< Luka 3 >

1 Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
La quinzième année du règne de Tibère César, lorsque Ponce Pilate était gouverneur de Judée, qu'Hérode était tétrarque de la Galilée, et Philippe, son frère, tétrarque de l'Iturie et delà Trachonite, et que Lysanias était tétrarque de l'Abilène,
2 Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
du temps du souverain sacrificateur Anne, et de Caïphe, la parole de Dieu fut adressée dans le désert à Jean, fils de Zacharie.
3 Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
Il vint dans toute la contrée qui avoisine le Jourdain, prêchant le baptême de la repentance pour le pardon des péchés,
4 Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
ainsi qu'il est écrit dans le livre des discours d'Esaïe, le prophète: «C'est une voix qui crie au désert: «Préparez le chemin du Seigneur, faites-lui des sentiers droits:
5 Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
toute vallée, sera comblée, toute montagne et toute colline seront abaissées; ce qui est tortu sera redressé, et les chemins raboteux seront aplanis:
6 Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
et toute chair verra le salut de Dieu.»
7 Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
Jean disait donc aux foules qui venaient se faire baptiser par lui: «Race de vipères, qui vous a appris à fuir la colère à venir?
8 Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
Produisez donc des fruits dignes de la repentance, et ne vous mettez pas à dire en vous-mêmes: «Nous avons pour père Abraham; » car je vous dis que de ces pierres, Dieu peut susciter des enfants à Abraham.
9 Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
Déjà même la cognée est mise à la racine des arbres; tout arbre donc qui ne produit pas de bon fruit, va être coupé et jeté au feu.»
10 Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
Et le peuple lui demanda: «Que faut-il donc faire?»
11 Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
Il leur répondit: «Que celui qui a deux tuniques partage avec celui qui n'en a point; et que celui qui a de quoi manger fasse de même.»
12 Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
Des publicains vinrent aussi se faire baptiser, et lui dirent: «Maître, que devons-nous faire?»
13 Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
Il leur dit: «N'exigez rien au delà de ce qui vous est commandé.»
14 Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
Des militaires l'interrogèrent aussi: «Et nous, que devons-nous faire?» Il leur dit: «Ne commettez point d'extorsions, et ne faites de chicanes à personne; contentez- vous de votre paie.»
15 Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
Comme le peuple était dans l'attente, et que chacun se demandait au dedans de soi, si Jean ne serait point le Messie,
16 Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
Jean, s'adressant à tous, leur dit: «Pour moi, je vous baptise d'eau; mais il vient, celui qui est plus puissant que moi, et je ne suis pas digne de délier la courroie de ses sandales: c'est lui qui vous baptisera d'esprit saint et de feu.
17 Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
Il a son van à la main, et il nettoiera son aire; il amassera le blé dans son grenier, mais il brûlera la paille dans un feu qui ne s'éteint point.»
18 Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
Il annonçait donc la bonne nouvelle au peuple, tout en lui adressant beaucoup d'autres exhortations.
19 Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
Mais Hérode, le tétrarque, qu'il reprit au sujet d'Hérodiade, femme de son frère, et de toutes les mauvaises actions que lui, Hérode, avait commises,
20 Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
ajouta à tous ses crimes celui de faire jeter Jean en prison.
21 Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
Comme tout le peuple se faisait baptiser, Jésus se fit aussi baptiser; et au moment où il priait, le ciel s'ouvrit;
22 Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
le Saint-Esprit descendit sur lui sous une forme corporelle, comme une colombe; et une voix sortit du ciel, disant: «Tu es mon Fils bien-aimé; c'est en toi que j'ai mis toute mon affection.»
23 Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
Jésus avait environ trente ans, quand il commença son ministère. Il était, à ce que l'on croyait, fils de Joseph, fils d'Héli,
24 mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
fils de Matthat, fils de Lévi, fils de Melchi, fils de Janné, fils de Joseph,
25 mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
fils de Mattathias, fils d'Anios, fils de Nahum, fils d'Hesli, fils de Naggé,
26 mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
fils de Maath, fils de Mattathias, fils de Semeï, fils de Joseph, fils de Juda,
27 mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
fils de Johanna, fils de Rhésa, fils de Zorobabel, fils de Salathiel, fils de Néri,
28 mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
fils de Melchi, fils d'Addi, fils de Cosam, fils d'Elmodain, fils de Her,
29 mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
fils de José; fils d'Eliézer, fils de Jorim, fils de Matthat, fils de Lévi,
30 mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
fils de Syméon, fils de Juda, fils de Joseph, fils de Jônan, fils d'Eliakim,
31 mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
fils de Méléa, fils de Maman, fils de Mattatha, fils de Nathan, fils de David,
32 mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
fils d'Issaï, fils de Jobed, fils de Booz, fils de Salmon, fils de Naasson,
33 mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
fils d'Aminadab, fils d'Admin, fils d'Ami, fils d'Esron, fils de Phares, fils de Juda,
34 mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
fils de Jacob, fils d'Isaac, fils d'Abraham, fils de Tharé, fils de Nachor,
35 mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
fils de Seruch, fils de Ragan, fils de Phalez, fils d'Héber, fils de Sala,
36 mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
fils de Caïnan, fils d'Arpaxad, fils de Sem, fils de Noé, fils de Lamech,
37 mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
fils de Mathusalem, fils d'Hénoch, fils de Jared, fils de Maleèl, fils de Caïnan,
38 mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.
fils d'Enos, fils de Seth, fils d'Adam, fils de Dieu.

< Luka 3 >