< Zekariya 12 >

1 Uthenga wa Yehova kwa Israeli. Yehova, amene amayala mlengalenga, amene amayika maziko a dziko lapansi, ndiponso amene amalenga mzimu wokhala mwa munthu, akunena kuti,
Breme rijeèi Gospodnje za Izrailja. Govori Gospod, koji je razapeo nebesa i osnovao zemlju, i stvorio èovjeku duh koji je u njemu:
2 “Taonani, ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala chakumwa choledzeretsa chimene chidzasokoneza mitundu yonse ya anthu yomuzungulira. Yuda adzazingidwa pamodzinso ndi Yerusalemu.
Evo, ja æu uèiniti Jerusalim èašom za opijanje svijem narodima unaokolo, koji æe opsjesti Jerusalim ratujuæi na Judu.
3 Pa tsiku limenelo, pamene mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi idzasonkhana kulimbana naye, ndidzasandutsa Yerusalemu thanthwe losatheka kusunthidwa ndi mitundu yonse ya anthu. Onse oyesa kumusuntha adzadzipweteka.
I u taj æu dan uèiniti Jerusalim teškim kamenom svijem narodima; koji ga god htjedbudu dignuti, satræe se, ako bi se i svi narodi zemaljski sabrali na nj.
4 Pa tsiku limenelo kavalo aliyense ndidzamuchititsa mantha kuti asokonezeke, ndipo wokwerapo wake ndidzamuchititsa misala,” akutero Yehova. “Ndidzayangʼanira nyumba ya Yuda koma ndidzachititsa khungu akavalo onse a anthu a mitundu ina.
U taj æu dan, govori Gospod, uèiniti da svi konji budu plašljivi i svi konjanici bezumni; i otvoriæu oèi svoje na dom Judin, i oslijepiæu sve konje narodima.
5 Pamenepo atsogoleri a Yuda adzayankhula mʼmitima mwawo kuti, ‘Anthu a ku Yerusalemu ndi amphamvu, chifukwa Yehova Wamphamvuzonse ndiye Mulungu wawo.’
Te æe govoriti glavari Judini u srcu svom: jaki su mi stanovnici Jerusalimski Gospodom nad vojskama, Bogom svojim.
6 “Pa tsiku limenelo ndidzasandutsa atsogoleri a Yuda kukhala ngati mbawula yotentha pakati pa nkhuni, ngati sakali yoyaka pa mitolo ya tirigu. Adzatentha mitundu yonse ya anthu yowazungulira, kumanja ndi kumanzere, koma Yerusalemu sadzasuntha pa malo ake.
U onaj æu dan uèiniti da glavari Judini budu kao ognjište u drvima i kao luè zapaljen u snopovima, te æe proždrijeti i nadesno i nalijevo sve narode unaokolo, a Jerusalim æe još ostati na svom mjestu, u Jerusalimu.
7 “Yehova adzapulumutsa malo okhala Yuda poyamba, kuti ulemu wa nyumba ya Davide ndi wa anthu okhala mu Yerusalemu usapambane ulemu wa Yuda.
I Gospod æe saèuvati šatore Judine najprije, da se ne diže nad Judom slava doma Davidova i slava stanovnika Jerusalimskih.
8 Pa tsiku limenelo Yehova adzatchinjiriza onse okhala mu Yerusalemu, kotero kuti anthu ofowoka kwambiri pakati pawo adzakhala ngati Davide, ndipo nyumba ya Davide idzakhala ngati Mulungu, ngati mngelo wa Yehova wowatsogolera.
U onaj æe dan Gospod zaklanjati stanovnike Jerusalimske, i najslabiji meðu njima biæe u taj dan kao David, i dom æe Davidov biti kao Bog, kao anðeo Gospodnji pred njima.
9 Pa tsiku limenelo ndidzawononga mitundu yonse yofuna kuthira nkhondo Yerusalemu.
I u taj dan tražiæu da istrijebim sve narode koji doðu na Jerusalim;
10 “Ndipo pa nyumba ya Davide ndi pa anthu okhala mu Yerusalemu ndidzakhuthulirapo mzimu wachisomo ndi wopemphera. Iwo adzandiyangʼana Ine, amene anamubaya, ndipo adzamulirira kwambiri monga momwe munthu amalirira mwana wake mmodzi yekhayo, ndiponso adzamva chisoni kwambiri monga momwe amachitira ndi mwana woyamba kubadwa.
I izliæu na dom Davidov i na stanovnike Jerusalimske duh milosti i molitava, i pogledaæe na mene kojega probodoše; i plakaæe za njim kao za jedincem, i tužiæe za njim kao za prvencem.
11 Pa tsiku limenelo mudzakhala kulira kwakukulu mu Yerusalemu, monga kulira kwa ku Hadadi-Rimoni ku chigwa cha Megido.
U ono æe vrijeme biti tužnjava velika u Jerusalimu kao tužnjava u Adadrimonu u polju Megidonskom.
12 Dziko lidzalira kwambiri, fuko lililonse pa lokha, akazi awo pa okhanso: fuko la Davide pamodzi ndi akazi awo, fuko la Natani pamodzi ndi akazi awo,
I tužiæe zemlja, svaka porodica napose; porodica doma Davidova napose, i žene njihove napose; porodica doma Natanova napose, i žene njihove napose;
13 nyumba ya Levi pamodzi ndi akazi awo, fuko la Simei pamodzi ndi akazi awo,
Porodica doma Levijeva napose, i žene njihove napose; porodica Semejeva napose, i žene njihove napose;
14 ndiponso mafuko onse pamodzi ndi akazi awo.
Sve ostale porodice, svaka napose, i žene njihove napose.

< Zekariya 12 >