< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Célébrez l’Éternel! Car il est bon; car sa bonté demeure à toujours.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Qu’Israël dise, que sa bonté demeure à toujours!
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Que la maison d’Aaron dise, que sa bonté demeure à toujours!
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Que ceux qui craignent l’Éternel disent, que sa bonté demeure à toujours!
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Dans ma détresse j’ai invoqué Jah; Jah m’a répondu, [et m’a mis] au large.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
L’Éternel est pour moi, je ne craindrai pas; que me fera l’homme?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
L’Éternel est pour moi entre ceux qui me secourent; et moi je verrai [mon plaisir] en ceux qui me haïssent.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
Mieux vaut mettre sa confiance en l’Éternel que de se confier en l’homme.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
Mieux vaut mettre sa confiance en l’Éternel que de se confier dans les principaux.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Toutes les nations m’avaient environné; au nom de l’Éternel, certes je les ai détruites.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Elles m’avaient environné, oui, environné; au nom de l’Éternel, certes je les ai détruites.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Elles m’avaient environné comme des abeilles; elles ont été éteintes comme un feu d’épines; au nom de l’Éternel, certes je les ai détruites.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Tu m’avais rudement poussé, pour que je tombe; mais l’Éternel m’a été en secours.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
Jah a été ma force et mon cantique, et il a été mon salut.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
La voix de triomphe et de salut est dans les tentes des justes: la droite de l’Éternel agit puissamment;
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
La droite de l’Éternel est haut élevée, la droite de l’Éternel agit puissamment;
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
Je ne mourrai pas, mais je vivrai, et je raconterai les œuvres de Jah.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
Jah m’a sévèrement châtié, mais il ne m’a pas livré à la mort.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Ouvrez-moi les portes de la justice; j’y entrerai, je célébrerai Jah.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
C’est ici la porte de l’Éternel, les justes y entreront.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
Je te célébrerai, car tu m’as répondu, et tu as été mon salut.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
La pierre que ceux qui bâtissaient avaient rejetée, est devenue la tête de l’angle.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
Ceci a été de par l’Éternel: c’est une chose merveilleuse devant nos yeux.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
C’est ici le jour que l’Éternel a fait; égayons-nous et réjouissons-nous en lui!
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Ô Éternel, sauve, je te prie! Éternel, je te prie, donne la prospérité!
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Béni soit celui qui vient au nom de l’Éternel! Nous vous avons bénis de la maison de l’Éternel.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
L’Éternel est Dieu, et il nous a donné la lumière. Liez avec des cordes le sacrifice aux cornes de l’autel.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Tu es mon Dieu, et je te célébrerai, – mon Dieu, je t’exalterai.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Célébrez l’Éternel! car il est bon, car sa bonté demeure à toujours.

< Masalimo 118 >