< Masalimo 28 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
To Dauid. Lord, Y schal crye to thee; my God, be thou not stille fro me, be thou not stille `ony tyme fro me; and Y schal be maad lijk to hem, that goen doun in to the lake.
2 Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
Lord, here thou the vois of my bisechyng, while Y preie to thee; whyle Y reise myn hondis to thin hooli temple.
3 Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
Bitake thou not me togidere with synneris; and leese thou not me with hem that worchen wickidnesse. Whyche speken pees with her neiybore; but yuels ben in her hertis.
4 Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
Yyue thou to hem vpe the werkis of hem; and vpe the wickidnesse of her fyndyngis. Yyue thou to hem vpe the werkis of her hondis; yelde thou her yeldyng to hem.
5 Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
For thei vndurstoden not the werkis of the Lord, and bi the werkis of hise hondis thou schalt destrie hem; and thou schalt not bilde hem.
6 Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
Blissid be the Lord; for he herde the vois of my bisechyng.
7 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
The Lord is myn helpere and my defendere; and myn herte hopide in hym, and Y am helpid. And my fleisch flouride ayen; and of my wille Y schal knowleche to hym.
8 Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
The Lord is the strengthe of his puple; and he is defendere of the sauyngis of his crist.
9 Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.
Lord, make thou saaf thi puple, and blesse thou thin eritage; and reule thou hem, and enhaunse thou hem til in to with outen ende.

< Masalimo 28 >