< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Agradecei ao SENHOR, porque ele é bom; pois sua bondade [dura] para sempre.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Diga agora Israel, que sua bondade [dura] para sempre.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Diga agora casa de Arão, que sua bondade [dura] para sempre.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Digam agora os que temem ao SENHOR, que sua bondade [dura] para sempre.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Na angústia clamei ao SENHOR; [e] o SENHOR me respondeu, e [me pôs] num lugar amplo.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
O SENHOR está comigo, não temerei; o que poderá me fazer o homem?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
O SENHOR está comigo entre os que ajudam; por isso verei [o fim] daqueles que me odeiam.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
Melhor é buscar refúgio no SENHOR do que confiar no homem.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
Melhor é buscar refúgio no SENHOR do que confiar em príncipes.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Todas as nações me cercaram; [mas foi] no nome do SENHOR que eu as despedacei.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Cercaram-me, cercaram-me mesmo; [mas foi] no nome do SENHOR que eu as despedacei.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Cercaram-me como abelhas, mas se apagaram como fogo de espinhos; [porque] foi no nome do SENHOR que eu as despedacei.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Com força me empurraste para que eu caísse; mas o SENHOR me ajudou.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
O SENHOR é minha força e [minha] canção, porque ele tem sido minha salvação.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
Nas tendas dos justos há voz de alegria e salvação; a mão direita do SENHOR faz proezas.
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
A mão direita do SENHOR se levanta; a mão direita do SENHOR faz proezas.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
Eu não morrerei, mas viverei; e contarei as obras do SENHOR.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
É verdade que o SENHOR me castigou, porém ele não me entregou à morte.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Abri para mim as portas da justiça; entrarei por elas [e] louvarei ao SENHOR.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
Esta é a porta do SENHOR, pela qual os justos entrarão.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
Eu te louvarei porque tu me respondeste e me salvaste.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
A pedra que os construtores rejeitaram se tornou cabeça de esquina.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
Pelo SENHOR isto foi feito, [e] é maravilhoso aos nossos olhos.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
Este é o dia em que o SENHOR agiu; alegremos e enchamos de alegria nele.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Ah, SENHOR, salva-nos! Ah, SENHOR, faze [-nos] prosperar!
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Bendito aquele que vem no nome do SENHOR; nós vos bendizemos desde a casa do SENHOR.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
O SENHOR é o [verdadeiro] Deus, que nos deu luz; atai os [sacrifícios] da festa, para [levá-los] aos chifres do altar.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Tu és meu Deus, por isso eu te louvarei. Eu te exaltarei, meu Deus.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Agradecei ao SENHOR, porque ele é bom; pois sua bondade [dura] para sempre.

< Masalimo 118 >