< Malaki 1 >

1 Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
Breme rijeèi Gospodnje Izrailju preko Malahije.
2 Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
Ljubim vas, veli Gospod; a vi govorite: u èem nas ljubiš? Ne bješe li Isav brat Jakovu? govori Gospod; ali Jakova ljubih.
3 koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
A na Isava mrzih; zato gore njegove opustih i našljedstvo njegovo dadoh zmajevima iz pustinje.
4 Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
Što Edom govori: osiromašismo, ali æemo se povratiti i sagraditi pusta mjesta, ovako veli Gospod nad vojskama: neka oni grade, ali æu ja razgraditi, i oni æe se zvati: krajina bezakonièka i narod na koji se gnjevi Gospod dovijeka.
5 Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
I oèi æe vaše vidjeti i vi æete reæi: velik je Gospod na meðama Izrailjevijem.
6 “Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
Sin poštuje oca i sluga gospodara svojega; ako sam ja otac, gdje je èast moja? i ako sam gospodar, gdje je strah moj? veli Gospod nad vojskama vama, sveštenici, koji prezirete ime moje, i govorite: u èem preziremo ime tvoje?
7 “Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
Donosite na moj oltar hljeb oskvrnjen, i govorite: èim te oskvrnismo? Tijem što govorite: sto je Gospodnji za preziranje.
8 Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
I kad donosite slijepo na žrtvu, nije li zlo? i kad donosite hromo ili bolesno, nije li zlo? odnesi ga starješini svojemu, hoæeš li mu ugoditi i hoæe li pogledati na te? veli Gospod nad vojskama.
9 “Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Zato, molite se Bogu da se smiluje na nas; kad je to iz vaših ruku, hoæe li na koga od vas gledati? govori Gospod nad vojskama.
10 “Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
Ko je meðu vama koji bi zatvorio vrata ili zapalio oganj na mom oltaru ni za što? Nijeste mi mili, veli Gospod nad vojskama, i neæu primiti dara iz vaše ruke.
11 Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Jer od istoka sunèanoga do zapada veliko æe biti ime moje meðu narodima, i na svakom æe se mjestu prinositi kad imenu mojemu i èist dar; jer æe ime moje biti veliko meðu narodima, veli Gospod nad vojskama.
12 “Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
A vi ga skvrnite govoreæi: sto je Gospodnji neèist, i što se postavlja na nj, jelo je za preziranje.
13 Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
I govorite: gle, kolika muka! a moglo bi se oduhnuti, govori Gospod nad vojskama; i donosite oteto, i hromo i bolesno donosite na dar; eda li æu primiti iz ruke vaše? govori Gospod.
14 “Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”
Proklet da je varalica, koji ima u svom stadu muško i zavjetuje, pa prinosi Gospodu kvarno; jer sam velik car, veli Gospod nad vojskama, i ime je moje strašno meðu narodima.

< Malaki 1 >