< Luka 21 >

1 Yesu atayangʼana, anaona olemera akuyika mphatso zawo mu chosungira ndalama za mʼNyumba ya Mulungu.
Поглянувши ж добачив, як кидали дари свої в скарбону заможні.
2 Iye anaonanso mkazi wamasiye wosauka akuyikamo timakopala tiwiri.
Побачив же й одну вдовицю вбогу, що кидала туди дві лепти.
3 Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mkazi wamasiye wosaukayu wapereka zambiri kuposa ena onsewa.
І рече: Правдиво глаголю вам, що вдовиця вбога ся більш усїх укинула:
4 Anthu onsewa atapa mphatso zawo kuchokera pa zochuluka zimene ali nazo; koma uyu, mwa umphawi wake, wapereka zonse zimene ali nazo.”
всі бо ті з достатку свого кидали у дари Божі, ся ж з недостатку свого увесь прожиток свій, що мала, вкинула.
5 Ena mwa ophunzira ake ankachita ndemanga za mmene Nyumba ya Mulungu anayikongoletsera ndi miyala yokongola ndiponso zinthu zina zomwe anthu anapereka kwa Mulungu. Koma Yesu anati,
І як деякі говорили про церкву, що каміннєм красним та посьвятами украшена, рече:
6 “Koma zimene mukuziona panozi, nthawi idzafika pamene ngakhale mwala umodzi omwe sudzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
Із сього, що бачите, прийдуть днї, в котрі не зоставить ся камінь на камені, щоб не зруйновано.
7 Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, kodi zonsezi zidzachitika liti? Ndipo tidzaonera chiyani kuti zili pafupi kuchitika?”
Питали ж Його, кажучи: Учителю, коли ж се буде? й що за ознака коли се мав стати ся?
8 Iye anayankha kuti, “Chenjerani kuti musanyengedwe. Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati ‘Ine ndine Iye’ ndi kuti ‘Nthawi yayandikira.’ Musadzawatsate iwo.
Він же рече: Гледїть, щоб не була введені; многі бо прийдуть в імя моє, кажучи: Що се я. А час приближив ся; не йдіть же за вами.
9 Mukadzamva zankhondo ndi zipolowe, musadzachite mantha. Zinthu izi ziyenera kuchitika poyamba, koma chimaliziro sichidzafika nthawi yomweyo.”
Яв же почуєте про войни та ворохобнї, не полохайтесь; мусить бо перш се статись; тільки ж не зараз конець.
10 Kenaka anawawuza kuti, “Mtundu wa anthu udzawukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu kuwukira ufumu wina.
Тодї рече їм: Устане нарід на нарід і царство на царство,
11 Kudzakhala zivomerezi zazikulu, njala ndi miliri mʼmalo osiyanasiyana, ndi zinthu zoopsa ndi zizindikiro zamphamvu kuchokera kumwamba.
і трус великий по місцях, і голоднеча, й помір буде, й страхи, й о-внаки з неба великі будуть.
12 “Koma zonsezi zisanachitike, adzakugwirani ndi kukuzunzani. Adzakuperekani ku masunagoge ndi ku ndende, ndipo adzakutengerani pamaso pa mafumu ndi olamulira, ndipo zonsezi zidzachitika chifukwa cha dzina langa.
Та перш того всього наложать на вас руки свої і гонити муть, видаючи в школи й темницї, і водячи перед царі та ігемони задля імя мого.
13 Umenewu udzakhala mwayi wanu ochitira umboni.
І станеть ж воно вам на сьвідкуваннє.
14 Koma tsimikizani mtima kuti musadzade nkhawa za momwe mudzadzitchinjirizire.
Постановіть же в серцях, ваших наперед, не готовитись відказувати:
15 Pakuti Ine ndidzakupatsani mawu ndi nzeru kotero kuti palibe mmodzi wa adani anu adzathe kuwakana kapena kuwatsutsa.
я бо дам вам уста й премудрість, котрій не здолїють противитись, анї встояти усї противники ваші.
16 Inu mudzaperekedwa ndi makolo anu, abale, anansi ndi abwenzi anu ndipo ena mwa inu adzakuphani.
Будете ж видавані й від родителїв, і братів, і родини, й приятелїв; і вбивати муть деяких з вас.
17 Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine.
І будете ненавиджені від усіх задля імя мого.
18 Koma palibe tsitsi limodzi la mʼmutu mwanu lidzawonongeke.
Та й волосина з голови вашої не загине.
19 Mukadzalimbikira ndiye mudzapeze moyo.
У терпінню вашому осягнїть душі ваші.
20 “Mukadzaona Yerusalemu atazingidwa ndi magulu ankhondo, inu mudzadziwe kuti kuwonongeka kwake kuli pafupi.
Як же побачите, що обгорнуто таборами Єрусалим, тоді знайте, що наближило ся спустїннє його.
21 Pamenepo amene ali ku Yudeya adzathawire ku mapiri, amene ali mu mzinda adzatulukemo, ndi amene ali ku midzi asadzalowe mu mzinda.
Тодї, хто в Юдеї, нехай біжять у гори; а хто в середині в йому, нехай виходять; а ті, що по селах, нехай не ввіходять у него.
22 Pakuti iyi ndi nthawi yachilango pokwaniritsa zonse zimene zinalembedwa.
Бо се днї мести, щоб справдилось усе написане.
23 Zidzakhala zoopsa nthawi imenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! Kudzakhala masautso aakulu mʼdziko ndipo anthu onse adzawakwiyira.
Горе ж важким і годуючим у ті днї! буде бо біда велика на землі, і гнів на народі сьому.
24 Iwo adzaphedwa ndi lupanga ndi kutengedwa ukapolo kupita ku mayiko wonse. Yerusalemu adzaponderezedwa ndi anthu a mitundu ina mpaka nthawi ya a mitundu ina itakwaniritsidwa.
І поляжуть від гострого меча, й позаймані будуть у полонь до всіх поган; і топтати муть Єрусалим погане, доки сповнять ся часи поган.
25 “Padzakhala zizindikiro zodabwitsa pa dzuwa, mwezi ndi nyenyezi. Pa dziko lapansi, mitundu ya anthu idzakhala mʼmasautso ndipo idzathedwa nzeru pakumva mkokomo ndi mafunde a mʼnyanja.
І будуть ознаки на сонцї, й місяці, й зорях, а на землї переполох народів у ваколотї; як зареве море та филї.
26 Anthu adzakomoka chifukwa cha mantha, akadzamva za zimene zikubwera pa dziko lapansi, pakuti zinthu zamlengalenga zidzagwedezeka.
І омертвіють люде від страху та дожидання того, що прийде на все-денну: сили бо небесні захитають ся.
27 Nthawi imeneyo adzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
І тодї побачять Сина чоловічого йдучого на хмарі з силою і славою великою.
28 Zinthu izi zikadzayamba kuchitika, mudzayimirire ndi kutukula mitu yanu, chifukwa chipulumutso chanu chayandikira.”
Як же почне се діятись, випростуйтесь і підіймайте голови ваші; бо наближилось викупленнє ваше.
29 Iye anawawuza fanizo ili, “Taonani mtengo wamkuyu ndi mitengo ina yonse.
І сказав приповість їм: Бачте смоківницю і всякі дерева:
30 Ikamatulutsa masamba, mumakhoza kudzionera nokha ndi kudziwa kuti dzinja lili pafupi.
Як розпукутоть ся вже, бачивши самі розумієте, що вже близько лїто.
31 Chimodzimodzinso, mukadzaona zinthu zonsezi, dziwani kuti ufumu wa Mulungu uli pafupi.
Так і ви, коли побачите, як се станеть ся, знайте, що близько царство Боже.
32 “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika.
Істино глаголи вам: Ще не перейде рід сей, доки все станеть ся.
33 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
Небо й земля перейде, слова ж мої не перейдуть.
34 “Samalani, kuti mitima yanu ingalemetsedwe ndi maphwando, kuledzera ndi kudera nkhawa za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingadzakupezeni modzidzimutsa ngati msampha.
Остерегайте ся ж, щоб часом не обтягчились ваші серця прожорством та пянством, та журбою життя сього, й щоб несподівано на вас не настиг день той.
35 Pakuti lidzafika pa onse okhala pa dziko lonse lapansi.
Бо, як сітка, впаде на всіх, що живуть на лицї всієї землі.
36 Khalani tcheru nthawi zonse ndi kupemphera kuti inu mudzathe kuthawa zonse zimene zili pafupi kuchitika, ndi kuti mudzathe kuyima pamaso pa Mwana wa Munthu.”
Пильнуйте, по всяк час молячись, щоб удостоїли ся втекти від того всього, що має статись, і станути перед Сином чоловічим.
37 Tsiku lililonse Yesu amaphunzitsa ku Nyumba ya Mulungu, ndi madzulo ali wonse Iye amachoka kukakhala pa phiri la Olivi usiku wonse.
Навчав же днями в церкві, ночами ж виходячи, пробував на горі, званій Оливною.
38 Ndipo anthu onse amabwera mmamawa kudzamumva Iye ku Nyumba ya Mulungu.
Усї ж люде сходились рано до Него в церкву слухати Його.

< Luka 21 >