< ⲖⲞⲨⲔⲞⲚ 16 >

1 ⲁ̅ ⲡⲉϫⲁϥ ⲇⲉ ⲛ̅ⲛⲉϥⲙⲁⲑⲏⲧⲏⲥ ϫⲉ ⲛⲉⲩⲛⲟⲩⲣⲱⲙⲉ ⲣ̅ⲣⲙ̅ⲙⲁⲟ ⲉⲩⲛ̅ⲧⲁϥ ⲙ̅ⲙⲁⲩ ⲛⲟⲩⲟⲓⲕⲟⲛⲟⲙⲟⲥ ⲁⲩⲧⲁⲁϥ ⲇⲉ ⲛ̅ϣⲧⲟⲩⲏⲧʾ ϫⲉ ϥϫⲱⲱⲣⲉ ⲉⲃⲟⲗ ⲛ̅ⲛⲉϥϩⲩⲡⲁⲣⲭⲟⲛⲧⲁ
Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho.
2 ⲃ̅ ⲁϥⲙⲟⲩⲧⲉ ⲉⲣⲟϥ ⲡⲉϫⲁϥ ⲛⲁϥ ϫⲉ ⲟⲩ ⲡⲉ ⲡⲁⲓ̈ ⲉϯⲥⲱⲧⲙ̅ ⲙ̅ⲙⲟϥ ⲉⲧⲃⲏⲧⲕ̅. ⲁⲩⲡⲱⲡ ⲛⲁⲓ̈ ⲛ̅ⲧⲉⲕⲟⲓⲕⲟⲛⲟⲙⲓⲁ ⲙ̅ⲙⲛ̅ϣϭⲟⲙ ⲅⲁⲣ ϫⲓⲛⲧⲉⲛⲟⲩ ⲉⲧⲣⲉⲕⲟⲓⲕⲟⲛⲟⲙⲓ.
Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’
3 ⲅ̅ ⲡⲉϫⲉⲡⲟⲓⲕⲟⲛⲟⲙⲟⲥ ⲇⲉ ϩⲙ̅ⲡⲉϥϩⲏⲧ ϫⲉ ⲉⲓ̈ⲛⲁⲣⲟⲩ ϫⲉ ⲡⲁϫⲟⲉⲓⲥ ⲛⲁϥⲓ ⲛ̅ⲧⲟⲓⲕⲟⲛⲟⲙⲓⲁ ⲛ̅ⲧⲟⲟⲧʾ ⲙ̅ⲙⲛ̅ϣϭⲟⲙ ⲙ̅ⲙⲟⲓ̈ ⲉϭⲣⲏ ⲁⲩⲱ ϯϣⲓⲡⲉ ⲉⲧⲱⲃⲁϩ.
“Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha.
4 ⲇ̅ ⲁⲓ̈ⲉ͡ⲓⲙⲉ ϫⲉ ⲉⲓ̈ⲛⲁⲣⲟⲩ ϫⲉⲕⲁⲥ ⲉⲩϣⲁⲛϥⲓⲧʾ ϩⲛⲧⲟⲓⲕⲟⲛⲟⲙⲓⲁ. ⲉⲩⲉϫⲓⲧʾ ⲉϩⲟⲩⲛ ⲉⲛⲉⲩⲏⲓ̈.
Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’
5 ⲉ̅ ⲁϥⲙⲟⲩⲧⲉ ⲇⲉ ⲉⲡⲟⲩⲁ ⲡⲟⲩⲁ ⲛ̅ⲛⲉⲧⲉⲟⲩⲛⲧⲉⲡⲉϥϫⲟⲉⲓⲥ ⲉⲣⲟⲟⲩ. ⲡⲉϫⲁϥ ⲙ̅ⲡϣⲟⲣⲡ̅ ϫⲉ ⲟⲩⲛⲧⲉⲡⲁϫⲟⲉⲓⲥⲟⲩⲏⲣ ⲉⲣⲟⲕ
“Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’
6 ⲋ̅ ⲛ̅ⲧⲟϥ ⲇⲉ ⲡⲉϫⲁϥ ϫⲉ ϣⲉ ⲃ̅ⲃⲁⲧⲟⲥ ⲛ̅ⲛⲉϩ. ⲡⲉϫⲁϥ ⲛⲁϥ ϫⲉ ϫⲓⲡⲉⲕⲥϩⲁⲓ̈ ⲛⲅ̅ϩⲙⲟⲟⲥ ϭⲉⲡⲏ ⲛⲅ̅ⲥϩⲁⲓ̈ ⲉⲧⲁⲓ̈ⲟⲩ.
“Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’ “Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’
7 ⲍ̅ ⲙ̅ⲙⲛ̅ⲛ̅ⲥⲱⲥ ⲡⲉϫⲁϥ ⲛ̅ⲕⲉⲟⲩⲁ ϫⲉ ⲛ̅ⲧⲟⲕ ⲟⲩⲛⲟⲩⲏⲣ ⲉⲣⲟⲕ. ⲡⲉϫⲁϥ ϫⲉ ϣⲉ ⲛ̅ⲕⲟⲣⲟⲥ ⲛ̅ⲥⲟⲩⲟ. ⲡⲉϫⲁϥ ϫⲉ ϫⲓⲡⲉⲕⲥϩⲁⲓ̈ ⲛⲅ̅ⲥϩⲁⲓ̈ ⲉϩⲙⲉⲛⲉ.
“Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’ “Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000. “Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’
8 ⲏ̅ ⲁⲡϫⲟⲉⲓⲥ ⲇⲉ ⲉⲡⲁⲓⲛⲟⲩ ⲙ̅ⲡⲟⲓⲕⲟⲛⲟⲙⲟⲥ ⲙ̅ⲡʾϫⲓ ⲛϭⲟⲛⲥ̅ ϫⲉ ⲁϥⲉ͡ⲓⲣⲉ ϩⲛ̅ⲟⲩⲙⲛⲧ̅ⲣⲙ̅ⲛ̅ϩⲏⲧʾ ϫⲉ ϩⲉⲛⲥⲁⲃⲉ ⲛⲉ ⲛ̅ϣⲏⲣⲉ ⲙ̅ⲡⲉⲓ̈ⲁⲓⲱⲛ ⲉϩⲟⲩⲉⲛ̅ϣⲏⲣⲉ ⲙ̅ⲡⲟⲩⲟⲓ̈ⲛ ⲉⲧⲉⲩⲅⲉⲛⲉⲁ. (aiōn g165)
“Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn g165)
9 ⲑ̅ ⲁⲛⲟⲕ ϩⲱ ϯϫⲱ ⲙ̅ⲙⲟⲥ ⲛⲏⲧⲛ̅ ϫⲉ. ⲕⲁϩⲉⲛϣⲃⲏⲣ ⲛⲏⲧⲛ̅ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲙ̅ⲡⲁⲙⲙⲱⲛⲁⲥ ⲛⲧⲁⲇⲓⲕⲓⲁ ϫⲉⲕⲁⲥ ⲉϥϣⲁⲛⲱ̑ϫⲛ̅. ⲉⲩⲉϫⲓⲧⲏⲩⲧⲛ ⲉϩⲟⲩⲛ ⲉⲛⲉⲥⲕⲏⲛⲏ ⲛ̅ϣⲁⲉⲛⲉϩ. (aiōnios g166)
Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios g166)
10 ⲓ̅ ⲡ̅ⲡⲓⲥⲧⲟⲥ ϩⲛ̅ⲟⲩⲕⲟⲩⲓ̈. ⲟⲩⲡⲓⲥⲧⲟⲥ ⲟⲛ ⲡⲉ ϩⲛ̅ⲟⲩⲛⲟϭ. ⲁⲩⲱ ⲡⲁⲇⲓⲕⲟⲥ ϩⲛ̅ⲟⲩⲕⲟⲩⲓ̈. ⲟⲩⲁⲇⲓⲕⲟⲥ ⲟⲛ ⲡⲉ ϩⲛ̅ⲟⲩⲛⲟϭ.
“Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri.
11 ⲓ̅ⲁ̅ ⲉϣϫⲉⲙ̅ⲡⲉⲧⲛ̅ϣⲱⲡⲉ ϭⲉ ⲙ̅ⲡⲓⲥⲧⲟⲥ ϩⲙ̅ⲡⲁⲙⲙⲱⲛⲁⲥ ⲛ̅ⲁⲇⲓⲕⲟⲥ ⲛⲓⲙ ⲡⲉⲧⲛⲁⲧⲁⲛϩⲉⲧʾⲧⲏⲟⲩⲧⲛ̅ ⲉⲡⲉⲧⲉϩⲱⲱϥ ⲡⲉ.
Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni?
12 ⲓ̅ⲃ̅ ⲁⲩⲱ ⲉϣϫⲉⲙ̅ⲡⲉⲧⲛ̅ⲣ̅ⲡⲓⲥⲧⲟⲥ ϩⲙ̅ⲡⲉⲧⲉⲙ̅ⲡⲱⲧⲛ̅ ⲁⲛ ⲡⲉ. ⲛⲓⲙ ⲡⲉⲧⲛⲁϯ ⲛⲏⲧⲛ̅ ⲙ̅ⲡⲉⲧⲉⲡⲱⲧⲛ̅ ⲡⲉ.
Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?
13 ⲓ̅ⲅ̅ ⲙ̅ⲙⲛϣϭⲟⲙ ⲗ̅ⲗⲁⲁⲩ ⲉⲣ̅ϩⲙ̅ϩⲁⲗ ⲛϫⲟⲉⲓⲥ ⲥⲛⲁⲩ. ⲏ ⲅⲁⲣ ϥⲛⲁⲙⲉⲥⲧⲉⲟⲩⲁ ⲛϥ̅ⲙⲉⲣⲉⲟⲩⲁ. ⲏ ⲛϥ̅ⲁⲛⲉⲭⲉⲟⲩⲁ ⲛϥ̅ⲕⲁⲧⲁⲫⲣⲟⲛⲓⲟⲩⲁ. ⲙⲙⲛϣϭⲟⲙ ⲙ̅ⲙⲱⲧⲛ̅ ⲉⲧⲣⲉⲧⲛ̅ⲣϩⲙ̅ϩⲁⲗ ⲙ̅ⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲛⲙ̅ⲡⲁⲙⲙⲱⲛⲁⲥ.
“Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”
14 ⲓ̅ⲇ̅ ⲁⲛⲉⲫⲁⲣⲓⲥⲥⲁⲓⲟⲥ ⲇⲉ ⲥⲱⲧⲙ̅ ⲉⲛⲁⲓ̈ ⲧⲏⲣⲟⲩ ⲉϩⲉⲛⲙⲁⲓ̈ϩⲟⲙⲛ̅ⲧ ⲛⲉ. ⲁⲩⲕⲱⲙϣ̅ ⲛ̅ⲥⲱϥ.
Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu.
15 ⲓ̅ⲉ̅ ⲡⲉϫⲁϥ ⲇⲉ ⲛⲁⲩ ϫⲉ ⲛ̅ⲧⲱⲧⲛ̅ ⲛⲉⲧʾⲧⲙⲁⲓ̈ⲟ ⲙ̅ⲙⲱⲧⲛ̅ ⲙ̅ⲡⲉⲙⲧⲟ ⲉⲃⲟⲗ ⲛⲣ̅ⲣⲱⲙⲉ. ⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲇⲉ ⲥⲟⲟⲩⲛ ⲛ̅ⲛⲉⲧⲛϩⲏⲧʾ ϫⲉ ⲧⲙⲛ̅ⲧϫⲁⲥⲓϩⲏⲧʾ ⲉⲧϩⲛ̅ⲣ̅ⲣⲱⲙⲉ. ⲟⲩⲃⲟⲧⲉ ⲧⲉ ⲙ̅ⲡⲉⲙⲧⲟ ⲉⲃⲟⲗ ⲙⲡⲛⲟⲩⲧⲉ.
Yesu anawawuza kuti, “Inu ndi amene mumadzilungamitsa nokha pamaso pa anthu, koma Mulungu amadziwa mitima yanu. Zinthu zimene anthu amaziyesa zopambana, ndi zonyansa pamaso pa Mulungu.
16 ⲓ̅ⲋ̅ ⲡⲛⲟⲙⲟⲥ ⲛⲙ̅ⲛⲉⲡⲣⲟⲫⲏⲧⲏⲥ ⲛ̅ⲧⲁⲩⲡⲱϩ ϣⲁⲓ̈ⲱϩⲁⲛⲛⲏⲥ. ϫⲓⲛⲡⲉⲩⲟⲉⲓϣ ⲉⲧⲙ̅ⲙⲁⲩ ⲥⲉⲉⲩⲁⲅⲅⲉⲗⲓⲍⲉ ⲛ̅ⲧⲙⲛ̅ⲧⲉⲣⲟ ⲙ̅ⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲁⲩⲱ ⲟⲩⲟⲛ ⲛⲓⲙ ϫⲓ ⲙ̅ⲙⲟϥ ⲛ̅ϭⲟⲛⲥ̅ ⲉⲣⲟⲥ.
“Malamulo ndi Aneneri zinagwira ntchito mpaka nthawi ya Yohane. Kuyambira nthawi imeneyo, Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ukulalikidwa, ndipo aliyense akuyesetsa mwamphamvu kuti alowemo.
17 ⲓ̅ⲍ̅ ⲥⲙⲟⲧⲛ̅ ⲇⲉ ⲉⲧⲣⲉⲧⲡⲉ ⲛⲙ̅ⲡⲕⲁϩ ⲡⲁⲣⲁⲅⲉ ⲏ ⲉⲧⲣⲉⲟⲩϣⲱⲗϩ̅ ⲛⲟⲩⲱⲧʾ ϩⲉ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲙ̅ⲡⲛⲟⲙⲟⲥ.
Nʼkwapafupi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zichoke kulekana ndi kuti kalemba kakangʼono kachoke mʼMalamulo.
18 ⲓ̅ⲏ̅ ⲟⲩⲟⲛ ⲛⲓⲙ ⲉⲧⲛⲁⲛⲉϫⲧⲉϥⲥϩⲓⲙⲉ ⲉⲃⲟⲗ ⲛϥ̅ϩⲙⲟⲟⲥ ⲛⲙ̅ⲕⲉⲩⲉ͡ⲓ ϥⲟ ⲛ̅ⲛⲟⲉⲓⲕ. ⲁⲩⲱ ⲡⲉⲧⲛⲁϩⲙⲟⲟⲥ ⲛⲙ̅ⲕⲉⲩⲉ͡ⲓ ⲉⲁⲡⲉⲥϩⲁⲓ̈ ⲛⲟϫⲥ̅ ⲉⲃⲟⲗ. ϥⲟ ⲛ̅ⲛⲟⲉⲓⲕ·
“Aliyense amene asiya mkazi wake ndi kukakwatira mkazi wina akuchita chigololo, ndipo mwamuna amene akwatira mkazi wosiyidwayo akuchitanso chigololo.”
19 ⲓ̅ⲑ̅ ⲛⲉⲩⲛⲟⲩⲣⲱⲙⲉ ⲇⲉ ⲣ̅ⲣⲙ̅ⲙⲁⲟ ⲉⲡⲉϥⲣⲁⲛ ⲡⲉ ⲛⲓⲛⲉⲩⲏ ⲉϣⲁϥϯ ϩⲓⲱⲱϥ ⲛ̅ⲟⲩϫⲏϭⲉ ⲛⲙ̅ⲟⲩϣⲛ̅ⲥ ⲉϥⲉⲩⲫⲣⲁⲛⲉ ⲙ̅ⲙⲏⲛⲉ ⲕⲁⲗⲱⲥ.
“Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse.
20 ⲕ̅ ⲛⲉⲩⲛⲟⲩϩⲏⲕⲉ ⲇⲉ ⲉⲡⲉϥⲣⲁⲛ ⲡⲉ ⲗⲁⲍⲁⲣⲟⲥ ⲉϥⲛⲏϫ ϩⲛ̅ⲧⲉϥϩⲁⲓ̈ⲧʾ ⲉϥⲟ̅ ⲛ̅ⲥⲁϣ
Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse
21 ⲕ̅ⲁ̅ ⲉϥⲉⲡⲓⲑⲩⲙⲓ ⲉⲥⲓ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲛ̅ⲛⲉϣⲁⲩϩⲉ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲛ̅ⲧⲉⲧⲣⲁⲡⲉⲍⲁ ⲙ̅ⲡⲣⲙ̅ⲙⲁⲟ̅. ⲁⲗⲗⲁ ⲛ̅ⲕⲉⲟⲩϩⲟⲟⲣ ϣⲁⲩⲉ͡ⲓ ⲛ̅ⲥⲉⲗⲱϫϩ̅ ⲛ̅ⲛⲉϥⲥⲁϣ.
ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.
22 ⲕ̅ⲃ̅ ⲁⲥϣⲱⲡⲉ ⲇⲉ ϩⲙⲡⲧⲣⲉⲡϩⲏⲕⲉ ⲙⲟⲩ ⲛ̅ⲥⲉϫⲓⲧϥ̅ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲓⲧⲛ̅ⲛ̅ⲛⲁⲅⲅⲉⲗⲟⲥ ⲉⲕⲟⲩⲛϥ̅ ⲛⲁⲃⲣⲁϩⲁⲙ ⲁⲡⲕⲉⲣⲙ̅ⲙⲁⲟ ⲇⲉ ⲙⲟⲩ ⲁⲩⲧⲟⲙⲥϥ̅.
“Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda.
23 ⲕ̅ⲅ̅ ⲁϥϥⲓⲁⲧϥ̅ ⲇⲉ ⲉϩⲣⲁⲓ̈ ϩⲛⲁⲙⲛ̅ⲧⲉ ⲉϥϣⲟⲟⲡ ϩⲛ̅ϩⲉⲛⲃⲁⲥⲁⲛⲟⲥ ⲁϥⲛⲁⲩ ⲉⲁⲃⲣⲁϩⲁⲙ ⲙⲡⲟⲩⲉ. ⲁⲩⲱ ⲗⲁⲍⲁⲣⲟⲥ ϩⲛ̅ⲕⲟⲩⲛϥ̅ (Hadēs g86)
Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs g86)
24 ⲕ̅ⲇ̅ ⲁϥⲙⲟⲩⲧⲉ ⲇⲉ ⲡⲉ(ϫⲁϥ) ϫⲉ ⲡⲓⲱⲧʾ ⲁⲃⲣⲁϩⲁⲙ ⲛ͡ⲁ ⲛⲁⲓ̈. ⲙⲁⲧⲛ̅ⲛⲉⲩⲗⲁⲍⲁⲣⲟⲥ ⲛϥ̅ⲥⲉⲡϩⲧⲏϥ ⲙⲡⲉϥⲧⲏⲏⲃⲉ ⲙ̅ⲙⲟⲟⲩ ⲛϥ̅ⲕⲃⲉⲡⲁⲗⲁⲥ ϫⲉ ϯⲙⲟⲕϩ̅ ⲁⲛⲟⲕ ϩⲙ̅ⲡⲉⲓ̈ⲕⲱϩⲧ̅ʾ.
Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’
25 ⲕ̅ⲉ̅ ⲡⲉϫⲉⲁⲃⲣⲁϩⲁⲙ ⲇⲉ ϫⲉ ⲡⲁϣⲏⲣⲉ ⲁⲣⲓⲡⲙⲉⲉⲩⲉ ϫⲉ ⲁⲕϫⲓ ⲛ̅ⲛⲉⲕⲁⲅⲁⲑⲟⲛ ϩⲙ̅ⲡⲉⲕⲱⲛⲁϩ. ⲁⲩⲱ ⲗⲁⲍⲁⲣⲟⲥ ϩⲱⲱϥ ϩⲛ̅ϩⲉⲛⲡⲉⲑⲟⲟⲩ. ⲧⲉⲛⲟⲩ ⲇⲉ ⲥⲉⲥⲟⲗⲥⲗ̅ ⲙ̅ⲙⲟϥ ⲙ̅ⲡⲉⲓ̈ⲙⲁ. ⲛ̅ⲧⲟⲕ ⲇⲉ ⲥⲉⲙⲟⲩⲕϩ̅ ⲙ̅ⲙⲟⲕ.
“Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo.
26 ⲕ̅ⲋ̅ ⲙⲛ̅ⲛ̅ⲥⲁⲛⲁⲓ̈ ⲇⲉ ⲧⲏⲣⲟⲩ ⲟⲩⲛⲟⲩⲛⲟϭ ⲛ̅ⲭⲁⲥⲙⲁ ⲧⲁϫⲣⲏⲟⲩ ϩⲛⲧⲉⲛⲙⲏⲧⲉ ϩⲓⲟⲩⲥⲟⲡ ϫⲉⲕⲁⲥ ⲛⲉⲧⲟⲩⲱϣ ⲉϫⲓⲟⲟⲣ ⲙ̅ⲡⲉⲓ̈ⲙⲁ ϣⲁⲣⲱⲧⲛ̅ ⲛ̅ⲛⲉⲩⲉϣϭⲙ̅ϭⲟⲙ. ⲟⲩⲇⲉ ⲛ̅ⲛⲉⲩⲉϣϫⲓⲟⲟⲣ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲓⲧⲉⲧⲏⲟⲩⲧⲛ̅ ⲛⲁⲛ.
Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’
27 ⲕ̅ⲍ̅ ⲡⲉϫⲁϥ ⲇⲉ ϫⲉ ϯⲥⲟⲡⲥ̅ ⲛ̅ⲧⲟⲟⲩⲛ ⲙⲙⲟⲕ ⲡⲁⲓ̈ⲱⲧʾ ϫⲉ ⲉⲕⲉϫⲟⲟⲩϥ ⲉⲡⲏⲓ̈ ⲙ̅ⲡⲁⲓ̈ⲱⲧʾ
“Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga,
28 ⲕ̅ⲏ̅ ⲟⲩⲛ̅ϯϯⲟⲩ ⲅⲁⲣ ⲛ̅ⲥⲟⲛ ϫⲉ ⲉϥⲉⲣ̅ⲙⲛ̅ⲧⲣⲉ ⲛⲁⲩ ϫⲉ ⲛ̅ⲛⲉⲩⲉ͡ⲓ ϩⲱⲟⲩ ⲉⲡⲉⲓ̈ⲙⲁ ⲃ̅ⲃⲁⲥⲁⲛⲟⲥ.
pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’
29 ⲕ̅ⲑ̅ ⲡⲉϫⲉⲁⲃⲣⲁϩⲁⲙ ⲇⲉ ⲛⲁϥ ϫⲉ ⲟⲩⲛⲧⲟⲩⲙⲱⲩ̈ⲥⲏⲥ ⲙ̅ⲙⲁⲩ ⲛⲙ̅ⲛⲉⲡⲣⲟⲫⲏⲧⲏⲥ ⲙⲁⲣⲟⲩⲥⲱⲧⲙ̅ ⲛ̅ⲥⲱⲟⲩ.
“Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’
30 ⲗ̅ ⲛ̅ⲧⲟϥ ⲇⲉ ⲡⲉϫⲁϥ ϫⲉ ⲙ̅ⲙⲟⲛ ⲡⲓⲱⲧʾ ⲁⲃⲣⲁϩⲁⲙ. ⲁⲗⲗⲁ ⲉⲣϣⲁⲛⲟⲩⲁ ⲃⲱⲕ ϣⲁⲣⲟⲟⲩ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲛ̅ⲛⲉⲧⲙⲟⲟⲩⲧʾ ⲥⲉⲛⲁⲙⲉⲧⲁⲛⲟⲓ̈
“Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’
31 ⲗ̅ⲁ̅ ⲡⲉϫⲁϥ ⲇⲉ ⲛⲁϥ ϫⲉ. ⲉϣϫⲉⲛ̅ⲥⲉⲛⲁⲥⲱⲧⲙ̅ ⲁⲛ ⲛ̅ⲥⲁⲙⲱⲩ̈ⲥⲏⲥ ⲛⲙ̅ⲛⲉⲡⲣⲟⲫⲏⲧⲏⲥ. ⲉⲓ̈ⲉ ⲉⲣϣⲁⲛⲟⲩⲁ ⲟⲛ ⲧⲱⲟⲩⲛ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲛⲛⲉⲧⲙⲟⲟⲩⲧʾ. ⲛ̅ⲥⲉⲛⲁⲥⲱⲧⲙ̅ ⲛ̅ⲥⲱϥ ⲁⲛ·
“Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’”

< ⲖⲞⲨⲔⲞⲚ 16 >