And the beasts of the forest, which are in Lebanon, passed by and trampled the thistle.
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 You have struck and prevailed over Idumea. And your heart has lifted you up. Be content with your own glory, and be seated in your own house. Why would you provoke evil, so that you would fall, and Judah with you?”
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 But Amaziah was not quieted. And so Joash, the king of Israel, went up. And he and Amaziah, the king of Judah, saw one another at Beth-shemesh, a town in Judah.
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 And Judah was struck down before Israel, and they fled, each to their own tents.
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 And truly, Joash, the king of Israel, captured Amaziah, the king of Judah, the son of Jehoash, the son of Ahaziah, at Beth-shemesh. And he brought him to Jerusalem. And he breached the wall of Jerusalem, from the gate of Ephraim as far as the gate of the Corner, four hundred cubits.
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 And he took away all the gold and silver, and all the vessels, which were found in the house of the Lord and in the treasuries of the king, and he returned to Samaria with hostages.
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 But the rest of the words of Joash, which he accomplished, and his strength, with which he fought against Amaziah, the king of Judah, have these not been written in the book of the words of the days of the kings of Israel?
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 And Joash slept with his fathers, and he was buried in Samaria, with the kings of Israel. And Jeroboam, his son, reigned in his place.
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 Now Amaziah, the son of Jehoash, the king of Judah, lived for fifteen years after the death of Joash, the son of Jehoahaz, the king of Israel.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 And the rest of the words of Amaziah, have these not been written in the book of the words of the days of the kings of Judah?
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 And they made a conspiracy against him in Jerusalem. And he fled to Lachish. And they sent after him, to Lachish, and they killed him there.
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 And they carried him away on horses. And he was buried in Jerusalem with his fathers, in the city of David.
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 Then all the people of Judah took Azariah, at sixteen years from birth, and they appointed him as king in place of his father, Amaziah.
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 He built up Elath, and he restored it to Judah, after which the king slept with his fathers.
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 In the fifteenth year of Amaziah, the son of Jehoash, the king of Judah: Jeroboam, the son of Joash, the king of Israel, reigned, in Samaria, for forty-one years.
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 And he did what is evil before the Lord. He did not withdraw from all the sins of Jeroboam, the son of Nebat, who caused Israel to sin.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 He restored the borders of Israel, from the entrance of Hamath as far as the Sea of the Wilderness, in accord with the word of the Lord, the God of Israel, which he spoke through his servant, the prophet Jonah, the son of Amittai, who was from Gath, which is in Hepher.
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 For the Lord saw the exceedingly bitter affliction of Israel, and that they were being consumed, even to those who were enclosed in prison, and even to the least ones, and that there was no one who would help Israel.
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 But the Lord did not say that he would wipe away the name of Israel from under heaven. So instead, he saved them by the hand of Jeroboam, the son of Joash.
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 But the rest of the words of Jeroboam, and all that he did, and his strength, with which he went to battle, and the manner in which he restored Damascus and Hamath to Judah, in Israel, have these not been written in the book of the words of the days of the kings of Israel?
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 And Jeroboam slept with his fathers, the kings of Israel. And Zechariah, his son, reigned in his place.
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Kings 14 >