< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
Bože od osvete, Gospode, Bože od osvete, pokaži se!
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Podigni se, sudijo zemaljski, podaj zaslugu oholima.
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
Dokle æe se bezbožnici, Gospode, dokle æe se bezbožnici hvaliti?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
Ruže i oholo govore, velièaju se svi koji èine bezakonje.
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
Gaze narod tvoj, Gospode, i dostojanje tvoje muèe.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
Udovicu i došljaka ubijaju, i sirote more.
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
I govore: neæe vidjeti Gospod, i neæe doznati Bog Jakovljev.
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Orazumite se, preludi ljudi! budale! kad æete biti pametni?
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
Koji je stvorio uho, zar ne èuje? i koji je oko naèinio, zar ne vidi?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
Zar neæe oblièiti koji narode urazumljuje, koji uèi èovjeka da zna?
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
Gospod zna misli ljudima kako su ništave.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Blago èovjeku koga ti, Gospode, urazumljuješ, i zakonom svojim uèiš;
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
Da bi mu dao mir u zle dane, dok se iskopa jama bezbožniku.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
Jer neæe odbaciti Gospod naroda svojega, i dostojanja svojega neæe ostaviti.
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
Jer æe se sud vratiti na pravdu, i njega æe naæi svi prava srca.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Ko æe ustati za mene suprot zlima? ko æe stati za mene suprot onima koji èine bezakonje?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Kad mi Gospod ne bi bio pomoænik, brzo bi se duša moja preselila onamo gdje se muèi.
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
Kad reèem: drkæe mi noga, milost tvoja, Gospode, prihvata me.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
Kad se umnože brige u srcu mom, utjehe tvoje razgovaraju dušu moju.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Eda li æe blizu tebe stati prijesto krvnièki, i onaj koji namišlja nasilje nasuprot zakonu?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
Spremaju se na dušu pravednikovu, i krv pravu okrivljuju.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
Ali je Gospod moje pristanište, i Bog je moj tvrdo utoèište moje.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
On æe im vratiti za bezakonje njihovo, za njihovu zloæu istrijebiæe ih, istrijebiæe ih Gospod, Bog naš.

< Masalimo 94 >