< Nehemiya 6 >

1 Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata.
A kad èu Sanavalat i Tovija i Gisem Arapin i ostali naši neprijatelji da sam sazidao zid i da nije ostalo u njemu ništa provaljeno, a do tada još ne bijah namjestio krila na vrata,
2 Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.” Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko.
Posla Sanavalat i Gisem k meni i poruèi: hodi da se sastanemo u kom selu u polju Ononskom. A oni mišljahu zlo po me.
3 Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?”
I poslah k njima glasnike i poruèih: u poslu sam velikom, zato ne mogu doæi. Jer bi stao posao kad bih ga ostavio da doðem k vama.
4 Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.
I slaše tako k meni èetiri puta; i ja im onako odgovorih.
5 Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata.
Tada Sanavalat posla k meni tako peti put slugu svojega s knjigom otvorenom u ruci.
6 Mu kalatamo munali mawu akuti, “Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo.
A u njoj pisaše: èuje se po narodima i Gasmuj kaže da se ti i Judejci mislite odmetnuti, zato zidaš zid, i hoæeš da im budeš car, kako se govori,
7 Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”
I da si postavio proroke da razglašuju za tebe u Jerusalimu i govore: car je u Judeji. A to æe doæi do cara; nego hodi da se dogovorimo.
8 Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”
Tada poslah k njemu i poruèih: nije tako kako ti kažeš; nego si sam izmislio.
9 Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.” Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”
Jer oni svi šæahu nas uplašiti govoreæi: klonuæe ruke njihove od posla i neæe se svršiti. Zato, Bože, ukrijepi ruke moje.
10 Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”
Jošte otidoh u kuæu Semaji sinu Dalaje sina Metaveilova, koji se bješe zatvorio, i reèe mi: da otidemo zajedno u dom Božji usred crkve i da zakljuèamo vrata crkvi, jer æe doæi da te ubiju, doæi æe noæu da te ubiju.
11 Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!”
A ja rekoh: zar æe èovjek kakav sam ja bježati? ili ko bi ovaki kakav sam ja ušao u crkvu da ostane u životu? neæu iæi.
12 Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi.
I razumjeh da ga nije Bog poslao, nego to proroštvo kaza za me, jer ga Tovija i Sanavalat potkupiše.
13 Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.
Zato bješe potkupljen da me uplaši da onako uèinim i zgriješim da bih se osramotio da me mogu ružiti.
14 Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”
Pomeni, Bože moj, Toviju i Sanavalata po ovijem djelima njihovijem, i Noadiju proroèicu i druge proroke koji me šæahu uplašiti.
15 Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52.
I tako dovrši se zid dvadeset petoga dana mjeseca Elula za pedeset i dva dana.
16 Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.
I kad èuše svi neprijatelji naši i vidješe svi narodi koji bijahu oko nas, uplašiše se vrlo, jer poznaše da je Bog naš uèinio to djelo.
17 Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo,
I u one dane mnogi glavari Judejski slahu knjige Toviji, i od Tovije njima dolažahu knjige.
18 pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya.
Jer mnogi Judejci bijahu mu se zakleli; jer bješe zet Sehaniji sinu Arahovu, i Joanan sin njegov bješe oženjen kæerju Mesulama sina Varahijina.
19 Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.
I govorahu preda mnom dobro o njemu, i rijeèi moje dokazivahu mu; i Tovija slaše knjige da me uplaši.

< Nehemiya 6 >