< Psalms 99 >

1 The Lord is King; let the peoples be in fear: his seat is on the winged ones; let the earth be moved.
Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
2 The Lord is great in Zion; he is high over all the nations.
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3 Let them give praise to your name, for it is great and to be feared; holy is he.
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
4 The king's power is used for righteousness; you give true decisions, judging rightly in the land of Jacob.
Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5 Give high honour to the Lord our God, worshipping at his feet; holy is he.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
6 Moses and Aaron among his priests, and Samuel among those who gave honour to his name; they made prayers to the Lord, and he gave answers to them.
Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
7 His voice came to them from the pillar of cloud; they kept his witness, and the law which he gave them.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8 You gave them an answer, O Lord our God; you took away their sin, though you gave them punishment for their wrongdoing.
Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9 Give high honour to the Lord our God, worshipping with your faces turned to his holy hill; for the Lord our God is holy.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

< Psalms 99 >