< Luka 4 >

1 Yesu, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anachoka ku mtsinje wa Yorodani ndipo anatsogozedwa ndi Mzimu Woyerayo kupita ku chipululu,
Jésus, rempli du Saint-Esprit, revint du Jourdain, et fut poussé par un mouvement de l'Esprit au désert:
2 kumene anayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anayi. Sanadye kena kalikonse pa masiku amenewo, ndipo pa mapeto pake anamva njala.
il y fut tenté par le diable pendant quarante jours. Il ne mangea rien dans ces jours-là, et, quand ils furent passés, il eut faim.
3 Mdierekezi anati kwa Iye, “Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza mwala uwu kuti usanduke buledi.”
Le diable lui dit: «Si tu es Fils de Dieu, commande à cette pierre de se changer en pain.»
4 Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha.’”
Jésus lui répondit: «Il est écrit que l'homme ne vivra pas de pain seulement.»
5 Mdierekezi anamutengera Iye pamalo aatali ndipo mʼkamphindi namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi.
Le diable l'ayant emmené, lui fit voir en un instant tous les royaumes de la terre,
6 Ndipo anati kwa Iye, “Ndidzakupatsani ulamuliro ndi ulemerero wawo; pakuti anandipatsa ine, ndipo ndingathe kupereka kwa aliyense amene ndikufuna.
et lui dit: «Je te donnerai toute cette puissance et la gloire de ces royaumes; car elles m'ont été données, et je les donne à qui je veux.
7 Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”
Si donc tu te prosternes devant moi, elles t'appartiendront tout entières.»
8 Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’”
Jésus lui répondit: «Il est écrit: «Tu adoreras le Seigneur ton Dieu, et tu le serviras lui seul.»
9 Mdierekezi anapita naye ku Yerusalemu namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu dziponyeni nokha pansi kuchokera pano.
Le diable le mena à Jérusalem, le posa à l'extrémité de l'aile du temple, et lui dit: «Si tu es Fils de Dieu, jette toi d'ici en bas;
10 Pakuti kwalembedwa, “Adzalamulira angelo ake za iwe kuti akutchinjirize mosamala;
car il est écrit qu'il ordonnera à ses anges de te garder,
11 ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.”
et qu'ils te porteront sur leurs bras, de peur que ton pied ne heurte contre une pierre.»
12 Yesu anayankha kuti, “Mawu akuti, ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’”
Jésus lui répliqua qu'il est dit: «Tu ne tenteras point le Seigneur ton Dieu.»
13 Mdierekezi atamaliza mayesero awa onse, anamusiya Iye kufikira atapeza mpata wina.
Et le diable ayant épuisé toute espèce de tentation, s'éloigna de lui jusqu’à nouvelle occasion.
14 Yesu anabwerera ku Galileya mu mphamvu ya Mzimu Woyera, ndipo mbiri yake inafalikira ku madera onse a ku midzi.
Jésus, animé de la puissance de l'Esprit, s'en retourna en Galilée, et sa renommée se répandit dans tout le pays d'alentour.
15 Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.
Il enseignait dans les synagogues, et tout le monde le glorifiait.
16 Iye anapita ku Nazareti, kumene anakulira, ndipo pa tsiku la Sabata anakalowa mʼsunagoge, monga mwa chikhalidwe chake. Ndipo anayimirira kuti awerenge malemba.
Il vint à Nazareth, où il avait été élevé, et, suivant sa coutume, il entra le jour du sabbat dans la synagogue, et se leva pour faire la lecture.
17 Anamupatsa buku la mneneri Yesaya. Atalitsekula, anapeza pamalo pamene panalembedwa kuti,
On lui remit le livre du prophète Ésaïe; et, l'ayant ouvert, il trouva l'endroit où il est écrit:
18 “Mzimu wa Ambuye ali pa Ine; chifukwa wandidzoza kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kwa osauka. Wandituma kuti ndilalikire kwa a mʼndende kuti amasulidwe ndi kwa osaona kuti apenyenso, kumasulidwa kwa osautsidwa,
L'Esprit du Seigneur est sur moi, parce qu'il m'a oint pour annoncer l'évangile aux pauvres:
19 ndi kulalikira za nthawi imene Ambuye adzakomere mtima anthu awo.”
il m'a envoyé pour annoncer la délivrance aux captifs, et aux aveugles le recouvrement de la vue; pour renvoyer en liberté les opprimés, et pour publier une année favorable du Seigneur.
20 Kenaka Iye anatseka bukulo, nalibwezera kwa wotumikira ndipo anakakhala pansi. Maso a aliyense mʼsunagogemo anali pa Iye,
Puis, il ferma le livre, le rendit au desservant, et s'assit; et tout le monde dans la synagogue avait les yeux fixés sur lui.
21 ndipo anawawuza kuti, “Lero malemba awa akwaniritsidwa mmene mwamveramu.”
Il se mit à leur dire: Aujourd'hui est accomplie la parole de l'Écriture, comme vous venez de l'entendre de vos oreilles.»
22 Onse anayankhula zabwino za Iye ndipo anadabwa ndi mawu ogwira moyo amene anatuluka mʼkamwa mwake. Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu si mwana wa Yosefe?”
Et tous témoignaient en sa faveur; ils étaient étonnés des paroles pleines de grâce qui sortaient de sa bouche, et ils disaient: «N'est-ce pas là le fils de Joseph?»
23 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, mudzandiwuza mwambi uwu: Singʼanga, dzichiritse wekha! Chitanso mʼmudzi wa kwanu kuno zimene ife tamva kuti Iwe unazichita ku Kaperenawo.”
Alors il leur dit: «Sans doute, vous m'alléguerez le proverbe: «Médecin, guéris-toi toi-même, » et vous me direz, fais également ici, dans ta patrie, tout ce que nous avons appris que tu as fait pour Capernaoum.»
24 Iye anapitiriza kuti, “Zoonadi, ndikukuwuzani kuti palibe mneneri amene amavomerezedwa ku mudzi kwawo.
Mais il ajouta: «En vérité, je vous dis qu'aucun prophète n'est bien venu dans son pays.
25 Ine ndikukutsimikizirani kunali amayi ambiri amasiye mu Israeli mʼnthawi ya Eliya, kumwamba kutatsekedwa kwa zaka zitatu ndi theka ndipo kunali njala yayikulu mʼdziko lonselo.
Vraiment, je vous le dis, il y avait beaucoup de veuves en Israël au temps d'Élie, quand le ciel fut fermé durant trois ans et demi, et qu'il y eut une grande famine sur toute la terre,
26 Komabe Eliya sanatumidwe kwa mmodzi mwa iwo, koma kwa mkazi wamasiye wa ku Zerefati ku chigawo cha Sidoni.
et pourtant Élie ne fut envoyé à aucune d'elles, mais à une veuve de Sarepta, dans le pays de Sidon.
27 Ndipo kunali akhate ambiri ku Israeli mʼnthawi ya mneneri Elisa, koma panalibe mmodzi mwa iwo anachiritsidwa kupatula Naamani wa ku Siriya.”
Il y avait de même beaucoup de lépreux en Israël au temps du prophète Élysée, et pourtant aucun d'eux ne fut guéri, mais Naaman le Syrien fut seul guéri.»
28 Anthu onse mʼsunagogemo anapsa mtima atamva izi.
Ces paroles remplirent de colère tous ceux qui étaient dans la synagogue;
29 Anayimirira namutulutsira kunja kwa mzindawo, ndipo anamutengera pamwamba pa phiri pamene mzindawo unamangidwapo, ndi cholinga chakuti amuponyere ku phompho.
ils se levèrent, entraînèrent Jésus hors de la ville, et l'emmenèrent jusqu'à un escarpement de la montagne sur laquelle leur ville était bâtie, pour le précipiter en bas;
30 Koma Iye anangoyenda pakati pa gulu la anthulo nachokapo.
mais il passa au milieu d'eux, et s'en alla.
31 Kenaka Iye anapita ku Kaperenawo, mudzi wa ku Galileya, ndipo pa Sabata anayamba kuphunzitsa anthu.
Il descendit à Capernaoum, ville de Galilée, et là il enseignait les habitants les jours de sabbat;
32 Iwo anadabwa ndi chiphunzitso chake chifukwa uthenga wake unali ndi ulamuliro.
et ils étaient frappés de son enseignement, parce que sa parole était pleine d'autorité.
33 Mʼsunagogemo munali munthu wogwidwa ndi mzimu woyipa. Iye analira ndi mawu akulu, akuti
Il y avait dans la synagogue un homme possédé d'un esprit, d'un démon impur; il poussa un grand cri, et dit
34 “Aa! Kodi mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
«Ah! Qu'y a-t-il entre nous et toi, Jésus de Nazareth? Tu es venu nous faire périr; je te connais, tu es le Saint de Dieu.»
35 Yesu anachidzudzula kwambiri nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye.” Chiwandacho chinamugwetsa munthuyo pansi pamaso pa onse ndipo chinatuluka wosamupweteka.
Jésus le tança: «Tais-toi, lui dit-il, et sors de cet homme.» Et le démon, ayant jeté cet homme par terre, au milieu de la synagogue, sortit de lui, sans lui avoir fait aucun mal.
36 Anthu onse anadabwa ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi chiphunzitso ichi ndi chotani? Ndi ulamuliro ndi mphamvu Iye akulamulira mizimu yoyipa ndipo ikutuluka!”
Tous les assistants étaient dans la stupéfaction, et ils se disaient les uns aux autres: «Quelle parole est la sienne? Il commande avec autorité et puissance aux esprits impurs, et ils sortent!»
37 Ndipo mbiri yake inafalikira madera onse ozungulira.
Et il n'était bruit que de Jésus dans tous les lieux d'alentour.
38 Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize.
Étant sorti de la synagogue, il entra dans la maison de Simon. Or la belle-mère de Simon avait une grosse fièvre, et l'on pria Jésus de la guérir.
39 Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.
Il se pencha sur elle, tança la fièvre, et la fièvre la quitta. A l'instant cette femme se leva et se mit à les servir.
40 Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa.
Quand le soleil fut couché, tous ceux qui avaient des malades atteints de divers maux, les lui amenèrent; et il les guérit en imposant les mains à chacun d'eux.
41 Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.
Des démons aussi sortaient de plusieurs malades, en criant: «Tu es le Fils de Dieu, » et Jésus les tançait pour leur imposer silence, parce qu'ils savaient qu'il était le Messie.
42 Kutacha, Yesu anapita ku malo a yekha. Anthu ankamufunafuna Iye ndipo pamene anafika kumene anali, anthuwo anayesetsa kumuletsa kuti asawachokere.
Quand le jour parut, il sortit et s'en alla dans un lieu désert. Une foule de gens vinrent le chercher jusqu'au lieu où il était, et ils le retenaient pour qu'il ne s'éloignât pas d'eux.
43 Koma Iye anati, “Ine ndikuyenera kulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ku mizinda inanso chifukwa ichi ndi chimene ananditumira.”
Mais il leur dit: «Il faut que je porte aussi à d'autres villes la bonne nouvelle du royaume de Dieu; car c'est dans ce but que j'ai été envoyé.»
44 Ndipo Iye anapitirirabe kulalikira mʼmasunagoge a ku Yudeya.
Et il prêchait dans les synagogues de la Galilée.

< Luka 4 >