< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Alleluia. I will give thee thanks, O Lord, with my whole heart, in the council of the upright, and [in] the congregation.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
The works of the Lord are great, sought out according to all his will.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
His work is [worthy of] thanksgiving and honour: and his righteousness endures for ever and ever.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
He has caused his wonderful works to be remembered: the Lord is merciful and compassionate.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
He has given food to them that fear him: he will remember his covenant for ever.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
He has declared to his people the power of his works, to give them the inheritance of the heathen.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
The works of his hands are truth and judgment: all his commandments are sure:
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
established for ever and ever, done in truth and uprightness.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
He sent redemption to his people: he commanded his covenant for ever: holy and fearful is his name.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
The fear of the Lord is the beginning of wisdom, and all that act accordingly have a good understanding; his praise endures for ever and ever.

< Masalimo 111 >