< Masalimo 142 >

1 Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero. Ndikulirira Yehova mofuwula; ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.
Glasom svojim ka Gospodu vièem, glasom svojim Gospodu se molim.
2 Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake; ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.
Izlivam pred njim moljenje svoje, tugu svoju pred njim kazujem,
3 Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga, ndinu amene mudziwa njira yanga. Mʼnjira imene ndimayendamo anthu anditchera msampha mobisa.
Kad iznemogne u meni duh moj. Ti znaš stazu moju. Na putu, kojim hodim, sakriše mi zamku.
4 Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani; palibe amene akukhudzika nane. Ndilibe pothawira; palibe amene amasamala za moyo wanga.
Pogledam nadesno, i vidim da me niko ne zna; nestade mi utoèišta, niko ne mari za dušu moju.
5 Ndilirira Inu Yehova; ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga, gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”
Vièem k tebi, Gospode; velim: ti si utoèište moje, dio moj na zemlji živijeh.
6 Mverani kulira kwanga pakuti ndathedwa nzeru; pulumutseni kwa amene akundithamangitsa pakuti ndi amphamvu kuposa ine.
Èuj tužnjavu moju; jer se muèim veoma. Izbavi me od onijeh koji me gone, jer su jaèi od mene.
7 Tulutseni mʼndende yanga kuti nditamande dzina lanu. Ndipo anthu olungama adzandizungulira chifukwa cha zabwino zanu pa ine.
Izvedi iz tamnice dušu moju, da slavim ime tvoje. Oko mene æe se skupiti pravednici, kad mi uèiniš dobro.

< Masalimo 142 >