< Zekariya 13 >

1 “Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.
In that dai an open welle schal be to the hous of Dauid, and to men dwellynge at Jerusalem, in to waischyng a wey of a synful man, and of womman defoulid in vnclene blood.
2 “Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa.
And it schal be, in that dai, seith the Lord of oostis, Y schal distrie names of idols fro `the lond, and thei schulen no more be `thouyt on; and Y schal take awei fro erthe false profetis, and an vnclene spirit.
3 Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.
And it schal be, whanne ony man schal profesie ouer, his fadir and modir that gendriden hym, schulen seie to hym, Thou schalt not lyue, for thou hast spoke leesyng in the name of the Lord; and his fadir and his modir, gendreris of hym, schulen `togidere fitche hym, whanne he hath profesied.
4 “Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu.
And it schal be, in that dai profetis schulen be confoundid, ech of his visioun, whanne he schal profesie; nether thei schulen be hilid with mentil of sak, that thei lie;
5 Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’
but `thei schulen seie, Y am not a profete; Y am a man `erthe tiliere, for Adam is myn ensaumple fro my yongthe.
6 Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’
And it schal be seid to hym, What ben these woundis in the myddil of thin hondis? And he schal seie, With these Y was woundid in the hous of hem that louyden me.
7 “Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga, ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Kantha mʼbusa ndipo nkhosa zidzabalalika, ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
Swerd, be thou reisid on my scheepherde, and on a man cleuynge to me, seith the Lord of oostis; smyte thou the scheepherde, and scheep of the floc schulen be scaterid. And Y schal turne myn hond to the litle.
8 Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse, “zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka; koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
And twei partis schulen be in ech lond, seith the Lord, and thei schulen be scaterid, and schulen faile, and the thridde part schal be left in it.
9 Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto; ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide. Adzayitana pa dzina langa ndipo Ine ndidzawayankha; Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’ ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’”
And Y schal lede the thridde part bi fier, and Y schal brenne hem, as siluer is brent, and Y schal preue hem, as gold is preuyd. He schal clepe to help my name, and Y schal graciously here him; and Y schal seie, Thou art my puple, and he schal seie, Thou art my Lord God.

< Zekariya 13 >