< Proverbs 1 >

1 The wise sayings of Solomon, the son of David, king of Israel.
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 To have knowledge of wise teaching; to be clear about the words of reason:
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 To be trained in the ways of wisdom, in righteousness and judging truly and straight behaviour:
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 To make the simple-minded sharp, and to give the young man knowledge, and serious purpose:
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 (The wise man, hearing, will get greater learning, and the acts of the man of good sense will be wisely guided: )
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 To get the sense of wise sayings and secrets, and of the words of the wise and their dark sayings.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 The fear of the Lord is the start of knowledge: but the foolish have no use for wisdom and teaching.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 My son, give ear to the training of your father, and do not give up the teaching of your mother:
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 For they will be a crown of grace for your head, and chain-ornaments about your neck.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 My son, if sinners would take you out of the right way, do not go with them.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 If they say, Come with us; let us make designs against the good, waiting secretly for the upright, without cause;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Let us overcome them living, like the underworld, and in their strength, as those who go down to death; (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 Goods of great price will be ours, our houses will be full of wealth;
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Take your chance with us, and we will all have one money-bag:
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 My son, do not go with them; keep your feet from their ways:
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 For their feet are running after evil, and they are quick to take a man's life.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Truly, to no purpose is the net stretched out before the eyes of the bird:
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 And they are secretly waiting for their blood and making ready destruction for themselves.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Such is the fate of everyone who goes in search of profit; it takes away the life of its owners.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 Wisdom is crying out in the street; her voice is loud in the open places;
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 Her words are sounding in the meeting-places, and in the doorways of the town:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 How long, you simple ones, will foolish things be dear to you? and pride a delight to the haters of authority? how long will the foolish go on hating knowledge?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Be turned again by my sharp words: see, I will send the flow of my spirit on you, and make my words clear to you.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Because your ears were shut to my voice; no one gave attention to my out-stretched hand;
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 You were not controlled by my guiding, and would have nothing to do with my sharp words:
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 So in the day of your trouble I will be laughing; I will make sport of your fear;
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 When your fear comes on you like a storm, and your trouble like a rushing wind; when pain and sorrow come on you.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Then I will give no answer to their cries; searching for me early, they will not see me:
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 For they were haters of knowledge, and did not give their hearts to the fear of the Lord:
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 They had no desire for my teaching, and my words of protest were as nothing to them.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 So the fruit of their way will be their food, and with the designs of their hearts they will be made full.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 For the turning back of the simple from teaching will be the cause of their death, and the peace of the foolish will be their destruction.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 But whoever gives ear to me will take his rest safely, living in peace without fear of evil.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Proverbs 1 >