< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Provérbios de Salomão, filho de Davi, rei de Israel.
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
Para conhecer a sabedoria e a instrução; para entender as palavras da prudência;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
Para obter a instrução do entendimento; justiça, juízo e equidades;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
Para dar inteligência aos simples, conhecimento e bom senso aos jovens.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
O sábio ouvirá, e crescerá em conhecimento; o bom entendedor obterá sábios conselhos.
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
Para entender provérbios e [sua] interpretação; as palavras dos sábios, e seus enigmas.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
O temor ao SENHOR [é] o principio do conhecimento; os tolos desprezam a sabedoria e a instrução.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Filho meu, ouve a instrução de teu pai; e não abandones a doutrina de tua mãe.
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Porque [serão] um ornamento gracioso para tua cabeça; e colares para teu pescoço.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Filho meu, se os pecadores tentarem te convencer, não te deixes influenciar.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
Se disserem: Vem conosco, vamos espiar [derramamento] de sangue; preparemos uma emboscada ao inocente sem razão.
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
Vamos tragá-los vivos, como o Xeol; e inteiros, como os que descem à cova. (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Acharemos toda espécie de coisas valiosas, encheremos nossas casas de despojos.
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Lança tua sorte entre nós, compartilharemos todos de uma [só] bolsa.
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Filho meu, não sigas teu caminho com eles; desvia teu pé [para longe] de onde eles passarem;
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
Porque os pés deles correm para o mal, e se apressam para derramar sangue.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Certamente [é] inútil se estender a rede diante da vista de todas as aves;
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
Porém estes estão esperando [o derramamento] de seu [próprio] sangue; e preparam emboscada para suas [próprias] almas.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Assim [são] os caminhos de todo aquele que tem ganância pelo lucro desonesto; ela tomará a alma daqueles que a tem.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
A sabedoria grita pelas ruas; nas praças ela levanta sua voz.
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
Ela clama nas encruzilhadas, onde [passam] muita gente; às entradas das portas, nas cidades ela diz suas mensagens:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Até quando, ó tolos, amareis a tolice? E vós zombadores, desejareis a zombaria? E [vós] loucos, odiareis o conhecimento?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Convertei-vos à minha repreensão; eis que vos derramarei meu espírito, [e] vos farei saber minhas palavras.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
[Mas] porque eu clamei, e recusastes; estendi minha mão, e não houve quem desse atenção,
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
E rejeitastes todo o meu conselho, e não quisestes minha repreensão,
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
Também eu rirei em vosso sofrimento, [e] zombarei, quando vier vosso medo.
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
Quando vier vosso temor como tempestade, e a causa de vosso sofrimento como ventania, quando vier sobre vós a opressão e a angústia,
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Então clamarão a mim; porém eu não responderei; de madrugada me buscarão, porém não me acharão.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Porque odiaram o conhecimento; e escolheram não temer ao SENHOR.
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
Não concordaram com meu conselho, [e] desprezaram toda a minha repreensão.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Por isso comerão do fruto do seu [próprio] caminho, e se fartarão de seus [próprios] conselhos.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Pois o desvio dos tolos os matará, e a confiança dos loucos os destruirá.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Porém aquele que me ouvir habitará em segurança, e estará tranquilo do temor do mal.

< Miyambo 1 >