< Numeri 12 >

1 Miriamu ndi Aaroni anayamba kuyankhula motsutsana ndi Mose chifukwa cha mkazi wa ku Kusi, popeza Moseyo anakwatira Mkusi.
I stadoše vikati Marija i Aron na Mojsija radi žene Madijanke, kojom se oženi, jer se oženi Madijankom.
2 Iwowo anafunsa kuti, “Kodi Yehova anayankhula kudzera mwa Mose yekha? Kodi sanayankhule kudzeranso mwa ife?” Ndipo Yehova anamva zimenezi.
I rekoše: zar je samo preko Mojsija govorio Gospod? nije li govorio i preko nas? I to èu Gospod.
3 (Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).
A Mojsije bješe èovjek vrlo krotak mimo sve ljude na zemlji.
4 Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko.
I odmah reèe Gospod Mojsiju i Aronu i Mariji: doðite vas troje u šator od sastanka. I otidoše njih troje.
5 Tsono Yehova anatsika mu mtambo, nayima pa khomo la chihema. Kenaka anayitana Aaroni ndi Miriamu. Ndipo onse awiri atapita patsogolo,
Tada siðe Gospod u stupu od oblaka, i stade na vratima od šatora. I viknu Arona i Mariju, i doðoše oboje.
6 Mulungu anati, “Mverani mawu anga: “Pakakhala mneneri wa Yehova pakati panu, ndimadzionetsera kwa iyeyo mʼmasomphenya, ndimayankhula naye mʼmaloto.
I reèe im: èujte sada rijeèi moje: prorok kad je meðu vama, ja æu mu se Gospod javljati u utvari i govoriæu s njim u snu.
7 Koma sinditero ndi Mose mtumiki wanga; Iyeyu ndi wokhulupirika mʼnyumba yanga yonse.
Ali nije taki moj sluga Mojsije, koji je vjeran u svem domu mojem.
8 Ndimayankhula naye maso ndi maso, momveka bwino osati mophiphiritsa; ndipo amaona maonekedwe a Yehova. Nʼchifukwa chiyani simunaope kuyankhula motsutsana ndi Mose mtumiki wanga?”
Njemu govorim iz usta k ustima, i on me gleda doista, a ne u tami niti u kakvoj prilici Gospodnjoj. Kako se dakle ne pobojaste vikati na slugu mojega, na Mojsija?
9 Ndipo Yehova anawakwiyira, nachoka.
I gnjev se Gospodnji raspali na njih, i on otide.
10 Pamene mtambo unachoka pamwamba pa Chihema, taonani, Miriamu anagwidwa ndi khate. Aaroni atachewuka anaona Miriamu ali ndi khate;
I oblak se podiže sa šatora; i gle, Marija bješe gubava, bijela kao snijeg. I Aron pogleda Mariju, a ona gubava.
11 ndipo Aaroni anawuza Mose kuti, “Pepani mbuye wanga, musatilange chifukwa cha tchimo limene tachita mopusa.
Tada reèe Aron Mojsiju: gospodaru, molim te, ne meæi na nas grijeha ovoga, jer ludo uèinismo i zgriješismo.
12 Musalole kuti Miriamu akhale ngati mwana wobadwa wakufa kuchoka mʼmimba mwa amayi ake, thupi lake litawonongeka.”
Nemoj da ova bude kao mrtvo dijete, kojemu je meso pola trulo kad izlazi iz utrobe matere svoje.
13 Tsono Mose anafuwulira Yehova kuti, “Chonde Inu Mulungu, muchiritseni!”
I vapi Mojsije ka Gospodu govoreæi: Bože, molim ti se, iscijeli je.
14 Yehova anayankha Mose kuti, “Abambo ake akanamulavulira malovu mʼmaso, kodi sakanakhala wonyozeka masiku asanu ndi awiri? Mutsekereni kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri, kenaka mumulowetsenso.”
A Gospod odgovori Mojsiju: da joj je otac njezin pljunuo u lice, ne bi li se stidjela sedam dana? Neka bude odluèena sedam dana izvan okola, a poslije neka bude opet primljena.
15 Choncho anamutsekera Miriamu kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri ndipo anthu sanayende ulendo wawo mpaka Miriamu atamulowetsanso.
Tako bi Marija odluèena izvan okola sedam dana; i narod ne poðe odande dokle Marija ne bi opet primljena.
16 Pambuyo pake anthu ananyamuka ku Heziroti ndi kukamanga mʼchipululu cha Parani.
A potom poðe narod od Asirota, i stadoše u pustinji Faranskoj.

< Numeri 12 >