< Masalimo 138 >

1 Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
Slavim te, Gospode, od svega srca svojega, pred bogovima pjevam tebi.
2 Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
Poklanjam se pred svetom crkvom tvojom, i slavim ime tvoje, za dobrotu tvoju i za istinu tvoju; jer si po svakom imenu svom podigao rijeè svoju.
3 Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
U dan, u koji zazvah, ti si me uslišio, dunuo slobodu u dušu moju.
4 Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
Slaviæe te, Gospode, svi carevi zemaljski, kad èuju rijeèi usta tvojih;
5 Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
I pjevaæe putove Gospodnje, jer je velika slava Gospodnja.
6 Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
Jer je visok Gospod, i vidi niskoga, i visokoga izdaleka poznaje.
7 Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
Ako poðem u tuzi, ti æeš me oživiti; na zloæu neprijatelja mojih pružiæeš ruku svoju i zakloniæe me desnica tvoja.
8 Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.
Gospod æe svršiti za mene. Gospode! milost je tvoja dovijeka; djela ruku svojih ne ostavljaj.

< Masalimo 138 >