< Masalimo 67 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
Bože, budi nam milostiv i blagosiljaj nas, obasjavaj nas licem svojim,
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
Da bi se znao na zemlji put tvoj, po svima narodima spasenje tvoje.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Da te slave narodi, Bože, da te slave svi narodi!
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Da se vesele i raduju plemena; jer sudiš narodima pravo, i plemenima na zemlji upravljaš.
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Da te slave narodi, Bože, da te slave svi narodi!
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
Zemlja dade plod svoj. Da nas blagosilja Bog, Bog naš!
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
Da nas blagosilja Bog, i da ga se boje svi krajevi zemaljski!

< Masalimo 67 >