< Masalimo 27 >

1 Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
To Dauid. The Lord is my liytnyng, and myn helthe; whom schal Y drede? The Lord is defendere of my lijf; for whom schal Y tremble?
2 Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
The while noiful men neiyen on me; for to ete my fleischis. Myn enemyes, that trobliden me; thei weren maad sijk and felden doun.
3 Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
Thouy castels stonden togidere ayens me; myn herte schal not drede. Thouy batel risith ayens me; in this thing Y schal haue hope.
4 Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
I axide of the Lord o thing; Y schal seke this thing; that Y dwelle in the hows of the Lord alle the daies of my lijf. That Y se the wille of the Lord; and that Y visite his temple.
5 Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
For he hidde me in his tabernacle in the dai of yuelis; he defendide me in the hid place of his tabernacle.
6 Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
He enhaunside me in a stoon; and now he enhaunside myn heed ouer myn enemyes. I cumpasside, and offride in his tabernacle a sacrifice of criyng; Y schal synge, and Y schal seie salm to the Lord.
7 Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
Lord, here thou my vois, bi which Y criede to thee; haue thou merci on me, and here me.
8 Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
Myn herte seide to thee, My face souyte thee; Lord, Y schal seke eft thi face.
9 Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
Turne thou not awei thi face fro me; bouwe thou not awei in ire fro thi seruaunt. Lord, be thou myn helpere, forsake thou not me; and, God, myn helthe, dispise thou not me.
10 Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
For my fadir and my modir han forsake me; but the Lord hath take me.
11 Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
Lord, sette thou a lawe to me in thi weie; and dresse thou me in thi path for myn enemyes.
12 Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
Bitake thou not me in to the soules of hem, that troblen me; for wickid witnessis han rise ayens me, and wickydnesse liede to it silf.
13 Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
I bileue to see the goodis of the Lord; in the lond of `hem that lyuen.
14 Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.
Abide thou the Lord, do thou manli; and thin herte be coumfortid, and suffre thou the Lord.

< Masalimo 27 >