< ⲖⲞⲨⲔⲞⲚ 14 >

1 ⲁ̅ ⲁⲥϣⲱⲡⲉ ⲇⲉ ϩⲙ̅ⲡⲧⲣⲉϥⲃⲱⲕ ⲉϩⲟⲩⲛ ⲉⲡⲏⲓ̈ ⲛ̅ⲟⲩⲁⲣⲭⲱⲛ ⲙ̅ⲫⲁⲣⲓⲥⲥⲁⲓⲟⲥ ⲙ̅ⲡⲥⲁⲃⲃⲁⲧⲟⲛ ⲉⲩⲙ̅ⲟⲉⲓⲕ ⲛ̅ⲧⲟⲟⲩ ⲇⲉ ⲛⲉⲩⲡⲁⲣⲁⲧⲏⲣⲓ ⲉⲣⲟϥ.
Pa tsiku lina la Sabata, Yesu atapita kukadya ku nyumba ya Mfarisi wodziwika, Afarisi anamulonda mosamalitsa.
2 ⲃ̅ ⲛⲉⲩⲛⲟⲩⲣⲱⲙⲉ ⲇⲉ ⲛ̅ϩⲩⲇⲣⲱⲡⲓⲕⲟⲥ ϩⲁⲧⲉϥϩⲏ.
Poteropo, patsogolo pake panali munthu amene anadwala matenda otupa mimba ndi miyendo.
3 ⲅ̅ ⲁⲓ̅ⲥ̅ ⲟⲩⲱϣⲃ̅ ⲡⲉϫⲁϥ ⲛⲛ̅ⲛⲟⲙⲓⲕⲟⲥ ⲛⲙ̅ⲛⲉⲫⲁⲣⲓⲥⲥⲁⲓⲟⲥ ⲉϥϫⲱ ⲙⲙⲟⲥ ϫⲉ ⲉⲝⲉⲥⲧⲓ ⲉⲣ̅ⲡⲁϩⲣⲉ ϩⲙ̅ⲡⲥⲁⲃⲃⲁⲧⲟⲛ ϫⲉⲛⲟⲩⲕ ⲉⲝⲉⲥⲧⲓ.
Yesu anafunsa Afarisi ndi akatswiri amalamulo kuti, “Kodi ndi zololedwa kuchiritsa pa tsiku la Sabata kapena ayi?”
4 ⲇ̅ ⲛ̅ⲧⲟⲟⲩ ⲇⲉ ⲁⲩⲕⲁⲣⲱⲟⲩ ⲁϥⲁⲙⲁϩⲧⲉ ⲇⲉ ⲙ̅ⲙⲟϥ ⲁϥⲧⲁⲗϭⲟϥ ⲁϥⲕⲁⲁϥ ⲉⲃⲟⲗ.
Koma iwo sanayankhe. Tsono atamutenga munthuyo, Iye anamuchiritsa ndipo anamuwuza kuti azipita.
5 ⲉ̅ ⲡⲉϫⲁϥ ⲛⲁⲩ ϫⲉ ⲛⲓⲙ ⲛ̅ϩⲏⲧʾⲧⲏⲟⲩⲧⲛ ⲡⲉⲧⲉⲣⲉⲡⲉϥϣⲏⲣⲉ ⲏ ⲡⲉϥⲙⲁⲥⲉ ⲛⲁϩⲉ ⲉⲩϣⲱⲧⲉ ⲉⲛϥ̅ⲛⲁⲛⲧϥ̅ ⲁⲛ ⲉϩⲣⲁⲓ̈ ⲛ̅ⲧⲉⲩⲛⲟⲩ ⲙ̅ⲡⲉϩⲟⲟⲩ ⲙ̅ⲡʾⲥⲁⲃⲃⲁⲧⲟⲛ
Kenaka Iye anawafunsa kuti, “Kodi ngati mmodzi mwa inu ali ndi mwana wamwamuna kapena ngʼombe imene yagwera mʼchitsime tsiku la Sabata, kodi simungamuvuwulemo tsiku lomwelo?”
6 ⲋ̅ ⲁⲩⲱ ⲙ̅ⲡⲟⲩϭⲙ̅ϭⲟⲙ ⲉⲟⲩⲟϣⲃⲉϥ ⲛ̅ⲛⲁϩⲣⲛ̅ⲛⲁⲉⲓ·
Ndipo iwo analibe choyankha.
7 ⲍ̅ ⲁϥϫⲱ ⲇⲉ ⲛⲟⲩⲡⲁⲣⲁⲃⲟⲗⲏ ⲛ̅ⲛⲁϩⲣⲛ̅ⲛⲉⲧʾⲧⲁϩⲙ̅ ⲉϥⲛⲁⲩ ⲉⲑⲉ ⲉⲧⲟⲩⲥⲱⲧⲡ̅ ⲛⲁⲩ ⲛⲙ̅ⲙⲁ ⲛ̅ⲛⲟϫⲟⲩ ⲛ̅ⲧⲡⲉ ⲉϥϫⲱ ⲙ̅ⲙⲟⲥ ⲛⲁⲩ
Iye ataona momwe alendo amasankhira malo aulemu pa tebulo, Iye anawawuza fanizo ili:
8 ⲏ̅ ϫⲉ. ϩⲟⲧⲁⲛ ⲉⲣϣⲁⲛⲟⲩⲁ ⲧⲁϩⲙⲉⲕ ⲙ̅ⲡⲣ̅ⲛⲟϫⲕ̅ ⲛ̅ⲧⲡⲉ ⲙⲏⲡⲟⲧⲉ ⲁϥⲧⲁϩⲙ̅ⲟⲩⲁ ⲉϥⲧⲁⲓ̈ⲏⲩ ⲉⲣⲟⲕ
“Pamene wina wakuyitanani ku phwando la ukwati, musakhale pa malo aulemu ayi, chifukwa mwina anayitananso munthu wina wolemekezeka kuposa inu.
9 ⲑ̅ ⲛϥ̅ⲉ͡ⲓ ⲛ̅ϭⲓⲡⲉⲛⲧⲁϥⲧⲁϩⲙⲉⲕ ⲛⲙ̅ⲙⲁϥ ⲛϥ̅ⲙⲟⲩⲧⲉ ⲉⲣⲟⲕ ⲛϥ̅ϫⲟⲟⲥ ⲛⲁⲕ ϫⲉ ⲕⲁⲡⲙⲁ ⲙ̅ⲡⲁⲓ̈. ⲧⲟⲧⲉ ⲕⲛⲁⲁⲣⲭⲓ ϩⲛ̅ⲟⲩϣⲓⲡⲉ ⲉϫⲓ ⲙ̅ⲡⲙⲁ ⲛ̅ϩⲁⲉ.
Ngati zitatero, ndiye kuti munthu uja amene anakuyitani inu nonse awiri adzakuwuzani kuti, ‘Mupatseni munthu uyu malo anu.’ Pamenepo inu mudzachita manyazi, pokakhala malo wotsika.
10 ⲓ̅ ⲁⲗⲗⲁ ⲉⲩϣⲁⲛⲧⲁϩⲙⲉⲕ ⲃⲱⲕ ⲛⲅ̅ⲛⲟϫⲕ̅ ⲙ̅ⲡⲙⲁ ⲛ̅ϩⲁⲉ. ϫⲉⲕⲁⲥ ⲉⲣϣⲁⲛⲡⲉⲛⲧⲁϥⲧⲁϩⲙⲉⲕ ⲉ͡ⲓ ⲛϥ̅ϫⲟⲟⲥ ⲛⲁⲕ ϫⲉ ⲡⲉϣⲃⲏⲣ ⲟ̅ⲗⲉⲕ ⲉϩⲣⲁⲓ ⲉⲡϫⲓⲥⲉ. ⲧⲟⲧⲉ ⲟⲩⲛⲟⲩⲉⲟⲟⲩ ⲛⲁϣⲱⲡⲉ ⲛⲁⲕ ⲙ̅ⲡⲉⲙⲧⲟ ⲉⲃⲟⲗ ⲛ̅ⲛⲉⲧⲛⲏϫ ⲛⲙ̅ⲙⲁⲕ ⲧⲏⲣⲟⲩ.
Koma akakuyitanani, khalani pa malo otsika, kuti amene anakuyitanani uja adzakuwuzeni kuti, ‘Bwenzi, bwera udzakhale pa malo aulemu pano.’ Pamenepo inu mudzalandira ulemu pamaso pa alendo anzanu onse.
11 ⲓ̅ⲁ̅ ϫⲉ ⲟⲩⲟⲛ ⲛⲓⲙ ⲉⲧϫⲓⲥⲉ ⲙ̅ⲙⲟϥ ⲥⲉⲛⲁⲑⲃ̅ⲃⲓⲟϥ. ⲁⲩⲱ ⲡⲉⲧʾⲑⲃ̅ⲃⲓⲟ ⲙ̅ⲙⲟϥ ⲥⲉⲛⲁϫⲁⲥⲧϥ̅.
Pakuti aliyense wodzikuza adzamuchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamukweza.”
12 ⲓ̅ⲃ̅ ⲡⲉϫⲁϥ ⲟⲛ ⲙ̅ⲡⲉⲛⲧⲁϥⲧⲁϩⲙⲉϥ. ϫⲉ ⲉⲕϣⲁⲛⲣ̅ⲟⲩⲁⲣⲓⲥⲧⲟⲛ ⲏ ⲟⲩⲇⲉⲓⲡⲛⲟⲛ ⲙ̅ⲡⲣ̅ⲙⲟⲩⲧⲉ ⲉⲛⲉⲕϣⲃⲉⲉⲣ ⲟⲩⲇⲉ ⲛⲉⲕⲥⲛⲏⲟⲩ. ⲟⲩⲇⲉ ⲛⲉⲕⲥⲩⲅⲅⲉⲛⲏⲥ ⲟⲩⲇⲉ ⲣ̅ⲣⲙ̅ⲙⲁⲟ̅ ⲉⲧϩⲓⲧⲟⲩⲱⲕ. ⲙⲏⲡⲟⲧⲉ ϩⲱⲟⲩ ⲛ̅ⲥⲉⲧⲁϩⲙⲉⲕ ⲛⲧⲉⲟⲩⲧⲟⲩⲓ̈ⲟ̅ ϣⲱⲡⲉ ⲛⲁⲕ.
Kenaka Yesu anati kwa mwini malo uja, “Ukakonza chakudya chamasana kapena chamadzulo, usamayitane abwenzi ako, abale ako, anthu afuko lako kapena anzako achuma; ngati iwe utero, iwo adzakuyitananso, choncho udzalandiriratu mphotho yako.
13 ⲓ̅ⲅ̅ ⲁⲗⲗⲁ ⲉⲕϣⲁⲛⲣ̅ⲟⲩϣⲟⲡⲥ̅. ⲧⲉϩⲙ̅ⲛ̅ϩⲏⲕⲉ ⲛⲙ̅ⲛⲉⲧⲙⲟⲕϩ̅. ⲛⲙ̅ⲛ̅ϭⲁⲗⲉ. ⲛⲙ̅ⲛ̅ⲃⲃⲗ̅ⲗⲉ.
Koma ukakonza phwando, itana anthu osauka, ofa ziwalo, olumala ndi osaona.
14 ⲓ̅ⲇ̅ ⲁⲩⲱ ⲕⲛⲁϣⲱⲡⲉ ⲙ̅ⲙⲁⲕⲁⲣⲓⲟⲥ ϫⲉ ⲙ̅ⲙⲛ̅ⲧⲁⲩ ⲙ̅ⲙⲁⲩ ⲉⲧⲱⲱⲃⲉ ⲛⲁⲕ. ⲥⲉⲛⲁⲧⲟⲟⲃⲟⲩ ⲅⲁⲣ ⲛⲁⲕ ϩⲛ̅ⲧⲁⲛⲁⲥⲧⲁⲥⲓⲥ ⲛⲛ̅ⲇⲓⲕⲁⲓⲟⲥ.
Pamenepo udzakhala wodala, chifukwa iwo sangakubwezere kanthu, koma Mulungu ndiye adzakubwezera pa chiukitso cha olungama.”
15 ⲓ̅ⲉ̅ ⲟⲩⲁ ⲇⲉ ⲉϥⲛⲏϫ ⲛⲙ̅ⲙⲁϥ ⲁϥⲥⲱⲧⲙ̅ ⲉⲛⲁⲓ̈ ⲡⲉϫⲁϥ ⲛⲁϥ ϫⲉ. ⲛⲁⲓ̈ⲁⲧϥ̅ ⲙ̅ⲡⲉⲧⲛⲁⲟⲩⲱⲙ ⲛ̅ⲟⲩⲟⲓ̈ⲕ ϩⲛ̅ⲧⲙⲛ̅ⲧⲉⲣⲟ ⲙ̅ⲡⲛⲟⲩⲧⲉ.
Mmodzi mwa amene amadya naye atamva izi, anati kwa Yesu, “Ndi wodala munthu amene adzadye nawo mu ufumu wa Mulungu.”
16 ⲓ̅ⲋ̅ ⲛ̅ⲧⲟϥ ⲇⲉ ⲡⲉϫⲁϥ ⲛⲁϥ ϫⲉ. ⲟⲩⲣⲱⲙⲉ ⲡⲉ ⲛⲧⲁϥⲣ̅ⲟⲩⲛⲟϭ ⲛ̅ⲇⲓⲡⲛⲟⲛ ⲁⲩⲱ ⲁϥⲧⲉϩⲙ̅ⲟⲩⲙⲏⲏϣⲉ.
Yesu anayankha kuti, “Munthu wina ankakonza phwando lalikulu ndipo anayitana alendo ambiri.
17 ⲓ̅ⲍ̅ ⲁϥϫⲟⲟⲩ ⲇⲉ ⲙⲡⲉϥϩⲙϩⲁⲗ ⲙ̅ⲡⲛⲁⲩ ⲙ̅ⲡⲇⲉⲓⲡⲛⲟⲛ ⲉϫⲟⲟⲥ ⲛ̅ⲛⲉⲧⲧⲁϩⲙ̅ ϫⲉ ⲁⲙⲏⲓ̈ⲧⲛ̅ ϫⲉ ⲁⲛⲕⲁ ⲛⲓⲙ ⲥⲟⲃⲧⲉ.
Nthawi yaphwando itakwana anatuma wantchito wake kuti akawuze onse amene anayitanidwa kuti, ‘Bwerani, pakuti zonse zakonzeka.’
18 ⲓ̅ⲏ̅ ⲁⲩⲁⲣⲭⲓ ⲇⲉ ϩⲓⲟⲩⲥⲟⲡ ⲧⲏⲣⲟⲩ ⲉⲡⲁⲣⲁⲓⲧⲓ. ⲡⲉϫⲉⲡϣⲟⲣⲡ̅ ⲛⲁϥ ϫⲉ ⲁⲓ̈ϣⲉⲡⲟⲩⲥⲱϣⲉ ϯⲛⲁϫⲡⲓⲃⲱⲕ ⲉⲃⲟⲗ ⲉⲛⲁⲩ ⲉⲣⲟⲥ ϯⲥⲟⲡⲥ̅ ⲙ̅ⲙⲟⲕ ⲕⲁⲁⲧʾ ⲛ̅ⲧⲟⲟⲧⲕ̅ ϩⲱⲥⲉⲓ̈ⲡⲁⲣⲁⲓⲧⲓ.
“Koma onse anayamba kupereka zifukwa mofanana. Woyamba anati, ‘Ine ndangogula kumene munda, ndipo ndikuyenera kupita kuti ndikawuone. Pepani mundikhululukire.’
19 ⲓ̅ⲑ̅ ⲡⲉϫⲉⲡⲕⲉⲩⲁ ⲇⲉ ⲛⲁϥ ϫⲉ ⲁⲓ̈ϣⲉⲡϯⲟⲩ ⲛ̅ⲥⲟⲓ̈ϣ ⲛ̅ⲉϩⲉ ϯⲛⲁⲃⲱⲕ ⲧⲁϫⲟⲛⲧⲟⲩ ϯⲥⲟⲡⲥ̅ ⲙ̅ⲙⲟⲕ ⲕⲁⲁⲧʾ ⲛ̅ⲧⲟⲟⲧⲕ̅ ϩⲱⲥⲉⲓ̈ⲡⲁⲣⲁⲓⲧⲓ.
“Wina anati, ‘Ndangogula kumene ngʼombe khumi zokoka ngolo ndipo kupita kukaziyesa. Pepani mundikhululukire.’
20 ⲕ̅ ⲡⲉϫⲉⲡⲕⲉⲟⲩⲁ ⲇⲉ ϫⲉ. ⲁⲓ̈ϩⲙⲟⲟⲥ ⲛⲙ̅ⲟⲩⲥϩⲓⲙⲉ ⲉⲧⲃⲉϫⲉⲙ̅ⲙⲛϣ̅ϭⲟⲙ ⲙ̅ⲙⲟⲓ̈ ⲉⲉ͡ⲓ.
“Wina anatinso, ‘Ine ndangokwatira kumene, choncho sinditha kubwera.’
21 ⲕ̅ⲁ̅ ⲁⲡϩⲙ̅ϩⲁⲗ ⲇⲉ ⲉ͡ⲓ ⲁϥϫⲱ ⲛ̅ⲛⲁⲓ ⲉⲡⲉϥϫⲟⲉⲓⲥ. ⲧⲟⲧⲉ ⲁⲡϫⲟⲉⲓⲥ ⲛⲟⲩϭⲥ̅ ⲡⲉϫⲁϥ ⲙ̅ⲡⲉϥϩⲙ̅ϩⲁⲗ ϫⲉ ⲃⲱⲕ ⲉⲃⲟⲗ ϭⲉⲡⲏ ⲉⲛⲉⲡⲗⲁⲧⲓⲁ ⲛⲙ̅ⲛ̅ϩⲓⲣ ⲛⲙ̅ⲙ̅ⲡⲟⲗⲓⲥ ⲛ̅ⲕⲛ̅ⲛ̅ϩⲏⲕⲉ ⲉϩⲟⲩⲛ ⲛⲙ̅ⲛⲉⲧⲙⲟⲕϩ̅ ⲛⲙ̅ⲛ̅ⲃⲗ̅ⲗⲉ. ⲛⲙ̅ⲛ̅ϭⲁⲗⲉ. ⲉϩⲟⲩⲛ ⲉⲡⲉⲓ̈ⲙⲁ.
“Wantchitoyo anabwera ndikudzamuwuza bwana wakeyo zimenezi. Pamenepo mphwandoyo anapsa mtima ndipo analamula wantchito wakeyo kuti, ‘Pita msangamsanga kunja mʼmisewu ndi mʼmakwalala a mu mzinda ndipo ukabweretse osauka, ofa ziwalo, osaona ndi olumala.’
22 ⲕ̅ⲃ̅ ⲡⲉϫⲉⲡϩⲙ̅ϩⲁⲗ ⲇⲉ ϫⲉ. ⲡϫⲟⲉⲓⲥ ⲁⲡⲉⲛⲧⲁⲕϫⲟⲟϥ ϣⲱⲡⲉ ⲁⲩⲱ ⲟⲛ ⲟⲩⲙ̅ⲙⲁ.
“Wantchitoyo anati, ‘Bwana, zimene munanena zachitika koma malo akanalipobe.’
23 ⲕ̅ⲅ̅ ⲡⲉϫⲉⲡϫⲟⲉⲓⲥ ⲙ̅ⲡϩⲙ̅ϩⲁⲗ ϫⲉ ⲃⲱⲕ ⲉⲃⲟⲗ ⲉⲛⲉϩⲓⲟⲟⲩⲉ ⲛⲙ̅ⲙⲁ ⲙ̅ⲙⲟⲟϣⲉ ⲛⲅ̅ⲁⲛⲁⲅⲕⲁⲍⲉ ⲙ̅ⲙⲟⲟⲩ ⲉⲉ͡ⲓ ⲉϩⲟⲩⲛ ϫⲉ ⲉⲣⲉⲡⲁⲏⲓ̈ ⲙⲟⲩϩ
“Ndipo mbuye uja anawuza wantchito wake kuti, ‘Pita kunja ku misewu ikuluikulu ndi kunja kwa mpanda ndipo ukawawuze kuti alowe, kuti nyumba yanga idzaze.
24 ⲕ̅ⲇ̅ ϯϫⲱ ⲙ̅ⲙⲟⲥ ⲛⲏⲧⲛ̅ ϫⲉ ⲙ̅ⲙⲛ̅ⲗⲁⲁⲩ ⲛ̅ⲛⲉⲧʾⲧⲁϩⲙ̅ ⲛⲁϫⲓϯⲡⲉ ⲙ̅ⲡⲁⲇⲉⲓⲡⲛⲟⲛ·
Ine ndikukuwuzani inu kuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anayitanidwa adzalawa phwandolo.’”
25 ⲕ̅ⲉ̅ ⲛⲉⲩⲙⲟⲟϣⲉ ⲇⲉ ⲛⲙ̅ⲙⲁϥ ⲡⲉ ⲛ̅ϭⲓϩⲉⲛⲙⲏⲏϣⲉ ⲉⲛⲁϣⲱⲟⲩ. ⲁϥⲕⲟⲧϥ̅ ⲇⲉ ⲡⲉϫⲁϥ ⲛⲁⲩ
Gulu lalikulu la anthu linkayenda naye Yesu ndipo atatembenukira kwa iwo anati,
26 ⲕ̅ⲋ̅ ϫⲉ. ⲡⲉⲧⲛⲏⲟⲩ ϣⲁⲣⲟⲓ̈ ⲉⲛϥ̅ⲙⲟⲥⲧⲉ ⲁⲛ ⲙ̅ⲡⲉϥⲓ̈ⲱⲧʾ. ⲛⲙ̅ⲧⲉϥⲙⲁⲁⲩ. ⲛⲙ̅ⲧⲉϥⲥϩⲓⲙⲉ. ⲛⲙ̅ⲛⲉϥϣⲏⲣⲉ. ⲛⲙ̅ⲛⲉϥⲥⲛⲏⲟⲩ. ⲛⲙ̅ⲛⲉϥⲥⲱⲛⲉ. ⲉⲧⲓ ⲇⲉ ⲧⲉϥⲕⲉⲯⲩⲭⲏ ⲙ̅ⲙⲛ̅ϣϭⲟⲙ ⲉⲧⲣⲉϥⲣ̅ⲙⲁⲑⲏⲧⲏⲥ ⲛⲁⲓ̈
“Ngati wina aliyense abwera kwa Ine ndipo sadana ndi abambo ndi amayi ake, mkazi wake ndi ana, abale ake ndi alongo ake, inde ngakhale moyo wake omwe, iye sangakhale ophunzira wanga.
27 ⲕ̅ⲍ̅ ⲁⲩⲱ ⲡⲉⲧⲉⲛϥ̅ⲛⲁϥⲓ ⲁⲛ ⲙ̅ⲡⲉϥⲥxⲟⲥ ⲙ̅ⲙⲏⲛⲉ ⲛϥ̅ⲟⲩⲁϩϥ̅ ⲛ̅ⲥⲱⲓ̈ ⲙ̅ⲙⲛ̅ϣϭⲟⲙ ⲉⲧⲣⲉϥϣⲱⲡⲉ ⲛⲁⲓ̈ ⲙ̅ⲙⲁⲑⲏⲧⲏⲥ.
Ndipo aliyense amene sasenza mtanda wake ndi kunditsata Ine sangakhale ophunzira wanga.
28 ⲕ̅ⲏ̅ ⲛⲓⲙ ⲅⲁⲣ ⲙ̅ⲙⲱⲧⲛ̅ ⲉϥⲟⲩⲉϣⲕⲉⲧʾⲟⲩⲡⲩⲣⲅⲟⲥ ⲙⲏ ⲛϥ̅ⲛⲁϩⲙⲟⲟⲥ ⲁⲛ ⲛ̅ϣⲟⲣⲡ̅ ⲛϥ̅ϥⲓⲡⲱⲡ ⲛ̅ⲧⲉϥⲧⲁⲡⲁⲛⲏ ϫⲉ ⲟⲩⲛⲧⲁϥ ⲉϫⲟⲕϥ̅ ⲉⲃⲟⲗ
“Taganizani, ngati wina mwa inu akufuna kumanga nsanja, kodi iye sayamba wakhala pansi ndi kuganizira za mtengo wake kuti aone ngati ali ndi ndalama zokwanira kuti atsirizire?
29 ⲕ̅ⲑ̅ ϫⲉⲕⲁⲥ ⲉⲛⲛⲉϥⲥⲙⲛ̅ⲥⲛⲧⲉ ⲛϥ̅ⲧⲙ̅ϭⲙ̅ϭⲟⲙ ⲉϫⲟⲕϥ̅ ⲉⲃⲟⲗ ⲛ̅ⲧⲉⲟⲩⲟⲛ ⲛⲓⲙ ⲉⲧⲛⲁⲩ ⲉⲣⲟϥ ⲥⲱⲃⲉ ⲛ̅ⲥⲱϥ
Pakuti ngati ayika maziko ndi kulephera kutsiriza, aliyense amene adzayiona adzamuseka,
30 ⲗ̅ ⲉⲩϫⲱ ⲙ̅ⲙⲟⲥ ϫⲉ ⲁⲡⲉⲓ̈ⲣⲱⲙⲉ ⲁⲣⲭⲓ ⲛ̅ⲕⲱⲧʾ ⲙ̅ⲡϥⲉϣϭⲙ̅ϭⲟⲙ ⲉϫⲟⲕϥ̅ ⲉⲃⲟⲗ.
nanena kuti, ‘Munthu uyu anayamba kumanga koma sanathe kutsiriza.’
31 ⲗ̅ⲁ̅ ⲏ ⲛⲓⲙ ⲛⲣ̅ⲣⲟ ⲉϥⲛⲁⲃⲱⲕ ⲉⲙⲓϣⲉ ⲛⲙ̅ⲕⲉⲣ̅ⲣⲟ ⲙⲏ ⲛϥ̅ⲛⲁϩⲙⲟⲟⲥ ⲁⲛ ⲛ̅ϣⲟⲣⲡ̅ ⲛϥ̅ϫⲓϣⲟϫⲛⲉ ϫⲉ ⲟⲩⲛϭⲟⲙ ⲙ̅ⲙⲟϥ ⲉⲧⲱⲙⲧ̅ʾ ϩⲛⲟⲩⲧⲃ͡ⲁ ⲉⲡⲉⲧⲛⲏⲟⲩ ⲉϫⲱϥ ⲛⲙ̅ⲧⲃⲁ ⲥⲛⲁⲩ.
“Kapena mfumu imene ikupita ku nkhondo kukamenyana ndi mfumu ina, kodi siyamba yakhala pansi ndi kulingalira ngati ingathe ndi anthu 10,000 kulimbana ndi amene akubwera ndi 20,000?
32 ⲗ̅ⲃ̅ ⲉϣⲱⲡⲉ ⲙ̅ⲙⲟⲛ ⲉⲧⲓ ⲉϥⲙ̅ⲡⲟⲩⲉ ϥⲛⲁϫⲟⲟⲩ ⲛ̅ϩⲉⲛϥⲁⲓ̈ϣⲓⲛⲉ ⲉϥⲥⲟⲡⲥ̅ ϫⲉ ⲁⲣⲓⲉ͡ⲓⲣⲏⲛⲏ.
Ngati singathe, idzatuma nthumwi pomwe winayo ali kutali ndi kukapempha mgwirizano wamtendere.
33 ⲗ̅ⲅ̅ ⲧⲁⲓ̈ ϭⲉ ⲧⲉ ⲑⲉ ⲛ̅ⲟⲩⲟⲛ ⲛⲓⲙ ⲉⲃⲟⲗ ⲛ̅ϩⲏⲧʾⲧⲏⲩⲧⲛ̅ ⲉⲛϥ̅ⲛⲁⲁⲡⲟⲧⲁⲥⲥⲉ ⲁⲛ ⲛ̅ⲛⲉϥϩⲩⲡⲁⲣⲭⲟⲛⲧⲁ ⲧⲏⲣⲟⲩ. ⲙ̅ⲙⲛ̅ϣϭⲟⲙ ⲙ̅ⲙⲟϥ ⲉⲧⲣⲉϥϣⲱⲡⲉ ⲛⲁⲓ̈ ⲙ̅ⲙⲁⲑⲏⲧⲏⲥ.
Mʼnjira yomweyo, wina aliyense wa inu amene sasiya zonse ali nazo sangakhale ophunzira wanga.
34 ⲗ̅ⲇ̅ ⲛⲁⲛⲟⲩⲡⲉϩⲙⲟⲩ ⲇⲉ ⲉⲣϣⲁⲛⲡⲕⲉϩⲙⲟⲩ ⲇⲉ ⲃⲁⲁⲃⲉ ⲉⲩⲛⲁⲙⲟⲗϩϥ̅ ⲛⲟⲩ.
“Mchere ndi wabwino, koma ngati usukuluka adzawukoleretsanso ndi chiyani?
35 ⲗ̅ⲉ̅ ⲙⲉϥⲣ̅ϣⲁⲩ ⲉⲡⲕⲁϩ ⲟⲩⲧⲉ ⲉⲧⲕⲟⲡⲣⲓⲁ ⲉϣⲁⲩⲛⲟϫϥ̅ ⲉⲃⲟⲗ. ⲡⲉⲧⲉⲟⲩⲛⲙⲁⲁϫⲉ ⲙ̅ⲙⲟϥ ⲉⲥⲱⲧⲙ̅ ⲙⲁⲣⲉϥⲥⲱⲧⲙ̅·
Suyeneranso ngakhale mʼnthaka kapena kudzala la manyowa; umatayidwa kunja. “Amene ali ndi makutu akumva, amve.”

< ⲖⲞⲨⲔⲞⲚ 14 >