< Estere 1 >

1 Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi.
U vrijeme Asvirovo, a taj Asvir carovaše od Indije do Etiopije u sto i dvadeset i sedam zemalja,
2 Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa,
U to vrijeme, kad sjeðaše car Asvir na prijestolu carstva svojega u Susanu carskom gradu,
3 ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.
Treæe godine carovanja svojega uèini gozbu svijem knezovima svojim i slugama svojim, te bijaše kod njega sila Persijska i Midska, vlastelji i upravitelji zemaljski;
4 Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake.
I on pokazivaše bogatstvo i slavu carstva svojega i diku i krasotu velièine svoje mnogo dana, sto i osamdeset dana.
5 Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu.
I poslije tih dana uèini car svemu narodu što ga bijaše u Susanu carskom gradu od maloga do velikoga gozbu za sedam dana u trijemu u vrtu od carskoga dvora.
6 Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira.
Zavjesi bijeli, zeleni i ljubièasti bijahu obješeni vrvcama bijelijem, lanenijem i skerletnijem o bioèuzima srebrnijem na stupovima mramornijem; odri bijahu zlatni i srebrni po podu od zelenoga, bijeloga, žutoga i crvenoga mramora.
7 Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu.
A piæe davahu u sudovima zlatnijem, i to u sudovima drugim i drugim, a vina carskoga bješe izobila, kako može biti u cara.
8 Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.
I piæem niko ne navaljivaše po naredbi, jer car bješe zapovjedio svijem pristavima doma svojega da èine kako ko hoæe.
9 Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.
I carica Astina uèini gozbu ženama u carskom dvoru cara Asvira.
10 Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi
Sedmi dan kad se car razveseli od vina reèe Meumanu, Visati, Arvoni, Vikti, Avakti, Zetaru i Harkasu, sedmorici dvorana koji dvorahu pred carem Asvirom,
11 kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri.
Da dovedu caricu Astinu pred cara pod carskim vijencem, da pokaže narodima i knezovima ljepotu njezinu, jer bijaše lijepa.
12 Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.
Ali carica Astina ne htje doæi na rijeè carevu, koju joj poruèi po dvoranima; zato se car vrlo razgnjevi i gnjev se njegov raspali u njemu.
13 Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama.
I reèe car mudarcima koji razumijevahu vremena jer tako car iznošaše stvari pred sve koji razumijevahu zakon i pravdu,
14 Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.
A najbliži do njega bijahu Karsena, Setar, Admata, Tarsis, Meres, Marsena i Memukan, sedam knezova Persijskih i Midskih, koji gledahu lice carevo i sjeðahu na prvijem mjestima u carstvu):
15 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”
Što treba po zakonu èiniti s caricom Astinom što nije uèinila što je zapovjedio car Asvir preko dvorana?
16 Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero.
Tada reèe Memukan pred carem i knezovima: nije samo caru skrivila carica Astina nego i svijem knezovima i svijem narodima po svijem zemljama cara Asvira.
17 Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’
Jer æe se djelo carièino raziæi meðu sve žene, pa æe prezirati muževe svoje govoreæi: car Asvir zapovjedi da dovedu preda nj caricu Astinu, a ona ne doðe.
18 Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”
I od danas æe kneginje Persijske i Midske koje èuju šta je uèinila carica tako govoriti svijem knezovima carevijem; te æe biti mnogo prkosa i svaðe.
19 “Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye.
Ako je ugodno caru, da izide carska zapovijest od njega i da se upiše meðu zakone Persijske i Midske da je nepromjenito, da Astina ne izlazi više pred cara Asvira i da æe car dati njezino carstvo drugoj boljoj od nje.
20 Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”
I kad se zapovijest careva koju uèini èuje po carstvu njegovu svemu kolikome, sve æe žene poštovati svoje muževe od velikoga do maloga.
21 Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani.
I ovo bi po volji caru i knezovima, i uèini car kako reèe Memukan.
22 Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.
I razasla knjige po svijem zemljama carskim, u svaku zemlju njezinijem pismom i svakomu narodu njegovijem jezikom, da bi svaki muž bio gospodar u svojoj kuæi; i bi proglašeno jezikom svakoga naroda.

< Estere 1 >