< Psalms 120 >

1 A Song of the going up. In my trouble my cry went up to the Lord, and he gave me an answer.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
2 O Lord, be the saviour of my soul from false lips, and from the tongue of deceit.
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
3 What punishment will he give you? what more will he do to you, you false tongue?
Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4 Sharp arrows of the strong, and burning fire.
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
5 Sorrow is mine because I am strange in Meshech, and living in the tents of Kedar.
Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6 My soul has long been living with the haters of peace.
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7 I am for peace: but when I say so, they are for war.
Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

< Psalms 120 >