< Masalimo 121 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
Podižem oèi svoje ka gorama, odakle mi dolazi pomoæ.
2 Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Pomoæ je meni od Gospoda, koji je stvorio nebo i zemlju.
3 Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
Neæe dati da popuzne noga tvoja; ne drijemlje èuvar tvoj.
4 Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
Gle, ne drijemlje i ne spava èuvar Izrailjev.
5 Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
Gospod je èuvar tvoj, Gospod je sjen tvoj, on ti je s desne strane.
6 Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
Danju te neæe sunce ubiti ni mjesec noæu.
7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
Gospod æe te saèuvati od svakoga zla, saèuvaæe dušu tvoju Gospod.
8 Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Gospod æe èuvati ulazak tvoj i izlazak tvoj, otsad i dovijeka.

< Masalimo 121 >