< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
The Proverbs of Solomon son of David, who reigned in Israel;
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
to know wisdom and instruction, and to perceive words of understanding;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
to receive also hard saying, and to understand true justice, and [how] to direct judgment;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
that he might give subtlety to the simple, and to the young man discernment and understanding.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
For by the hearing of these a wise man will be wiser, and man of understanding will gain direction;
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
and will understand a parable, and a dark speech; the saying of the wise also, and riddles.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
The fear of the Lord is the beginning of wisdom; and [there is] good understanding to all that practise it: and piety toward God is the beginning of discernment; but the ungodly will set at nought wisdom and instruction.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Hear, [my] son, the instruction of thy father, and reject not the rules of thy mother.
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
For thou shalt receive for thine head a crown of graces, and a chain of gold round thy neck.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
[My] son, let not ungodly men lead thee astray, neither consent thou [to them].
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
If they should exhort thee, saying, Come with us, partake in blood, and let us unjustly hide the just man in the earth:
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
and let us swallow him alive, as Hades [would], and remove the memorial of him from the earth: (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
let us seize on his valuable property, and let us fill our houses with spoils:
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
but do thou cast in thy lot with us, and let us all provide a common purse, and let us have one pouch:
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
go not in the way with them, but turn aside thy foot from their paths:
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
[For their feet run to do evil, and are swift to shed blood. ]
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
for nets are not without cause spread for birds.
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
For they that are concerned in murder store up evils for themselves; and the overthrow of transgressors is evil.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
These are the ways of all that perform lawless deeds; for by ungodliness they destroy their own life.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Wisdom sings aloud in passages, and in the broad places speaks boldly.
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
And she makes proclamation on the top of the walls, and sits by the gates of princes; and at the gates of the city boldly says,
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
So long as the simple cleave to justice, they shall not be ashamed: but the foolish being lovers of haughtiness, having become ungodly have hated knowledge, and are become subject to reproofs.
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Behold, I will bring forth to you the utterance of my breath, and I will instruct you in my speech.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Since I called, and ye did not hearken; and I spoke at length, and ye gave no heed;
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
but ye set at nought my counsels, and disregarded my reproofs;
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
therefore I also will laugh at your destruction; and I will rejoice against [you] when ruin comes upon you:
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
yea when dismay suddenly comes upon you, and [your] overthrow shall arrive like a tempest; and when tribulation and distress shall come upon you, or when ruin shall come upon you.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
For it shall be that when ye call upon me, I will not hearken to you: wicked men shall seek me, but shall not find [me].
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
For they hated wisdom, and did not choose the word of the Lord:
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
neither would they attend to my counsels, but derided my reproofs.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Therefore shall they eat the fruits of their own way, and shall be filled with their own ungodliness.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
For because they wronged the simple, they shall be slain; and an inquisition shall ruin the ungodly.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
But he that hearkens to me shall dwell in confidence, and shall rest securely from all evil.

< Miyambo 1 >