< 2 Kings 16 >

1 In the seventeenth year of Pekah, the son of Remaliah: Ahaz, the son of Jotham, reigned as king of Judah.
Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Ahaz was twenty years old when he had begun to reign, and he reigned for sixteen years in Jerusalem. He did not do what was pleasing in the sight of the Lord, his God, as his father David did.
Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
3 Instead, he walked in the way of the kings of Israel. Moreover, he even consecrated his son, making him pass through fire, in accord with the idols of the nations that the Lord destroyed before the sons of Israel.
Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
4 Also, he was immolating victims, and burning incense, in the high places, and on the hills, and under every leafy tree.
Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
5 Then Rezin, the king of Syria, and Pekah, the son of Remaliah, the king of Israel, ascended to do battle against Jerusalem. And they besieged Ahaz, but they were not able to overcome him.
Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
6 At that time, Rezin, the king of Syria, restored Elath to Syria, and he expelled the Judeans from Elath. And the Idumeans went into Elath, and they have lived there, even to this day.
Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
7 Then Ahaz sent messengers to Tiglath-pileser, the king of the Assyrians, saying: “I am your servant, and I am your son. Ascend and accomplish my salvation from the hand of the king of Syria, and from the hand of the king of Israel, who have risen up together against me.”
Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
8 And when he had collected the silver and the gold that could be found in the house of the Lord, and in the treasuries of the king, he sent it as a gift to the king of the Assyrians.
Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
9 And he agreed to his will. For the king of the Assyrians ascended against Damascus, and he laid waste to it. And he carried away its inhabitants to Cyrene. But Rezin he killed.
Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
10 And king Ahaz traveled to Damascus to meet Tiglath-pileser, the king of the Assyrians. And when he had seen the altar of Damascus, king Ahaz sent to Uriah, the priest, its pattern and likeness, according to all of its work.
Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
11 And Uriah, the priest, constructed an altar in accord with all that king Ahaz had commanded from Damascus. Uriah, the priest, did so, until king Ahaz arrived from Damascus.
Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
12 And when the king had arrived from Damascus, he saw the altar, and he venerated it. And he went up and immolated holocausts, with his own sacrifice.
Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
13 And he offered libations, and he poured out the blood of the peace offerings, which he had offered, upon the altar.
Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
14 But the altar of brass, which was before the Lord, he took away from the face of the temple, and from the place of the altar, and from the place of the temple of the Lord. And he positioned it at the side of the altar, toward the north.
Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
15 Also, king Ahaz instructed Uriah, the priest, saying: “Upon the great altar, offer the morning holocaust, and the evening sacrifice, and the holocaust of the king, and his sacrifice, and the holocaust of the entire people of the land, and their sacrifices. But their libations, and all the blood of the holocaust, and all the blood of the victim, you shall pour out upon it. Then truly, the altar of brass shall be prepared for use at my will.”
Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
16 And so Uriah, the priest, acted in accord with all that king Ahaz had instructed to him.
Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
17 Then king Ahaz took away the engraved bases, and the basin that was upon them. And he took down the sea from the bronze oxen, which were holding it up. And he positioned it upon a layer of pavement stone.
Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
18 Also, the canopy for the Sabbath, which he had built in the temple, and the exterior entrance of the king, he converted into the temple of the Lord, because of the king of the Assyrians.
Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
19 Now the rest of the words of Ahaz that he did, have these not been written in the book of the words of the days of the kings of Judah?
Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
20 And Ahaz slept with his fathers, and he was buried with them in the city of David. And Hezekiah, his son, reigned in his place.
Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Kings 16 >