< Nehemiya 8 >

1 Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
Tada se skupi sav narod jednodušno na ulicu koja je pred vratima vodenijem, i rekoše Jezdri književniku da donese knjigu zakona Mojsijeva koji dade Gospod Izrailju.
2 Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
I donese Jezdra sveštenik zakon pred zbor, u kom bjehu ljudi i žene i svi koji mogahu razumjeti, prvoga dana sedmoga mjeseca.
3 Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
I èita je na ulici koja je pred vratima vodenijem od jutra do podne pred ljudima i ženama i onijem koji mogahu razumjeti, i uši svemu narodu bijahu obraæene ka knjizi zakonskoj.
4 Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
A Jezdra književnik stajaše na mjestu povisoku, koje bjehu naèinili od drveta za to; i do njega stajaše Matatija i Sema i Anaja i Urija i Helkija i Masija s desne strane, a s lijeve Fedaja i Misailo i Malhija i Asum i Asvadana, Zaharija i Mesulam.
5 Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
I otvori Jezdra knjigu na vidiku svemu narodu, jer bijaše više svega naroda, i kad je otvori, usta sav narod.
6 Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
I Jezdra blagoslovi Gospoda Boga velikoga, a sav narod odgovori: amin, amin, podigavši ruke svoje, pa se saviše i pokloniše se Gospodu licem do zemlje.
7 Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
A Isus i Vanije i Serevija, Jamin, Akuv, Savetaj, Odija, Masija, Kelita, Azarija, Jozavad, Anan, Felaja i drugi Leviti pouèavahu narod zakonu, i narod stajaše na mjestu.
8 Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
I èitahu knjigu, zakon Božji, razgovijetno, i razlagahu smisao, te se razumijevaše što se èitaše.
9 Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
Potom Nemija, koji je Tirsata, i sveštenik Jezdra književnik i Leviti koji pouèavahu narod, rekoše svemu narodu: ovaj je dan svet Gospodu Bogu vašemu; ne tužite ni plaèite. Jer plakaše sav narod slušajuæi što govori zakon.
10 Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
I reèe im: idite i jedite pretilo i pijte slatko i šaljite dijelove onima koji nemaju ništa zgotovljeno, jer je ovaj dan svet Gospodu našemu. Zato ne budite žalosni, jer je radost Gospodnja vaša sila.
11 Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
I Leviti utišaše narod govoreæi: muèite, jer je ovaj dan svet, i ne budite žalosni.
12 Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
I otide sav narod da jede i pije i da šalje dijelove, i veseliše se veoma što razumješe rijeèi koje im se kazaše.
13 Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
A sjutradan skupiše se glavari domova otaèkih iz svega naroda, sveštenici i Leviti, k Jezdri književniku da uèe što zakon govori.
14 Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
I naðoše napisano u zakonu da je Gospod zapovjedio preko Mojsija da sinovi Izrailjevi borave u sjenicama na praznik sedmoga mjeseca.
15 Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
I objaviše i proglasiše po svijem gradovima svojim i u Jerusalimu govoreæi: idite u goru, i donesite granja maslinova i granja od divlje masline i granja mirtova i palmova i granja od šumnatijeh drveta, da naèinite sjenice, kako je napisano.
16 Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
I narod izide i donese i naèini sjenice svaki na svom krovu i u svom trijemu i u trijemovima doma Božijega i na ulici kod vrata vodenijeh i na ulici kod vrata Jefremovijeh.
17 Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
I tako naèini sjenice sav zbor, što se bješe vratio iz ropstva, i boravljahu pod sjenicama. A od vremena Isusa sina Navina do toga dana ne èiniše tako sinovi Izrailjevi. I bi veselje veoma veliko.
18 Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.
I èitaše se knjiga zakona Božijega svaki dan, od prvoga dana do pošljednjega; i praznovaše praznik sedam dana, a osmi dan bi sabor, kako je ureðeno.

< Nehemiya 8 >