< Marko 1 >

1 Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu,
Почин євангелиї Ісуса Христа, Сина Божого,
2 monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya: “Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu,”
як написано в пророків: Ось я посилаю ангела мого перед лицем Твоїм, що приготовить дорогу Твою перед Тобою.
3 “Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
Голос покликуючого в пустинї: Готовте дорогу Господню, простими робіть стежки Його.
4 Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo.
Появивсь Йоан, хрестячи в пустинї, й проповідуючи хрещеннє покаяння на прощеннє гріхів.
5 Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani.
І виходила до него вся сторона Юдейська й Єрусалимцї, й хрестились від него всї в ріці Йордані, сповідаючи гріхи свої.
6 Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo.
Був же Йоан одягнений у верблюжий волос і в пояс шкуряний на поясницї своїй, а їв сарану та дикий мед;
7 Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake.
і проповідував, глаголючи: Гряде потужнїщий над мене слїдом за мною; у Него недостоєн я, нахилившись, розвязати ремінь обувя Його.
8 Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”
Я хрестив вас водою, Він же хрестите ме вас Духом сьвятим.
9 Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
І сталось тими днями: Прийшов Ісус із Назарету Галилейського, й охрестивсь у Йоана в Йордані.
10 Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda.
І, зараз вийшовши з води, побачив небеса, що відчинились, і Дух, як голуб, злинув на Него.
11 Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”
І зійшов голос із небес: Ти єси Син мій любий, що я вподобав: ,
12 Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu,
І зараз Дух випровадив Його в пустиню.
13 ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.
І був там у пустиш днїв сорок, спокушуваний од сатани; й пробував з дикими зьвірми, й ангели служили Йому.
14 Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati,
Як же видано Йоана, прийшов Ісус у Галилею, проповідуючи євангелию царства Божого,
15 “Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”
і глаголючи: Що сповнив ся час, і наближило ся царство Боже. Покайтесь і віруйте в євангелию.
16 Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi.
Ходячи ж понад морем Галилейським, побачив Симона та Андрея, брата його, як вони закидали невід у море; були бо рибалки.
17 Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
І рече до них Ісус: Ійдїть слїдом за мною, то зроблю, що станетесь ловцями людей.
18 Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.
І, зараз покинувши неводи свої, пійшли слїдом за Ним.
19 Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo.
І, відійшовши трохи дальше звідтіля, побачив Якова Зеведеєвого та Йоана, брата його, так само в човні, налагоджуючих неводи.
20 Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.
І зараз покликав Їх; і, покинувши батька свого Зеведея в човні з наймитами, пійшли слїдом за Ним.
21 Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa.
І приходять у Капернаум; і зараз субітнього дня, увійшовши в школу, навчав.
22 Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo.
І дивувались наукою Його, навчав бо їх яко маючий власть, а не як письменники.
23 Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti,
І був у них у школї чоловік з духом нечистим; і закричав,
24 “Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
кажучи: Остав! що нам і Тобі, Ісусе Назарянине? чи прийшов єси погубити нас? Знаю Тебе, хто єси: Сьвятий Божий.
25 Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!”
І погрозив йому Ісус, глаголючи: Мовчи й вийди з него.
26 Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.
І стрепенувши його дух нечистий, і закричавши голосом великим, вийшов з него.
27 Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.”
І полякались усї так, що питали один в одного, говорячи; Що се таке? що се за Наука така нова? що по власти й духам нечистим повелїває, і слухають Його?
28 Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.
І розійшлась чутка про Него зараз по всій околиці Галилейській.
29 Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya.
І зараз, із школи вийшовши, пійшли в господу Симона та Андрея, з Яковом та Йоаном.
30 Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye.
Теща ж Симонова лежала в пропасниці, й зараз кажуть Йому про неї.
31 Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.
І приступивши Він, підвів її, взявши за руку її; й покинула її пропасниця зараз; і послугувала вона їм.
32 Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda.
Як же настав вечір, після заходу сонця, поприносили до Него всїх недужих і біснуватих.
33 Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo,
І ввесь город зібрав ся до дверей.
34 Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.
І сцїлив многих недужих на всякі болестї, і бісів многих вигнав; і не дозволяв говорити бісам, бо вони знали Його.
35 Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera.
І вранцї, ще геть за ночи, вставши, вийшов, і пійшов у пусте місце. й там молив ся.
36 Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye,
І пустились за Ним Симон і ті що з ним.
37 ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”
І, знайшовши Його, кажуть Йому: Що всї шукають Тебе.
38 Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.”
І рече до них: Ходімо в близькі містечка, щоб і там проповідував; на те бо прийшов я.
39 Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.
І проповідував по шкодах їх скрізь по всїй Галилеї, і виганяв біси.
40 Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
І приходить до Него прокажений, і благаючи Його, впавши на коліна перед Ним, каже до Него: Коли хочеш, зможеш мене очистити.
41 Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!”
Ісус же, змилосердившись, простяг руку, доторкнувсь до него, й рече йому: Хочу; очистись.
42 Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.
І, як Він сказав, зараз зникла з него проказа, й очистив ся.
43 Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti,
І, заказавши йому, зараз відослав його,
44 “Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.”
і рече до него: Гледи ж, нікому нічого не кажи, а йди, покажись священникові, і принеси за очищеннє твоє, що повелїв Мойсей на сьвідкуваннє їм.
45 Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.
Він же, вийшовши, почав проповідувати багато, й ширити кругом чутку; так, що Він не міг уже явно ввійти в город, а пробував осторонь у пустих місцях; і приходили до Него звідусюди.

< Marko 1 >