< Masalimo 53 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
Reèe bezumnik u srcu svojemu: nema Boga; pronevaljališe se i zagrdješe u bezakonju, nema nikoga dobro da tvori.
2 Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
Bog s neba pogleda na sinove èovjeèije da vidi ima li koji razuman, i traži li koji Boga.
3 Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
Svi zastraniše, svi se pokvariše, nema nikoga dobro da tvori, nema ni jednoga.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
Zar neæe da se orazume koji god èine bezakonje, jedu narod moj kao što jedu hljeb, i ne prizivaju Boga?
5 Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
Drktaæe od straha gdje straha nema. Jer æe Bog rasuti kosti onijeh koji ustaju na tebe. Ti æeš ih posramiti, jer ih Bog odvrže.
6 Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!
Ko æe poslati sa Siona spasenje Izrailju? Kad Bog povrati zarobljeni narod svoj, radovaæe se Jakov, veseliæe se Izrailj.

< Masalimo 53 >