< Numeri 11 >

1 Anthu atadandaula kwa Yehova chifukwa cha mavuto awo, Yehovayo anamva ndipo anakwiya kwambiri. Kenaka moto wa Yehova unayaka pakati pawo ndi kutentha zigawo zina za kunja kwa msasa.
Poslije stade se tužiti narod da mu je teško; a to ne bi po volji Gospodu; i kad Gospod èu, razgnjevi se; i raspali se na njih oganj Gospodnji, i sažeže krajnje u okolu.
2 Anthuwo analira kwa Mose ndipo Moseyo atapemphera kwa Yehova, motowo unazima.
Tada zavapi narod k Mojsiju, a Mojsije se pomoli Gospodu, i ugasi se oganj.
3 Motero malowo anawatcha Tabera, chifukwa moto wa Yehova unayaka pakati pawo.
I prozva se ono mjesto Tavera, jer se raspali na njih oganj Gospodnji.
4 Anthu ena osokoneza amene anali pakati pa Aisraeli anayamba kukhumba chakudya cha ku Igupto ndipo Aisraeli nawonso anayamba kufuwula kwambiri nʼkumati, “Tikanangopeza nyama yoti nʼkudya!
A svjetina što bijaše meðu njima, bješe vrlo lakoma, te i sinovi Izrailjevi stadoše plakati govoreæi: ko æe nas nahraniti mesa?
5 Tikukumbukira nsomba zaulere zimene tinkadya ku Igupto komanso nkhaka, mavwende, anyezi wamitundumitundu ndi adyo.
Opomenusmo se riba što jeðasmo u Misiru zabadava, i krastavaca i dinja i luka crnoga i bijeloga.
6 Koma tsopano chilakolako chathu chatha. Sitikuona kanthu kena kakudya koma mana basi!”
A sada posahnu duša naša, nema ništa osim mane pred oèima našima.
7 Mana ankafanana ndi mbewu zamapira ndipo maonekedwe ake anali ngati ulimbo wowuma.
A mana bješe kao sjeme korijandrovo, a boja mu bješe kao boja u bdela.
8 Anthu ankapita kukatola manawo, nʼkumasinja mu mtondo kapena kupera. Ankawaphika mu mʼphika kapena kupanga makeke. Ndipo ankakoma ngati makeke ophikira mafuta a olivi.
I izlažaše narod, te kupljahu, i meljahu na žrvnjima ili tucahu u stupama, i kuhahu u kotlu, ili miješahu pogaèe; a kus joj bijaše kao kus od novoga ulja.
9 Mame akamagwa pa msasawo usiku ankagwera kumodzi ndi manawo.
I kad padaše rosa po okolu noæu, padaše s njom i mana.
10 Mose anamva anthu a banja lililonse akufuwula, banja lililonse pa khomo la tenti yake. Yehova anakwiya kwambiri ndipo Mose anavutikanso mu mtima.
I èu Mojsije gdje narod plaèe u porodicama svojim, svaki na vratima od šatora svojega; i Gospod se razgnjevi vrlo, i Mojsiju bi teško.
11 Mose anafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani mwabweretsa mavuto otere pa mtumiki wanune? Nʼchiyani chimene ndachita choti sichinakusangalatseni mpaka kundisenzetsa katundu wa anthu onsewa?
Pa reèe Mojsije Gospodu: zašto uèini tako zlo sluzi svojemu? i zašto ne naðoh milosti pred tobom, nego metnu na me teret svega naroda ovoga?
12 Kodi Ndine amene ndinatenga pathupi pa anthu onsewa? Kodi ndinawabala ndine? Bwanji mukundiwuza kuti ndiwanyamule mʼmanja mwanga, monga momwe mlezi amanyamulira kamwana, kupita nawo ku malo omwe munalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo?
Eda li ja zaèeh sav ovaj narod? eda li ga ja rodih, kad mi kažeš: iznesi ga u naruèju svojem, kao što nosi dojilja dijete, u onu zemlju za koju si se zakleo ocima njihovijem.
13 Ndingayipeze kuti nyama yoti anthu onsewa adye? Iwowa akulirira ine kuti, ‘Tipatse nyama tidye!’
Otkuda meni mesa da dam svemu ovom narodu? jer plaèu preda mnom govoreæi: daj nam mesa da jedemo.
14 Sindingathe kusamala anthu onsewa ndekha. Katundu ameneyu ndi wolemera kwambiri kwa ine.
Ne mogu ja sam nositi svega naroda ovoga, jer je teško za mene.
15 Ngati umu ndi mmene muzichitira nane, chonde ingondiphani pompano. Koma ngati mwandikomera mtima ndiye ndisaonenso mavutowa.”
Ako æeš tako èiniti sa mnom, ubij me bolje, ako sam našao milost pred tobom, da ne gledam zla svojega.
16 Yehova anawuza Mose kuti, “Undibweretsere anthu 70 ochokera pakati pa akuluakulu a Aisraeli, amene umawadziwa kuti ndiwo atsogoleri komanso akuluakulu a mabanja. Abwere ku tenti ya msonkhano kuti ayime kumeneko pamodzi ndi iwe.
A Gospod reèe Mojsiju: saberi mi sedamdeset ljudi izmeðu starješina Izrailjevijeh, koje znaš da su starješine narodu i upravitelji njegovi, i dovedi ih k šatoru od sastanka, neka ondje stanu s tobom.
17 Ndidzatsika ndi kuyankhula nawe kumeneko, ndipo ndidzatenga mzimu umene uli pa iwe ndi kuyika pa iwowo. Adzakuthandiza kusenza nkhawa za anthuwa ndipo sudzasenzanso wekha.”
Tada æu siæi i govoriti ondje s tobom, i uzeæu od duha koji je na tebi i metnuæu na njih, da nose s tobom teret narodni i da ne nosiš ti sam.
18 “Uwawuze anthuwo kuti, ‘Mudziyeretse, kukonzekera mawa, pamene mudzadya nyama.’ Yehova anakumvani pamene munkalira kuti, ‘Zikanakhala bwino tikanapeza nyama yoti tidye! Tinkakhala bwino ku Igupto!’ Tsopano Yehova adzakupatsani nyama ndipo mudzayidyadi.
A narodu reci: pripravite se za sjutra da jedete mesa, jer plakaste da Gospod èu, i rekoste: ko æe nas nahraniti mesa? jer nam dobro bijaše u Misiru. Daæe vam dakle Gospod mesa i ješæete.
19 Simudzadya tsiku limodzi lokha, kapena masiku awiri, kapena asanu, khumi kapena masiku makumi awiri,
Neæete jesti jedan dan, ni dva dana, ni pet dana, ni deset dana, ni dvadeset dana;
20 koma mwezi wonse, mpaka itakukolani ndi kutopa nayo chifukwa mwakana Yehova yemwe ali pakati panu ndipo mwalira pamaso pake kuti, ‘Bwanji tinachoka ku Igupto?’”
Nego cio mjesec dana, dokle vam na nos ne udari i ne ogadi vam se, zato što odbaciste Gospoda koji je meðu vama i plakaste pred njim govoreæi: zašto izidosmo iz Misira?
21 Koma Mose anati, “Taonani pano ndili pakati pa anthu 600,000 amene ndi kuyenda nawo ndipo Inuyo mukuti, ‘Ndidzawapatsa nyama kuti adye mwezi wathunthu!’
A Mojsije reèe: šest stotina tisuæa pješaka ima naroda, u kojem sam, pa ti kažeš: daæu im mesa da jedu cio mjesec dana.
22 Kodi ngakhale titapha nkhosa ndi ngʼombe, zingawakwanire? Ngakhale titagwira nsomba zonse za mʼnyanja, kodi zingawakwanire iwowa?”
Eda li æe im se poklati ovce i goveda da im dostane? ili æe im se pokupiti sve ribe morske da im bude dosta?
23 Yehova anayankha Mose kuti, “Kodi dzanja langa ndi lalifupi? Uwona tsopano ngati zimene ndanenazo zichitike kapena ayi.”
A Gospod reèe Mojsiju: zar ruka Gospodnja neæe biti dovoljna? Vidjeæeš hoæe li biti što ti rekoh ili neæe.
24 Choncho Mose anatuluka nakawuza anthu zomwe Yehova ananena. Anasonkhanitsa pamodzi akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja ndi kuwayimiritsa mozungulira Chihema.
I Mojsije izide i reèe narodu rijeèi Gospodnje; i sabra sedamdeset ljudi izmeðu starješina narodnijeh, i postavi ih oko šatora.
25 Ndipo Yehova anatsika mʼmitambo ndi kuyankhula naye ndipo anatengako mzimu womwe unali pa Mose ndi kuwuyika pa akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja. Pamene mzimuwo unakhazikika pa akuluakuluwo, anayamba kunenera koma sanapitirize.
I Gospod siðe u oblaku, i govori k njemu, i uzevši od duha koji bješe na njemu metnu na onijeh sedamdeset ljudi starješina; i kad duh doðe na njih, prorokovahu, ali više nikad.
26 Koma anthu ena awiri omwe mayina awo anali Elidadi ndi Medadi, anatsalira mu msasa. Anali nawo mʼgulu la olembedwa aja, koma sanapite nawo ku Chihema. Komabe mzimu unakhala pa iwo ndipo ananenera ali mu msasa.
A dva èovjeka ostaše u okolu, jednom bješe ime Eldad, a drugom Modad, na koje doðe duh, jer i oni bijahu zapisani ali ne doðoše k šatoru, i stadoše prorokovati u okolu.
27 Mnyamata wina anathamanga kudzawuza Mose kuti, “Elidadi ndi Medadi akunenera mu msasa.”
I dotrèa momak, te javi Mojsiju govoreæi: Eldad i Modad prorokuju u okolu.
28 Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose kuyambira ubwana wake, anayankha kuti, “Mbuye wanga Mose, aletseni!”
A Isus sin Navin, sluga Mojsijev, jedan od momaka njegovijeh, reèe govoreæi: Mojsije gospodaru moj, zabrani im.
29 Koma Mose anati, “Kodi ukuchita nsanje chifukwa cha ine? Ndikanakonda kuti anthu onse a Yehova akhale aneneri ndi kuti Yehova ayike mzimu wake pa iwo!”
A Mojsije mu odgovori: zar zavidiš mene radi? kamo da sav narod Gospodnji postanu proroci i da Gospod pusti duh svoj na njih!
30 Mose ndi akuluakulu a Israeli aja anabwerera ku msasa.
Potom se vrati Mojsije u oko sa starješinama Izrailjevijem.
31 Pamenepo Yehova anawutsa mphepo yochokera ku nyanja imene inabweretsa zinziri. Zinzirizo zinagwera pansi kuzungulira msasa, mtunda wa kilomita imodzi mbali zonse ndipo msinkhu wake unali mita imodzi.
Tada se podiže vjetar od Gospoda, i potjera od mora prepelice, i razasu ih po okolu, na dan hoda odovuda i na dan hoda odonuda oko okola, na dva lakta od zemlje.
32 Tsiku limenelo masana onse mpaka usiku ndiponso tsiku lotsatiralo, anthu anatuluka kunja kukatola zinziri. Palibe amene anasonkhanitsa zochepera makilogalamu 1,000 ndipo anaziyanika kuzungulira msasa wonse.
I ustavši narod vas onaj dan i svu noæ i vas drugi dan kupljaše prepelice: i ko nakupi najmanje nakupi deset gomora; i povješaše ih sebi redom oko okola.
33 Koma pamene anthuwo ankadya nyamayo, asanayimeze nʼkomwe, ukali wa Yehova unafika pa iwo ndipo Iye anawakantha ndi mliri woopsa.
Ali meso još im bijaše u zubima, jošte ga ne pojedoše, a Gospod se razgnjevi na narod, i udari Gospod narod pomorom vrlo velikim.
34 Nʼchifukwa chake malowo anawatcha Kibiroti Hatava chifukwa pamenepo anakwirirapo anthu osusuka aja.
I prozva se ono mjesto Kivrot-Atava jer ondje ukopaše narod koji se bješe polakomio.
35 Kuchoka pa Kibiroti Hatava anthuwo anayenda kupita ku Heziroti ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi.
I poðe narod od Kivrot-Atave u Asirot, i stadoše u Asirotu.

< Numeri 11 >