< Masalimo 14 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa; palibe amene amachita zabwino.
Reèe bezumnik u srcu svojem: nema Boga; nevaljali su, gadna su djela njihova; nema nikoga dobro da tvori.
2 Yehova kumwamba wayangʼana pansi, kuyangʼana anthu onse kuti aone ngati alipo wina wanzeru, amene amafunafuna Mulungu.
Gospod pogleda s neba na sinove èovjeèije, da vidi ima li koji razuman, traži li koji Boga.
3 Onse atembenukira kumbali, onse pamodzi asanduka oyipa; palibe amene amachita zabwino, palibiretu ndi mmodzi yemwe.
Svi su zašli, svi se pokvarili, nema nikoga dobro da tvori, nema nijednoga.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse? Akudya anthu anga ngati chakudya chawo ndipo satamanda Yehova?
Zar se neæe opametiti koji èine bezakonje, jedu narod moj kao što jedu hljeb, ne prizivaju Gospoda?
5 Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu, pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
Ondje æe zadrhtati od straha; jer je Gospod u rodu pravednom.
6 Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka, koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
Smijete se onome što ubogi radi; ali Gospod njega zaklanja.
7 Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni! Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake, Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!
Ko æe poslati sa Siona pomoæ Izrailju? Kad Gospod povrati zarobljeni narod svoj, onda æe se radovati Jakov i veseliæe se Izrailj.

< Masalimo 14 >