< Nehemiya 13 >

1 Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
U to vrijeme èita se knjiga Mojsijeva narodu, i u njoj se naðe napisano da ne ulazi Amonac ni Moavac u sabor Božji dovijeka;
2 Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
Jer ne sretoše sinova Izrailjevijeh s hljebom i vodom, nego najmiše na njih Valama da ih prokune, ali Bog naš obrati onu kletvu u blagoslov.
3 Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
A kad èuše taj zakon, odluèiše od Izrailja sve tuðince.
4 Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
A prije toga Elijasiv sveštenik, koji bješe nad klijetima doma Boga našega, oprijatelji se s Tovijom,
5 Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
I naèini mu veliku klijet, gdje se prije ostavljahu dari i kad i sudovi i desetak od žita, vina i ulja, odreðeni Levitima i pjevaèima i vratarima, i prinosi za sveštenike.
6 Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
A kad to sve bivaše, ne bjeh u Jerusalimu, jer trideset druge godine Artakserksa cara Vavilonskoga vratih se k caru, i poslije nekoliko godina izmolih se opet u cara.
7 ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
I kad doðoh u Jerusalim, vidjeh zlo što uèini Elijasiv radi Tovije naèinivši mu klijet u trijemu doma Božijega.
8 Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
I bi mi vrlo mrsko, te izbacih sve pokuæstvo Tovijino napolje iz klijeti.
9 Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
I zapovjedih, te oèistiše klijeti; i unesoh u njih opet posuðe doma Božijega, dare i kad.
10 Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
Potom doznah da se Levitima nijesu davali dijelovi, te su se razbjegli svaki na svoju njivu i Leviti i pjevaèi, koji raðahu posao.
11 Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
I ukorih starješine i rekoh: zašto je ostavljen dom Božji? I sabrah ih opet i postavih na njihovo mjesto.
12 Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
I svi Judejci donosiše desetke od žita i vina i ulja u spreme.
13 Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
I postavih nastojnike nad spremama, Selemiju sveštenika i Sadoka književnika, i izmeðu Levita Fedaju, i uz njih Anana sina Zahura sina Matanijina, jer se za vjerne držahu; i bijaše im posao dijeliti braæi svojoj.
14 Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
Pomeni me, Bože moj, za to, i nemoj izbrisati dobara mojih koja uèinih domu Boga svojega i službi njegovoj.
15 Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
U to vrijeme vidjeh u Judeji gdje gaze u kacama u subotu i nose snopove natovarivši na magarce, i vino, grožðe i smokve i svakojake tovare, i nose u Jerusalim u subotu, i prekorih ih onaj dan kad prodavahu žitak.
16 Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
I Tirci koji življahu u Jerusalimu donošahu ribu i svakojaki trg i prodavahu u subotu sinovima Judinijem u Jerusalimu.
17 Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
Zato prekorih glavare Judejske i rekoh im: kako je to zlo što èinite te skvrnite subotu?
18 Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
Nijesu li tako èinili oci vaši, te Bog naš pusti na nas i na ovaj grad sve ovo zlo? I vi još umnožavate gnjev na Izrailja skvrneæi subotu.
19 Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
I kad doðe sjen na vrata Jerusalimska uoèi subote, zapovjedih te zatvoriše vrata, i zapovjedih da ih ne otvoraju do poslije subote; i postavih nekoliko svojih momaka na vratima da se ne unosi nikakav tovar u subotu.
20 Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
I prenoæiše trgovci i koji prodavahu svakojaki trg iza Jerusalima jednom i drugom.
21 Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
I opomenuh ih i rekoh im: zašto noæujete oko zida? Ako još jednom to uèinite, uložiæu na vas. Od tada ne dolaziše u subotu.
22 Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
A Levitima zapovjedih da se oèiste i da doðu i èuvaju vrata da bude svet dan subotni. I za ovo pomeni me, Bože moj, i oprosti mi po velikoj milosti svojoj.
23 Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
Još vidjeh u to vrijeme Judejce koji se bijahu oženili Azoæankama, Amonkama i Moavkama.
24 Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
I sinovi njihovi govorahu pola Azotski, i ne umijahu govoriti Judejski nego jezikom i jednoga i drugoga naroda.
25 Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
Zato ih karah i psovah, i neke izmeðu njih bih i èupah, i zakleh ih Bogom da ne daju kæeri svojih sinovima njihovijem niti da uzimaju kæeri njihovijeh za sinove svoje ili za sebe.
26 Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
Nije li tijem zgriješio Solomun car Izrailjev, ako i ne bješe u mnogim narodima cara njemu ravna i mio bješe Bogu svojemu i Bog ga bješe postavio carem nad svijem Izrailjem? pa opet ga navratiše na grijeh žene tuðinke.
27 Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
A vama li æemo dopustiti da èinite to sve veliko zlo i griješite Bogu našemu uzimajuæi žene tuðinke?
28 Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
I od sinova Jojade sina Elijasiva poglavara sveštenièkoga jedan bješe zet Sanavalatu Oronjaninu, kojega otjerah od sebe.
29 Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
Pomeni ih, Bože moj, što oskvrniše sveštenstvo i zavjet sveštenièki i Levitski.
30 Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
I tako ih oèistih od svijeh tuðinaca, i opet postavih redove sveštenièke i Levitske, svakoga na posao njegov,
31 Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.
I da se donose drva za žrtve na rokove, i prvine. Pomeni me, Bože moj, na dobro.

< Nehemiya 13 >