< Psalms 78 >

1 Maschil. Of Asaph. Give ear, O my people, to my law; let your ears be bent down to the words of my mouth.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 Opening my mouth I will give out a story, even the dark sayings of old times;
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 Which have come to our hearing and our knowledge, as they were given to us by our fathers.
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 We will not keep them secret from our children; we will make clear to the coming generation the praises of the Lord and his strength, and the great works of wonder which he has done.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 He put up a witness in Jacob, and made a law in Israel; which he gave to our fathers so that they might give knowledge of them to their children;
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 So that the generation to come might have knowledge of them, even the children of the future, who would give word of them to their children;
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 So that they might put their hope in God, and not let God's works go out of their minds, but keep his laws;
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 And not be like their fathers, a stiff-necked and uncontrolled generation; a generation whose heart was hard, whose spirit was not true to God.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 The children of Ephraim, armed with bows, were turned back on the day of the fight.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 They were not ruled by God's word, and they would not go in the way of his law;
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 They let his works go out of their memory, and the wonders which he had made them see.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 He did great works before the eyes of their fathers, in the land of Egypt, in the fields of Zoan.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 The sea was cut in two so that they might go through; the waters were massed together on this side and on that.
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 In the daytime he was guiding them in the cloud, and all through the night with a light of fire.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 The rocks of the waste land were broken by his power, and he gave them drink as out of the deep waters.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 He made streams come out of the rock; and waters came flowing down like rivers.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 And they went on sinning against him even more, turning away from the Most High in the waste land;
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 Testing God in their hearts, requesting meat for their desire.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 They said bitter words against God, saying, Is God able to make ready a table in the waste land?
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 See, the rock was cut open by his power, so that the water came rushing out, and overflowing streams; is he able to give us bread? is he able to get meat for his people?
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 So these things came to the Lord's ears, and he was angry; and a fire was lighted against Jacob, and wrath came up against Israel;
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 Because they had no faith in God, and no hope in his salvation.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 And he gave orders to the clouds on high, and the doors of heaven were open;
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 And he sent down manna like rain for their food, and gave them the grain of heaven.
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Man took part in the food of strong ones; he sent them meat in full measure.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 He sent an east wind from heaven, driving on the south wind by his power.
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 He sent down meat on them like dust, and feathered birds like the sand of the sea,
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 And he let it come down into their resting-place, round about their tents.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 So they had food and were full; for he gave them their desire;
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 But they were not turned from their desires; and while the food was still in their mouths,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 The wrath of God came on them, and put to death the fattest of them, and put an end to the young men of Israel.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 For all this they went on sinning even more, and had no faith in his great wonders.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 So their days were wasted like a breath, and their years in trouble.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 When he sent death on them, then they made search for him; turning to him and looking for him with care;
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 In the memory that God was their Rock, and the Most High God their saviour.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 But their lips were false to him, and their tongues were untrue to him;
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 And their hearts were not right with him, and they did not keep their agreement with him.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 But he, being full of pity, has forgiveness for sin, and does not put an end to man: frequently turning back his wrath, and not being violently angry.
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 So he kept in mind that they were only flesh; a breath which is quickly gone, and will not come again.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 How frequently did they go against him in the waste land, and give him cause for grief in the dry places!
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Again they put God to the test, and gave pain to the Holy One of Israel.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 They did not keep in mind the work of his hand, or the day when he took them from the power of their haters;
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 How he had done his signs in Egypt, and his wonders in the field of Zoan;
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 So that their rivers were turned to blood, and they were not able to get drink from their streams.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 He sent different sorts of flies among them, poisoning their flesh; and frogs for their destruction.
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 He gave the increase of their fields to worms, the fruits of their industry to the locusts.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 He sent ice for the destruction of their vines; their trees were damaged by the bitter cold.
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 Ice was rained down on their cattle; thunderstorms sent destruction among the flocks.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 He sent on them the heat of his wrath, his bitter disgust, letting loose evil angels among them.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 He let his wrath have its way; he did not keep back their soul from death, but gave their life to disease.
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 He gave to destruction all the first sons of Egypt; the first-fruits of their strength in the tents of Ham;
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 But he took his people out like sheep, guiding them in the waste land like a flock.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 He took them on safely so that they had no fear; but their haters were covered by the sea.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 And he was their guide to his holy land, even to the mountain, which his right hand had made his;
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 Driving out nations before them, marking out the line of their heritage, and giving the people of Israel their tents for a resting-place.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 But they were bitter against the Most High God, testing him, and not keeping his laws;
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 Their hearts were turned back and untrue like their fathers; they were turned to one side like a twisted bow.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 They made him angry with their high places; moving him to wrath with their images.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 When this came to God's ears he was very angry, and gave up Israel completely;
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 So that he went away from the holy place in Shiloh, the tent which he had put among men;
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 And he let his strength be taken prisoner, and gave his glory into the hands of his hater.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 He gave his people up to the sword, and was angry with his heritage.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Their young men were burned in the fire; and their virgins were not praised in the bride-song.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 Their priests were put to death by the sword, and their widows made no weeping for them.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Then was the Lord like one awaking from sleep, and like a strong man crying out because of wine.
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 His haters were turned back by his blows and shamed for ever.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 And he put the tent of Joseph on one side, and took not the tribe of Ephraim;
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 But he took the tribe of Judah for himself, and the mountain of Zion, in which he had pleasure.
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 And he made his holy place like the high heaven, like the earth which is fixed by him for ever.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 He took David to be his servant, taking him from the place of the flocks;
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 From looking after the sheep which were giving milk, he took him to give food to Jacob his people, and to Israel his heritage.
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 So he gave them food with an upright heart, guiding them by the wisdom of his hands.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

< Psalms 78 >