< Miyambo 28 >

1 Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
A wickid man fleeth, whanne no man pursueth; but a iust man as a lioun tristynge schal be with out ferdfulnesse.
2 Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
For the synnes of the lond ben many princis therof; and for the wisdom of a man, and for the kunnyng of these thingis that ben seid, the lijf of the duyk schal be lengere.
3 Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
A pore man falsli calengynge pore men, is lijk a grete reyn, wherynne hungur is maad redi.
4 Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
Thei that forsaken the lawe, preisen a wickid man; thei that kepen `the lawe, ben kyndlid ayens hym.
5 Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
Wickid men thenken not doom; but thei that seken the Lord, perseyuen alle thingis.
6 Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
Betere is a pore man goynge in his sympilnesse, than a riche man in schrewid weies.
7 Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
He that kepith the lawe, is a wijs sone; but he that fedith glotouns, schendith his fadir.
8 Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
He that gaderith togidere richessis bi vsuris, and fre encrees, gaderith tho togidere ayens pore men.
9 Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
His preyer schal be maad cursid, that bowith awei his eere; that he here not the lawe.
10 Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
He that disseyueth iust men in an yuel weye, schal falle in his perisching; and iuste men schulen welde hise goodis.
11 Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
A ryche man semeth wijs to him silf; but a pore man prudent schal serche him.
12 Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
In enhaunsing of iust men is miche glorie; whanne wickid men regnen, fallyngis of men ben.
13 Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
He that hidith hise grete trespassis, schal not be maad riytful; but he that knoulechith and forsakith tho, schal gete merci.
14 Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
Blessid is the man, which is euere dredeful; but he that is `harde of soule, schal falle in to yuel.
15 Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
A rorynge lioun, and an hungry bere, is a wickid prince on a pore puple.
16 Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
A duyk nedi of prudence schal oppresse many men bi fals chalenge; but the daies of hym that hatith aueryce, schulen be maad longe.
17 Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
No man susteyneth a man that falsly chalengith the blood of a man, if he fleeth `til to the lake.
18 Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
He that goith simpli, schal be saaf; he that goith bi weiward weies, schal falle doun onys.
19 Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
He that worchith his lond, schal be fillid with looues; he that sueth ydelnesse, schal be fillid with nedynesse.
20 Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
A feithful man schal be preisid myche; but he that hastith to be maad riche, schal not be innocent.
21 Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
He that knowith a face in doom, doith not wel; this man forsakith treuthe, yhe, for a mussel of breed.
22 Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
A man that hastith to be maad riche, and hath enuye to othere men; woot not that nedinesse schal come on hym.
23 Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
He that repreueth a man, schal fynde grace aftirward at hym; more than he that disseyueth bi flateryngis of tunge.
24 Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
He that withdrawith ony thing fro his fadir and fro his modir, and seith that this is no synne, is parcener of a manquellere.
25 Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
He that auauntith hym silf, and alargith, reisith stryues; but he that hopith in the Lord, schal be sauyd.
26 Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
He that tristith in his herte, is a fool; but he that goith wiseli,
27 Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
schal be preysid. He that yyueth to a pore man, schal not be nedi; he that dispisith `a pore man bisechynge, schal suffre nedynesse.
28 Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.
Whanne vnpitouse men risen, men schulen be hid; whanne tho `vnpitouse men han perischid, iust men schulen be multiplied.

< Miyambo 28 >