< Masalimo 95 >

1 Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe, tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
Hodite, zapjevajmo Gospodu, pokliknimo Bogu, gradu spasenja svojega!
2 Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
Izaðimo pred lice njegovo s hvalom, u pjesmama pokliknimo mu!
3 Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu, mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
Jer je Gospod velik Bog i velik car nad svijem bogovima.
4 Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi, ndipo msonga za mapiri ndi zake.
U njegovoj su ruci dubine zemaljske, i visine gorske njegove su.
5 Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye, ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
Njegovo je more i on ga je stvorio, i suhotu ruke su njegove naèinile.
6 Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira, tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
Hodite, poklonimo se, pripadnimo, kleknimo pred Gospodom tvorcem svojim.
7 pakuti Iye ndiye Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za mʼdzanja lake. Lero ngati inu mumva mawu ake,
Jer je on Bog naš, i mi narod paše njegove i ovce ruke njegove. Sad kad biste poslušali glas njegov:
8 musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba, monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
“Nemojte da vam odrveni srce vaše kao u Merivi, kao u dan kušanja u pustinji,
9 Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa, ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
Gdje me kušaše oci vaši, ispitaše i vidješe djelo moje.
10 Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo; ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera ndipo sanadziwe njira zanga.”
Èetrdeset godina srdih se na rod onaj, i rekoh: ovi ljudi tumaraju srcem, i ne znaju putova mojih;
11 Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti, “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”
I zato se zakleh u gnjevu svom da neæe uæi u mir moj.”

< Masalimo 95 >