< Masalimo 147 >

1 Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
Hvalite Gospoda, jer je slatko pjevati Boga našega, jer blagome prilikuje hvala.
2 Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
Gospod zida Jerusalim, sabira rasijane sinove Izrailjeve;
3 Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
Iscjeljuje one koji su skrušena srca, i lijeèi tuge njihove;
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
Izbraja mnoštvo zvijezda, i sve ih zove imenom.
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
Velik je Gospod naš i velika je krjepost njegova, i razumu njegovu nema mjere.
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
Prihvata smjerne Gospod, a bezbožne ponižava do zemlje.
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
Redom pjevajte Gospodu hvalu, udarajte Bogu našemu u gusle.
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
On zastire nebo oblacima, sprema zemlji dažd, èini te raste na gorama trava;
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
Daje stoci piæu njezinu, i vraniæima, koji vièu k njemu.
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
Ne mari za silu konjsku, niti su mu mili kraci èovjeèiji.
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
Mili su Gospodu oni koji ga se boje, koji se uzdaju u milost njegovu.
12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
Slavi, Jerusalime, Gospoda; hvali Boga svojega, Sione!
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
Jer on utvrðuje prijevornice vrata tvojih, blagosilja sinove tvoje u tebi.
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
Ograðuje meðe tvoje mirom, nasiæava te jedre pšenice.
15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
Šalje govor svoj na zemlju, brzo teèe rijeè njegova.
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
Daje snijeg kao vunu, sipa inje kao pepeo.
17 Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
Baca grad svoj kao zalogaje, pred mrazom njegovijem ko æe ostati?
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
Pošlje rijeè svoju, i sve se raskravi; dune duhom svojim, i poteku vode.
19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
On je javio rijeè svoju Jakovu, naredbe i sudove svoje Izrailju.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.
Ovo nije uèinio nijednome drugom narodu, i sudova njegovijeh oni ne znaju. Aliluja!

< Masalimo 147 >