< Masalimo 137 >

1 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
Na vodama Vavilonskim sjeðasmo i plakasmo opominjuæi se Siona.
2 Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
O vrbama sred njega vješasmo harfe svoje.
3 pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
Ondje iskahu koji nas zarobiše da pjevamo, i koji nas oboriše da se veselimo: “pjevajte nam pjesmu Sionsku.”
4 Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
Kako æemo pjevati pjesmu Gospodnju u zemlji tuðoj?
5 Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
Ako zaboravim tebe, Jerusalime, neka me zaboravi desnica moja.
6 Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
Neka prione jezik moj za usta moja, ako tebe ne uspamtim, ako ne uzdržim Jerusalima svrh veselja svojega.
7 Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
Napomeni, Gospode, sinovima Edomovijem dan Jerusalimski, kad govoriše: raskopajte, raskopajte ga do temelja.
8 Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
Kæeri Vavilonska, krvnico, blago onome ko ti plati za djelo koje si nama uèinila!
9 Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
Blago onome koji uzme i razbije djecu tvoju o kamen.

< Masalimo 137 >