< Masalimo 32 >

1 Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
Blago onome, kojemu je oproštena krivica, kojemu je grijeh pokriven.
2 Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
Blago èovjeku, kojemu Gospod ne prima grijeha i u èijem duhu nema lukavstva.
3 Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
Kad muèah, posahnuše kosti moje od uzdisanja mojega po vas dan.
4 Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
Jer dan i noæ tištaše me ruka tvoja; nesta soka u meni kao na ljetnoj pripeci.
5 Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
Grijeh svoj kazah tebi, i krivice svoje ne zatajih; rekoh: ispovijedam Gospodu prijestupe svoje; i ti skide s mene krivicu grijeha mojega.
6 Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
Zato neka ti se moli svaki svetac, kad se možeš naæi; i onda potop velike vode neæe ga stignuti.
7 Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
Ti si zaklon moj, ti me èuvaš od tjeskobe; okružavaš me radostima u izbavljanju.
8 Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
Urazumiæu te, i pokazaæu ti put kojim da ideš; svjetovaæu te, oko je moje na tebi.
9 Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
Nemojte biti kao konj, kao mazga bez razuma, kojima uzdom i žvalama valja obuzdati gubicu, kad ne idu k tebi.
10 Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
Mnogo muke ima bezbožnik, a koji se uzda u Gospoda, oko njega je milost.
11 Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!
Radujte se o Gospodu, i pjevajte, pravednici; veselite se svi koji ste prava srca.

< Masalimo 32 >