< Numeri 11 >

1 Anthu atadandaula kwa Yehova chifukwa cha mavuto awo, Yehovayo anamva ndipo anakwiya kwambiri. Kenaka moto wa Yehova unayaka pakati pawo ndi kutentha zigawo zina za kunja kwa msasa.
Yn the meene tyme the grutchyng of the puple, as of men sorewynge for trauel, roos ayens the Lord. And whanne Moises hadde herd this thing, he was wrooth; and the fier of the Lord was kyndelid on hem, and deuouride the laste part of the tentis.
2 Anthuwo analira kwa Mose ndipo Moseyo atapemphera kwa Yehova, motowo unazima.
And whanne the puple hadde cried to Moises, Moises preiede the Lord, and the fier was quenchid.
3 Motero malowo anawatcha Tabera, chifukwa moto wa Yehova unayaka pakati pawo.
And he clepid the name of that place Brennyng, for the fier of the Lord was kyndlid ayens hem.
4 Anthu ena osokoneza amene anali pakati pa Aisraeli anayamba kukhumba chakudya cha ku Igupto ndipo Aisraeli nawonso anayamba kufuwula kwambiri nʼkumati, “Tikanangopeza nyama yoti nʼkudya!
And the comyn puple of `malis and femalis, that hadde stied with hem, brent with desire of fleischis, and sat, and wepte with the sones of Israel ioyned togidere to hem, and seide, Who schal yyue to vs fleischis to ete?
5 Tikukumbukira nsomba zaulere zimene tinkadya ku Igupto komanso nkhaka, mavwende, anyezi wamitundumitundu ndi adyo.
We thenken on the fischis whiche we eten in Egipt freli; gourdis, and melouns, and lekis, and oyniouns, and garlekis comen in to mynde `to vs;
6 Koma tsopano chilakolako chathu chatha. Sitikuona kanthu kena kakudya koma mana basi!”
oure soule is drie; oure iyen byholden noon other thing `no but manna.
7 Mana ankafanana ndi mbewu zamapira ndipo maonekedwe ake anali ngati ulimbo wowuma.
Forsothe manna was as the seed of coriaundre, of the colour of bdellyum, which is whijt and briyt as cristal.
8 Anthu ankapita kukatola manawo, nʼkumasinja mu mtondo kapena kupera. Ankawaphika mu mʼphika kapena kupanga makeke. Ndipo ankakoma ngati makeke ophikira mafuta a olivi.
And the puple yede aboute, and gaderide it, and brak with a queerne stoon, ether pownede in a morter, and sethide in a pot; and made therof litle cakis of the sauour, as of breed maad with oile.
9 Mame akamagwa pa msasawo usiku ankagwera kumodzi ndi manawo.
And whanne dew cam doun in the niyt on the tentis, also manna cam doun togidere.
10 Mose anamva anthu a banja lililonse akufuwula, banja lililonse pa khomo la tenti yake. Yehova anakwiya kwambiri ndipo Mose anavutikanso mu mtima.
Therfor Moises herde the puple wepynge bi meynees, and `alle bi hem silf bi the doris of her tentis; and the woodnesse of the Lord was wrooth greetli, but also the thing was seyn vnsuffrable to Moises.
11 Mose anafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani mwabweretsa mavuto otere pa mtumiki wanune? Nʼchiyani chimene ndachita choti sichinakusangalatseni mpaka kundisenzetsa katundu wa anthu onsewa?
And he seide to the Lord, Whi hast thou turmentid thi seruaunt? whi fynde Y not grace bifor thee? and whi hast thou put on me the burthun of al this puple?
12 Kodi Ndine amene ndinatenga pathupi pa anthu onsewa? Kodi ndinawabala ndine? Bwanji mukundiwuza kuti ndiwanyamule mʼmanja mwanga, monga momwe mlezi amanyamulira kamwana, kupita nawo ku malo omwe munalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo?
whethir Y conseyuede al this multitude, ethir gendride it, that thou seie to me, Bere thou hem in thi bosum as a nurise is wont to bere a litil yong child, and bere thou in to the lond for which thou hast swore to the fadris `of hem.
13 Ndingayipeze kuti nyama yoti anthu onsewa adye? Iwowa akulirira ine kuti, ‘Tipatse nyama tidye!’
wherof ben fleischis to me, that Y `yyue to so greet multitude? Thei wepen bifore me, and seyn, `Yyue thou fleischis to vs that we ete;
14 Sindingathe kusamala anthu onsewa ndekha. Katundu ameneyu ndi wolemera kwambiri kwa ine.
I mai not aloone suffre al this puple, for it is greuouse to me.
15 Ngati umu ndi mmene muzichitira nane, chonde ingondiphani pompano. Koma ngati mwandikomera mtima ndiye ndisaonenso mavutowa.”
If in other maner it semeth to thee, Y biseche that thou sle me, and that Y fynde grace in thin iyen, that Y be not punyschid bi so grete yuelis.
16 Yehova anawuza Mose kuti, “Undibweretsere anthu 70 ochokera pakati pa akuluakulu a Aisraeli, amene umawadziwa kuti ndiwo atsogoleri komanso akuluakulu a mabanja. Abwere ku tenti ya msonkhano kuti ayime kumeneko pamodzi ndi iwe.
And the Lord seide to Moises, Gadere thou to me seuenti men of the eldre men of Israel, whiche thou knowist, `that thei ben the elde men and maistris of the puple; and thou schalt lede hem to the dore of the tabernacle of boond of pees, and thou schalt make to stonde there with thee,
17 Ndidzatsika ndi kuyankhula nawe kumeneko, ndipo ndidzatenga mzimu umene uli pa iwe ndi kuyika pa iwowo. Adzakuthandiza kusenza nkhawa za anthuwa ndipo sudzasenzanso wekha.”
that Y come doun, and speke to thee; and Y schal take awey of thi spirit, and Y schal yyue to hem, that thei susteyne with thee the birthun of the puple, and not thou aloone be greuyd.
18 “Uwawuze anthuwo kuti, ‘Mudziyeretse, kukonzekera mawa, pamene mudzadya nyama.’ Yehova anakumvani pamene munkalira kuti, ‘Zikanakhala bwino tikanapeza nyama yoti tidye! Tinkakhala bwino ku Igupto!’ Tsopano Yehova adzakupatsani nyama ndipo mudzayidyadi.
And thou schalt seie to the puple, Be ye halewid; to morew ye schulen ete fleischis; for Y herde you seie, Who schal yyue to vs the metis of fleischis? it was wel to vs in Egipt; that the Lord yyue `fleischis to you,
19 Simudzadya tsiku limodzi lokha, kapena masiku awiri, kapena asanu, khumi kapena masiku makumi awiri,
and that ye ete not o dai, ethir tweyne, ethir fyue, ethir ten, sotheli nether twenti,
20 koma mwezi wonse, mpaka itakukolani ndi kutopa nayo chifukwa mwakana Yehova yemwe ali pakati panu ndipo mwalira pamaso pake kuti, ‘Bwanji tinachoka ku Igupto?’”
but `til to a monethe of daies, til it go out bi youre nosethirlis, and turne in to wlatyng; for ye han put awei the Lord, which is in the myddis of you, and ye wepten bifor hym, and seiden, Whi yeden we out of Egipt?
21 Koma Mose anati, “Taonani pano ndili pakati pa anthu 600,000 amene ndi kuyenda nawo ndipo Inuyo mukuti, ‘Ndidzawapatsa nyama kuti adye mwezi wathunthu!’
And Moises seide to the Lord, Sixe hundrid thousynde of foot men ben of this puple, and thou seist, Y schal yyue to hem `mete of fleischis an hool monethe.
22 Kodi ngakhale titapha nkhosa ndi ngʼombe, zingawakwanire? Ngakhale titagwira nsomba zonse za mʼnyanja, kodi zingawakwanire iwowa?”
Whether the multitude of scheep and of oxun schal be slayn, that it may suffice to mete, ethir alle the fischis of the see schulen be gaderid to gidere, that tho fille hem?
23 Yehova anayankha Mose kuti, “Kodi dzanja langa ndi lalifupi? Uwona tsopano ngati zimene ndanenazo zichitike kapena ayi.”
To whom the Lord answeride, Whether the `hond of the Lord is vnmyyti? riyt now thou schalt se, wher my word schal be fillid in werk.
24 Choncho Mose anatuluka nakawuza anthu zomwe Yehova ananena. Anasonkhanitsa pamodzi akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja ndi kuwayimiritsa mozungulira Chihema.
Therfor Moises cam, and telde to the puple the wordis of the Lord; and he gaderide seuenti men of the eldere of Israel, whiche he made stonde aboute the tabernacle.
25 Ndipo Yehova anatsika mʼmitambo ndi kuyankhula naye ndipo anatengako mzimu womwe unali pa Mose ndi kuwuyika pa akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja. Pamene mzimuwo unakhazikika pa akuluakuluwo, anayamba kunenera koma sanapitirize.
And the Lord cam doun bi a cloude, and spak to Moises, and took a weye of the spirit that was in Moises, and yaf to the seuenti men; and whanne the spirit hadde restid in hem, thei profesieden, and ceessiden not `aftirward.
26 Koma anthu ena awiri omwe mayina awo anali Elidadi ndi Medadi, anatsalira mu msasa. Anali nawo mʼgulu la olembedwa aja, koma sanapite nawo ku Chihema. Komabe mzimu unakhala pa iwo ndipo ananenera ali mu msasa.
Forsothe twei men dwelliden stille in the tentis, of whiche men oon was clepid Heldad, and the tothir Medad, on whiche the spirit restide; for also thei weren descryued, and thei yeden not out to the tabernacle.
27 Mnyamata wina anathamanga kudzawuza Mose kuti, “Elidadi ndi Medadi akunenera mu msasa.”
And whanne thei profesieden in the tentis, a child ran, and teld to Moises, and seide, Heldad and Medad profecien in the tentis.
28 Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose kuyambira ubwana wake, anayankha kuti, “Mbuye wanga Mose, aletseni!”
Anoon Josue, the sone of Nun, the `mynystre of Moises, and chosun of manye, seide, My lord Moises, forbede thou hem.
29 Koma Mose anati, “Kodi ukuchita nsanje chifukwa cha ine? Ndikanakonda kuti anthu onse a Yehova akhale aneneri ndi kuti Yehova ayike mzimu wake pa iwo!”
And he seide, What hast thou enuye for me? who yyueth that al the puple profesie, and that God yyue his spirit to hem?
30 Mose ndi akuluakulu a Israeli aja anabwerera ku msasa.
And Moises turnede ayen, and the eldre men in birthe of Israel in to the tentis.
31 Pamenepo Yehova anawutsa mphepo yochokera ku nyanja imene inabweretsa zinziri. Zinzirizo zinagwera pansi kuzungulira msasa, mtunda wa kilomita imodzi mbali zonse ndipo msinkhu wake unali mita imodzi.
Forsothe a wynde yede forth fro the Lord, and took curlewis, and bar ouer the see, and lefte in to the tentis, in the iurney, as myche as mai be parformed in o day, bi ech part of the tentis bi cumpas; and tho flowen in the eir bi twei cubitis in `hiynesse ouer the erthe.
32 Tsiku limenelo masana onse mpaka usiku ndiponso tsiku lotsatiralo, anthu anatuluka kunja kukatola zinziri. Palibe amene anasonkhanitsa zochepera makilogalamu 1,000 ndipo anaziyanika kuzungulira msasa wonse.
Therfor the puple roos in al that dai and nyyt and in to the tothir dai, and gaderide the multitude of curlewis; he that gaderide litil, gaderide ten `mesuris clepid chorus; `and o chorus conteyneth ten buschels; and thei drieden tho curlewis bi the cumpas of the tentis.
33 Koma pamene anthuwo ankadya nyamayo, asanayimeze nʼkomwe, ukali wa Yehova unafika pa iwo ndipo Iye anawakantha ndi mliri woopsa.
Yit `fleischis weren in the teeth `of hem, and siche mete failide not; and lo! the woodnesse of the Lord was reisid ayens the puple, and smoot it with a ful greet veniaunce.
34 Nʼchifukwa chake malowo anawatcha Kibiroti Hatava chifukwa pamenepo anakwirirapo anthu osusuka aja.
And thilke place was clepid The sepulcris of coueitise, for there thei birieden the puple that desiride fleischis.
35 Kuchoka pa Kibiroti Hatava anthuwo anayenda kupita ku Heziroti ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi.
Sotheli thei yeden `out of the sepulcris of coueitise, and camen in to Asseroth, and dwelliden there.

< Numeri 11 >