< Masalimo 59 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
`In Jeroms translacioun thus, To the ouercomer, that thou lese not Dauid, meke and simple, `whanne Saul sente and kepte the hous, to slee hym. `In Ebreu thus, To the ouercomyng, leese thou not the semeli song of Dauid, and so forth. Mi God, delyuer thou me fro myn enemyes; and delyuer thou me fro hem that risen ayens me.
2 Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
Delyuer thou me fro hem that worchen wickidnesse; and saue thou me fro menquelleris.
3 Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
For lo! thei han take my soule; stronge men fellen in on me.
4 Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
Nethir my wickidnesse, nether my synne; Lord, Y ran with out wickidnesse, and dresside `my werkis.
5 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
Rise vp thou in to my meetyng, and se; and thou, Lord God of vertues, art God of Israel. Yyue thou tent to visite alle folkis; do thou not merci to alle that worchen wickidnesse.
6 Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
Thei schulen be turned at euentid, and thei as doggis schulen suffre hungir; and thei schulen cumpas the citee.
7 Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
Lo! thei schulen speke in her mouth, and a swerd in her lippis; for who herde?
8 Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
And thou, Lord, schalt scorne hem; thou schalt bringe alle folkis to nouyt.
9 Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
I schal kepe my strengthe to thee;
10 Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
for God is myn vptaker, my God, his mercy schal come byfore me.
11 Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
God schewide to me on myn enemyes, slee thou not hem; lest ony tyme my puples foryete. Scatere thou hem in thi vertu; and, Lord, my defender, putte thou hem doun.
12 Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
Putte thou doun the trespas of her mouth, and the word of her lippis; and be thei takun in her pride. And of cursyng and of leesyng; thei schulen be schewid in the endyng.
13 muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
In the ire of ending, and thei schulen not be; and thei schulen wite, that the Lord schal be Lord of Jacob, and of the endis of erthe.
14 Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
Thei schulen be turned at euentid, and thei as doggis schulen suffre hungur; and thei schulen cumpas the citee.
15 Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
Thei schulen be scaterid abrood, for to eete; sotheli if thei ben not fillid, and thei schulen grutche.
16 Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
But Y schal synge thi strengthe; and eerli Y schal enhaunse thi merci. For thou art maad myn vptaker; and my refuyt, in the dai of my tribulacioun.
17 Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.
Myn helper, Y schal synge to thee; for thou art God, myn vptaker, my God, my mercy.

< Masalimo 59 >