< Masalimo 51 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
Smiluj se na me, Bože, po milosti svojoj, i po velikoj dobroti svojoj oèisti bezakonje moje.
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
Operi me dobro od bezakonja mojega, i od grijeha mojega oèisti me.
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
Jer ja znam prijestupe svoje, i grijeh je moj jednako preda mnom.
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
Samome tebi zgriješih, i na tvoje oèi zlo uèinih, a ti si pravedan u rijeèima svojim i èist u sudu svojem.
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
Gle, u bezakonju rodih se, i u grijehu zatrudnje mati moja mnom.
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
Gle, istinu ljubiš u srcu, i iznutra javljaš mi mudrost.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
Pokropi me isopom, i oèistiæu se; umij me, i biæu bjelji od snijega.
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
Daj mi da slušam radost i veselje, da se prenu kosti koje si potro.
9 Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
Odvrati lice svoje od grijeha mojih, i sva bezakonja moja oèisti.
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
Uèini mi, Bože, èisto srce, i duh prav ponovi u meni.
11 Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
Nemoj me odvrgnuti od lica svojega, i svetoga duha svojega nemoj uzeti od mene.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
Vrati mi radost spasenja svojega, i duh vladalaèki neka me potkrijepi.
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
Nauèiæu bezakonike putovima tvojim, i grješnici k tebi æe se obratiti.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
Izbavi me od krvi, Bože, Bože, spasitelju moj, i jezik æe moj glasiti pravdu tvoju.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
Gospode! otvori usta moja, i ona æe kazati hvalu tvoju.
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
Jer žrtve neæeš: ja bih je prinio; za žrtve paljenice ne mariš.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
Žrtva je Bogu duh skrušen, srca skrušena i poništena ne odbacuješ, Bože.
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
Po dobroti svojoj, Gospode, èini dobro Sionu, podigni zidove Jerusalimske.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
Onda æe ti biti mile žrtve pravde, prinosi i žrtve paljenice; onda æe metati na žrtvenik tvoj teoce.

< Masalimo 51 >