< Masalimo 143 >

1 Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
Gospode, usliši molitvu moju, primi moljenje moje po istini svojoj, usliši me po pravdi svojoj.
2 Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
I ne idi na sud sa slugom svojim, jer se neæe opravdati pred tobom niko živ.
3 Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
Neprijatelj goni dušu moju, gazi u prah život moj, posaðuje me u mrak, kao davno pomrle.
4 Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
Trne u meni duh moj, nestaje u meni srca mojega.
5 Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
Pominjem dane stare, prebrajam sve poslove tvoje, razmišljam o djelima ruku tvojih.
6 Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
Pružam k tebi ruke svoje; duša je moja kao suha zemlja pred tobom.
7 Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
Pohitaj, usliši me; Gospode, nestaje duha mojega, nemoj odvratiti lica svojega od mene; jer æu biti kao oni koji odlaze u grob.
8 Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
Rano mi javi milost svoju, jer se u tebe uzdam. Pokaži mi put, kojim da idem, jer k tebi podižem dušu svoju.
9 Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
Izbavi me od neprijatelja mojih, Gospode, k tebi pritjeèem.
10 Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
Nauèi me tvoriti volju tvoju, jer si ti Bog moj; duh tvoj blagi neka me vodi po stazi pravoj.
11 Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
Imena radi svojega, Gospode, oživi me, po pravdi svojoj izvedi iz muke dušu moju.
12 Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.
I po milosti svojoj istrijebi neprijatelje moje, i pogubi sve koji muèe dušu moju, jer sam tvoj sluga.

< Masalimo 143 >