< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Proverbes de Salomon, fils de David, roi d’Israël,
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
pour connaître la sagesse et l’instruction, pour discerner les paroles d’intelligence;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
pour recevoir instruction dans la sagesse, la justice, le juste jugement, et la droiture;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
pour donner aux simples de la prudence, au jeune homme de la connaissance et de la réflexion.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Le sage écoutera, et croîtra en science, et l’intelligent acquerra du sens
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
pour comprendre un proverbe et une allégorie, les paroles des sages et leurs énigmes.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
La crainte de l’Éternel est le commencement de la connaissance; les fous méprisent la sagesse et l’instruction.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Écoute, mon fils, l’instruction de ton père, et n’abandonne pas l’enseignement de ta mère;
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
car ce sera une guirlande de grâce à ta tête, et des colliers à ton cou.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Mon fils, si les pécheurs cherchent à te séduire, n’y acquiesce pas.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
S’ils disent: Viens avec nous, nous serons aux embûches pour le sang, nous nous cacherons pour [guetter] l’innocent, sans cause;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
nous les engloutirons vivants, comme le shéol, et tout entiers comme ceux qui descendent dans la fosse; (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
nous trouverons toute sorte de biens précieux, nous remplirons nos maisons de butin;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
prends ton lot parmi nous, il n’y aura qu’une bourse pour nous tous:
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
mon fils, ne fais pas route avec eux, retiens ton pied de leur sentier;
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
car leurs pieds courent au mal, et ils se hâtent pour verser le sang.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Car en vain le filet est étendu devant les yeux de tout ce qui a des ailes;
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
et eux, ils sont aux embûches contre leur propre sang, ils se cachent pour [guetter] leurs propres âmes.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Telles sont les voies de tout homme qui cherche le gain déshonnête, lequel ôte la vie à ceux qui le possèdent.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
La sagesse crie au-dehors, elle fait retentir sa voix sur les places;
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
elle crie à l’entrée des lieux bruyants, aux ouvertures des portes; elle prononce ses paroles dans la ville:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Simples, jusques à quand aimerez-vous la simplicité, et [jusques à quand] les moqueurs prendront-ils plaisir à la moquerie, et les sots haïront-ils la connaissance?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Revenez à ma répréhension; voici, je ferai couler pour vous mon esprit, je vous ferai savoir mes paroles.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Parce que j’ai crié et que vous avez refusé [d’écouter], parce que j’ai étendu ma main et que personne n’a pris garde,
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
et que vous avez rejeté tout mon conseil et que vous n’avez pas voulu de ma répréhension,
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
moi aussi je rirai lors de votre calamité, je me moquerai quand viendra votre frayeur,
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
quand votre frayeur viendra comme une subite destruction et que votre calamité arrivera comme un tourbillon, quand la détresse et l’angoisse viendront sur vous:
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
alors ils crieront vers moi, et je ne répondrai pas; ils me chercheront de bonne heure, mais ils ne me trouveront point.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Parce qu’ils ont haï la connaissance et qu’ils n’ont pas choisi la crainte de l’Éternel,
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
qu’ils n’ont point voulu de mon conseil, qu’ils ont méprisé toute ma répréhension,
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
ils mangeront du fruit de leur voie et seront rassasiés de leurs propres conseils.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Car la révolte des simples les tue, et la prospérité des sots les fait périr.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Mais celui qui m’écoute habitera en sécurité et sera tranquille, sans crainte du mal.

< Miyambo 1 >