< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Blago onima kojima je put èist, koji hode u zakonu Gospodnjem.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Blago onima koji èuvaju otkrivenja njegova, svijem srcem traže ga;
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Koji ne èine bezakonja, hode putovima njegovijem!
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Ti si dao zapovijesti svoje, da se èuvaju dobro.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Kad bi putovi moji bili upravljeni da èuvam naredbe tvoje!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Onda se ne bih postidio, pazeæi na zapovijesti tvoje;
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Hvalio bih te s pravijem srcem, uèeæi se pravednijem zakonima tvojim.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Èuvaæu naredbe tvoje, nemoj me ostaviti sasvijem.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Kako æe mladiæ oèistiti put svoj? Vladajuæi se po tvojim rijeèima.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Svijem srcem svojim tražim tebe, ne daj mi da zaðem od zapovijesti tvojih.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
U srce svoje zatvorio sam rijeè tvoju, da ti ne griješim.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Blagosloven si, Gospode! nauèi me naredbama svojim.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Ustima svojim javljam sve sudove usta tvojih.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Na putu otkrivenja tvojih radujem se kao za veliko bogatstvo.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
O zapovijestima tvojim razmišljam, i pazim na putove tvoje.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Naredbama tvojim tješim se, ne zaboravljam rijeèi tvoje.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Uèini milost sluzi svojemu, da bih živio i èuvao rijeè tvoju.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Otvori oèi moje, da bih vidio èudesa zakona tvojega;
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Gost sam na zemlji, nemoj sakriti od mene zapovijesti svojih.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Iznemože duša moja želeæi bez prestanka poznati sudove tvoje.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Ti si strašan prokletim oholicama, koje zastranjuju od zapovijesti tvojih.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Odvrati od mene rug i sramotu, jer èuvam otkrivenja tvoja.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Sjede knezovi i dogovaraju se na mene; a sluga tvoj razmišlja o naredbama tvojim.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Otkrivenja su tvoja utjeha moja, savjetnici moji.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Duša moja leži u prahu; oživi me po rijeèi svojoj.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Kazujem putove svoje, i èuješ me; nauèi me naredbama svojim.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Urazumi me o putu zapovijesti svojih, i razmišljaæu o èudesima tvojim.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Suze proliva duša moja od tuge, okrijepi me po rijeèi svojoj.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Put lažni ukloni od mene i zakon svoj daruj mi.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Put istini izbrah, zakone tvoje tražim.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Prionuh za otkrivenja tvoja, Gospode; nemoj me osramotiti.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Putem zapovijesti tvojih trèim, jer si raširio srce moje.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Pokaži mi, Gospode, put naredaba svojih, da ga se držim do kraja.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Urazumi me, i držaæu se zakona tvojega, i èuvati ga svijem srcem.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Postavi me na stazu zapovijesti svojih, jer mi je ona omiljela.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Privij srce moje k otkrivenjima svojim, a ne k lakomstvu.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Odvrati oèi moje da ne gledaju ništavila, putem svojim oživi me.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Ispuni sluzi svojemu rijeè svoju da te se boji.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Ukloni rug moj, kojega se plašim; jer su sudovi tvoji blagi.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Mile su mi zapovijesti tvoje, pravdom svojom oživi me.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Neka doðe na me milost tvoja, Gospode, pomoæ tvoja po rijeèi tvojoj.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
I ja æu odgovoriti onome koji me ruži; jer se uzdam u rijeè tvoju.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Nemoj uzeti nigda od usta mojih rijeèi istine, jer èekam sudove tvoje.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
I èuvaæu zakon tvoj svagda, dovijeka i bez prestanka.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Hodiæu slobodno, jer tražim zapovijesti tvoje.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Govoriæu o otkrivenjima tvojim pred carevima, i neæu se stidjeti.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Tješiæu se zapovijestima tvojim, koje ljubim.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Ruke svoje pružam k zapovijestima tvojim, koje ljubim, i razmišljam o naredbama tvojim.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Opomeni se rijeèi svoje k sluzi svojemu, na koju si mi zapovjedio da se oslanjam.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
U nevolji mojoj tješi me što me rijeè tvoja oživljava.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Oholi mi se rugaju veoma; ali ja ne otstupam od zakona tvojega.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Pamtim sudove tvoje od iskona, Gospode, i tješim se.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Gnjev me obuzima na bezbožnike, koji ostavljaju zakon tvoj.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Naredbe su tvoje pjesma moja u putnièkom stanu mojem.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Noæu pominjem ime tvoje, Gospode, i èuvam zakon tvoj.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
To je moje, da èuvam zapovijesti tvoje.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Dio moj ti si, Gospode; naumio sam èuvati rijeèi tvoje.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Molim ti se iz svega srca, smiluj se na me po rijeèi svojoj.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Razmatram putove svoje, i obraæam noge svoje k otkrivenjima tvojim.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Hitim, i ne zatežem se èuvati zapovijesti tvoje.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Mreže bezbožnièke opkoliše me, ali zakona tvojega ne zaboravljam.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
U po noæi ustajem da te slavim za pravedne sudove tvoje.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
U zajednici sam sa svima koji se tebe boje i koji èuvaju zapovijesti tvoje.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Dobrote je tvoje, Gospode, puna sva zemlja; naredbama svojim nauèi me.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Uèinio si dobro sluzi svojemu, Gospode, po rijeèi svojoj.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Dobroj misli i znanju nauèi me, jer zapovijestima tvojim vjerujem.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Prije stradanja svojega lutah, a sad èuvam rijeè tvoju.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Ti si dobar, i dobro èiniš; nauèi me naredbama svojim.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Oholi pletu na mene laž, ali se ja svijem srcem držim zapovijesti tvojih.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Zadriglo je srce njihovo kao salo, a ja se tješim zakonom tvojim.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Dobro mi je što stradam, da se nauèim naredbama tvojim.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Miliji mi je zakon usta tvojih nego tisuæe zlata i srebra.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Ruke tvoje stvorile su me i naèinile me; urazumi me, i nauèiæu se zapovijestima tvojim.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Koji se tebe boje, vidjeæe me, i radovaæe se što se uzdam u tvoju rijeè.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Znam da su sudovi tvoji, Gospode, pravedni, i po pravdi me karaš.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Neka bude dobrota tvoja utjeha moja, kao što si rekao sluzi svojemu.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Neka doðe k meni milosrðe tvoje, i oživim; jer je zakon tvoj utjeha moja.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Nek se postide oholi; jer me bez krivice oboriše. Ja razmišljam o zapovijestima tvojim.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Nek se obrate k meni koji se tebe boje, i koji znadu otkrivenja tvoja.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Srce moje neka bude savršeno u naredbama tvojim, da se ne postidim.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Èezne duša moja za spasenjem tvojim, rijeè tvoju èekam.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Èeznu oèi moje za rijeèju tvojom; govorim: kad æeš me utješiti?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Postadoh kao mijeh u dimu, ali tvojih naredaba ne zaboravih.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Koliko æe biti dana sluge tvojega? Kad æeš suditi onima koji me gone?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Oholi iskopaše mi jamu nasuprot zakonu tvojemu.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Sve su zapovijesti tvoje istina; bez krivice me gone, pomozi mi.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Umalo me ne ubiše na zemlji, ali ja ne ostavljam zapovijesti tvojih.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Po milosti svojoj oživi me, i èuvaæu otkrivenja usta tvojih.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Dovijeka je, Gospode, rijeè tvoja utvrðena na nebesima,
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Od koljena do koljena istina tvoja; ti si postavio zemlju, i stoji.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Po tvojoj naredbi sve stoji sad; jer sve služi tebi.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Da nije zakon tvoj bio utjeha moja, poginuo bih u nevolji svojoj.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Zapovijesti tvojih neæu zaboraviti dovijeka, jer me njima oživljavaš.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Ja sam tvoj, pomozi mi, jer tražim zapovijesti tvoje.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Bezbožnici gledaju da me ubiju; a ja razmišljam o tvojim otkrivenjima.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Svemu savršenome vidjeh kraj; ali je zapovijest tvoja veoma široka.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Kako ljubim zakon tvoj! Vas dan mislim o njemu.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Zapovijest tvoja èini me mudrijega od neprijatelja mojih; jer je sa mnom uvijek.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Razumniji postah od svijeh uèitelja svojih; jer razmišljam o tvojim otkrivenjima.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Mudriji sam od staraca; jer zapovijesti tvoje èuvam.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Od svakoga zloga puta zaustavljam noge svoje, da bih èuvao rijeè tvoju.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Od naredaba tvojih ne otstupam; jer si me ti nauèio.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Kako su slatke jeziku mojemu rijeèi tvoje, slaðe od meda ustima mojima!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Od zapovijesti tvojih postadoh razuman; toga radi mrzim na svaki put lažni.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Rijeè je tvoja žižak nozi mojoj, i vidjelo stazi mojoj.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Zakleh se da æu èuvati naredbe pravde tvoje, i izvršiæu.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Poništen sam veoma, Gospode, oživi me po rijeèi svojoj.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Neka ti bude ugodna, Gospode, dobrovoljna žrtva usta mojih, i sudovima svojim nauèi me.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Duša je moja u ruci mojoj neprestano u nevolji; ali zakona tvojega ne zaboravljam.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Bezbožnici su mi metnuli zamku; ali od zapovijesti tvojih ne zastranih.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Prisvojih otkrivenja tvoja zavavijek; jer su radost srcu mojemu.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Privolio sam srce svoje da tvori naredbe tvoje navijek, do kraja.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Koji prestupaju zakon, ja na njih mrzim, a zakon tvoj ljubim.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Ti si zaklon moj i štit moj; rijeè tvoju èekam.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Idite od mene, bezakonici! I èuvaæu zapovijesti Boga svojega.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Ukrijepi me po rijeèi svojoj i biæu živ, i nemoj me osramotiti u nadanju mom.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Utvrdi me, i spašæu se, i razmišljaæu o naredbama tvojim bez prestanka.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Obaraš sve koji otstupaju od naredaba tvojih; jer su pomisli njihove laž.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Kao gar bacaš sve bezbožnike na zemlji; toga radi omilješe mi otkrivenja tvoja.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Drkæe od straha tvojega tijelo moje, i sudova tvojih bojim se.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Èinim sud i pravdu, ne daj me onima koji me gone.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Odbrani slugu svojega na dobro njegovo, da mi ne èine sile oholi.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Oèi moje èeznu za spasenjem tvojim i za rijeèju pravde tvoje.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Uèini sluzi svojemu po milosti svojoj, i naredbama svojim nauèi me.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Ja sam sluga tvoj; urazumi me, i poznaæu otkrivenja tvoja.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Vrijeme je da Gospod radi; oboriše zakon tvoj.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Toga radi ljubim zapovijesti tvoje veæma nego zlato i drago kamenje.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Toga radi zapovijesti tvoje držim da su vjerne, na svaki put lažni mrzim.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Divna su otkrivenja tvoja; zato ih èuva duša moja.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Rijeèi tvoje kad se jave, prosvjetljuju i urazumljuju proste.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Otvoram usta svoja da odahnem, jer sam žedan zapovijesti tvojih.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Pogledaj me i smiluj se na me, kao što radiš s onima koji ljube ime tvoje.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Tvrdi stope moje u rijeèi svojoj, i ne daj nikakome bezakonju da oblada mnom.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Izbavi me od nasilja ljudskoga, i èuvaæu zapovijesti tvoje.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Svjetlošæu lica svojega obasjaj slugu svojega, i nauèi me naredbama svojim.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Oèi moje liju potoke, zato što ne èuvaju zakona tvojega.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Pravedan si, Gospode, i pravi su sudovi tvoji.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Javio si pravdu u otkrivenjima svojim, i istinu cijelu.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Revnost moja jede me, zato što moji neprijatelji zaboraviše rijeèi tvoje.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Rijeè je tvoja veoma èista, i sluga je tvoj veoma ljubi.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Ja sam malen i poništen, ali zapovijesti tvojih ne zaboravljam.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Pravda je tvoja pravda vjeèna, i zakon tvoj istina.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Tuga i nevolja naðe me, zapovijesti su tvoje utjeha moja.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Vjeèna je pravda u otkrivenjima tvojim; urazumi me, i biæu živ.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Vièem iz svega srca: usliši me, Gospode; saèuvaæu naredbe tvoje.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Prizivam te, pomozi mi; držaæu se otkrivenja tvojih.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Pretjeèem svanuæe, i vièem; rijeè tvoju èekam.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Pretjeèu oèi moje jutrenju stražu, da bih razmišljao o rijeèi tvojoj.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Èuj glas moj po milosti svojoj, Gospode; po sudu svojemu oživi me.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Prikuèuju se koji ljube bezakonje; udaljili su se od zakona tvojega.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Ti si blizu, Gospode, i sve su zapovijesti tvoje istina.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Odavna znam za otkrivenja tvoja, da si ih postavio zavavijek.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Pogledaj nevolju moju, i izbavi me, jer ne zaboravljam zakona tvojega.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Primi se stvari moje, i odbrani me; po rijeèi svojoj oživi me.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Daleko je od bezbožnika spasenje, jer se ne drže naredaba tvojih.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Milosrðe je tvoje, Gospode, veliko; po pravome sudu svom oživi me.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Mnogo je protivnika mojih i neprijatelja mojih; ali ja ne otstupam od otkrivenja tvojih.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Vidim odmetnike, i mrsko mi je; jer ne èuvaju rijeèi tvoje.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Gledaj, kako ljubim zapovijesti tvoje, Gospode, po milosti svojoj oživi me.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Osnova je rijeèi tvoje istina, i vjeèan je svaki sud pravde tvoje.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Knezovi me gone ni za što, ali se srce moje boji rijeèi tvoje.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Radujem se rijeèi tvojoj kao onaj koji zadobije velik plijen.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Mrzim na laž i gadim se na nju, ljubim zakon tvoj.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Sedam puta na dan hvalim te za sudove pravde tvoje.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Velik mir imaju oni koji ljube zakon tvoj, i u njih nema spoticanja.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Èekam spasenje tvoje, Gospode, i zapovijesti tvoje izvršujem.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Duša moja èuva otkrivenja tvoja, i ja ih ljubim veoma.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Èuvam zapovijesti tvoje i otkrivenja; jer su svi putovi moji pred tobom.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Neka izaðe tužnjava moja preda te, Gospode! Po rijeèi svojoj urazumi me.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Neka doðe moljenje moje preda te! Po rijeèi svojoj izbavi me.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Usta æe moja pjevati hvalu, kad me nauèiš naredbama svojim.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Jezik æe moj kazivati rijeè tvoju, jer su sve zapovijesti tvoje pravedne.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Neka mi bude ruka tvoja u pomoæi; jer mi omilješe zapovijesti tvoje;
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Žedan sam spasenja tvojega, Gospode, i zakon je tvoj utjeha moja.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Neka živi duša moja i tebe hvali, i sudovi tvoji neka mi pomogu.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Zaðoh kao ovca izgubljena: traži slugu svojega; jer zapovijesti tvojih ne zaboravih.

< Masalimo 119 >