< Masalimo 27 >

1 Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
Gospod je vidjelo moje i spasenje moje; koga da se bojim? Gospod je krjepost života mojega; koga da se strašim?
2 Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
Ako navale na me zlikovci da pojedu tijelo moje, protivnici i neprijatelji moji, spotaæi æe se i pašæe.
3 Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
Ako protiv mene vojska u oko stane, neæe se uplašiti srce moje; ako se na me rat digne, ja se ni onda neæu bojati.
4 Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
Za jedno samo molim Gospoda, samo to ištem, da živim u domu Gospodnjem sve dane života svojega, da gledam krasotu Gospodnju i ranim u crkvu njegovu.
5 Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
Jer bi me sakrio u kolibi svojoj u zlo doba; sklonio bi me pod krovom šatora svojega; na kamenu goru popeo bi me.
6 Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
Tada bih podigao glavu svoju pred neprijateljima koji bi me opkolili; prinio bih u njegovu šatoru žrtvu hvale; zapjevao bih i hvalio Gospoda.
7 Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
Èuj, Gospode, glas moj, tebe prizivljem, smiluj se na me i usliši me.
8 Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
Srce moje govori pred tobom što si rekao: “tražite lice moje”; tražim lice tvoje, Gospode!
9 Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
Nemoj odvratiti od mene lica svojega, nemoj u gnjevu ostaviti sluge svojega; budi pomoænik moj; nemoj me odbiti, i nemoj me ostaviti, Bože, spasitelju moj!
10 Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
Jer otac moj i mati moja ostaviše me; ali Gospod neka me prihvati.
11 Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
Uputi me, Gospode, na put svoj i vodi me pravom stazom poradi onijeh koji me vrebaju.
12 Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
Nemoj me dati na volju neprijateljima mojim; jer ustaše na me lažni svjedoci; ali zloba govori sama protiv sebe.
13 Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Vjerujem da æu vidjeti dobrotu Gospodnju na zemlji živijeh.
14 Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.
Uzdaj se u Gospoda, budi slobodan; neka bude srce tvoje krjepko, uzdaj se u Gospoda.

< Masalimo 27 >